< Masalimo 120 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
A Song of Ascents. In my distress I called unto the LORD, and He answered me.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
O LORD, deliver my soul from lying lips, from a deceitful tongue.
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
What shall be given unto thee, and what shall be done more unto thee, thou deceitful tongue?
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
Sharp arrows of the mighty, with coals of broom.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Woe is me, that I sojourn with Meshech, that I dwell beside the tents of Kedar!
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
My soul hath full long had her dwelling with him that hateth peace.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
I am all peace; but when I speak, they are for war.