< Masalimo 120 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
song [the] step to(wards) LORD in/on/with distress [to] to/for me to call: call to and to answer me
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
LORD to rescue [emph?] soul: myself my from lips deception from tongue deceit
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
what? to give: give to/for you and what? to add to/for you tongue deceit
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
arrow mighty man to sharpen with coal broom
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
woe! to/for me for to sojourn Meshech to dwell with tent Kedar
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
many to dwell to/for her soul: myself my with to hate peace
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
I peace and for to speak: speak they(masc.) to/for battle