< Masalimo 120 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
In my trouble I cried to the Lord: and he heard me.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
O Lord, deliver my soul from wicked lips, and a deceitful tongue.
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
What shall be given to thee, or what shall be added to thee, to a deceitful tongue.
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
The sharp arrows of the mighty, with coals that lay waste.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Woe is me, that my sojourning is prolonged! I have dwelt with the inhabitants of cedar:
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
My soul hath been long a sojourner.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
With them that hate peace I was peaceable: when I spoke to them they fought against me without cause.

< Masalimo 120 >