< Masalimo 12 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
Przewodnikowi chóru, na Seminit. Psalm Dawida. Ratuj, PANIE, bo [już] nie ma pobożnego, zniknęli wierni spośród synów ludzkich.
2 Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
Wszyscy mówią kłamliwie do bliźniego, mówią schlebiającymi wargami i z obłudnym sercem.
3 Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
Niech PAN wytępi wszystkie wargi schlebiające [i] język mówiący przechwałki.
4 Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
Oni mówią: Swoim językiem zwyciężymy, nasze wargi należą do nas, któż jest naszym panem?
5 “Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
Ze względu na ucisk ubogich [i] jęk nędzarzy teraz powstanę – mówi PAN – zapewnię bezpieczeństwo [temu], na kogo zastawiają sidła.
6 Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
Słowa PANA to słowa czyste jak srebro wypróbowane w ziemnym tyglu, siedmiokrotnie oczyszczone.
7 Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
Ty, PANIE, zachowasz ich, będziesz ich strzegł od tego pokolenia aż na wieki.
8 Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.
Niegodziwi krążą wokoło, gdy najpodlejsi z ludzi zostają wywyższeni.

< Masalimo 12 >