< Masalimo 120 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
Cantique des degrés. À l’Éternel, en ma détresse, j’ai crié; et il m’a répondu.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
Éternel! délivre mon âme de la lèvre menteuse, de la langue qui trompe.
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Que te donnera-t-on, et que t’ajoutera-t-on, langue trompeuse? –
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
Des flèches aiguës d’un homme puissant, et des charbons ardents de genêt.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Malheur à moi de ce que je séjourne en Méshec, de ce que je demeure avec les tentes de Kédar; –
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Que mon âme ait tant demeuré avec ceux qui haïssent la paix!
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
Je veux la paix; mais si j’en parle, ils sont, eux, pour la guerre.