< Masalimo 120 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
(Sang til Festrejserne.) Jeg råbte til HERREN i Nød, og han svarede mig.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
HERRE, udfri min Sjæl fra Løgnelæber, fra den falske Tunge!
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Der ramme dig dette og hint, du falske Tunge!
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
Den stærkes Pile er hvæsset ved glødende Gyvel.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Ve mig, at jeg må leve som fremmed i Mesjek, bo iblandt Kedars Telte!
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Min Sjæl har længe nok boet blandt Folk, som hader Fred.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
Jeg vil Fred; men taler jeg, vil de Krig!