< Masalimo 120 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
“A song of the degrees.” Unto the Lord, when I was in distress, did I call, and he hath answered me.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
O Lord, deliver my soul from lips of falsehood, and from a tongue of deceit.
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
What will [God] give unto thee? or what will he add unto thee, thou tongue of deceit?
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
Sharpened arrows of the mighty, with coals of the broom-bush.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Woe is me, that I sojourn in Meshech, that I dwell in the tents of Kedar!
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Too long for herself hath my soul dwelt with him that hateth peace.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
I am for peace; but when I speak, they are for war.