< Masalimo 120 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
Cantique des degrés. Vers l’Eternel j’ai crié dans ma détresse, et il m’a exaucé.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
Seigneur, délivre-moi des lèvres mensongères, de la langue perfide.
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Quel profit te donnera-t-elle, quel avantage, cette langue perfide,
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
pareille aux flèches des guerriers, aiguisées aux charbons ardents des genêts?
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Quel malheur pour moi d’avoir séjourné à Méchec, demeuré près des tentes de Kêdar!
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Trop longtemps mon âme a vécu dans le voisinage de ceux qui haïssent la paix.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
Je suis, moi, tout à la paix, et quand je la proclame, eux ne méditent que guerre.

< Masalimo 120 >