< Masalimo 12 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
Pour le chef musicien; sur une lyre à huit cordes. Un psaume de David. Au secours, Yahvé, car l'homme pieux s'arrête. Car les fidèles disparaissent d'entre les enfants des hommes.
2 Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
Chacun ment à son voisin. Ils parlent avec des lèvres flatteuses, et avec un cœur double.
3 Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
Que Yahvé coupe toutes les lèvres flatteuses, et la langue qui se vante,
4 Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
qui ont dit: « Avec notre langue, nous vaincrons. Nos lèvres sont les nôtres. Qui est le seigneur sur nous? »
5 “Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
« A cause de l'oppression des faibles et des gémissements des nécessiteux, Je vais maintenant me lever, dit Yahvé; « Je le mettrai à l'abri de ceux qui le calomnient. »
6 Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
Les paroles de Yahvé sont des paroles irréprochables, comme l'argent affiné dans un fourneau d'argile, purifié sept fois.
7 Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
Tu les garderas, Yahvé. Tu les préserveras à jamais de cette génération.
8 Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.
Les méchants marchent de tous côtés, quand ce qui est vil est exalté parmi les fils des hommes.

< Masalimo 12 >