< Masalimo 12 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
Help, Adonai; for the godly man ceases. For the faithful fail from among the children of men.
2 Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
Everyone lies to his neighbor. They speak with flattering lips, and with a double heart.
3 Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
May Adonai cut off all flattering lips, and the tongue that boasts,
4 Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
who have said, “With our tongue we will prevail. Our lips are our own. Who is lord over us?”
5 “Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
“Because of the oppression of the weak and because of the groaning of the needy, I will now arise,” says Adonai; “I will set him in yesha' ·salvation· far from those who malign him.”
6 Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
Adonai’s words are flawless words, as silver refined in a clay furnace, purified seven times.
7 Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
You will keep them, Adonai. You will preserve them from this generation forever.
8 Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.
The wicked walk on every side, when what is vile is exalted among the sons of men.

< Masalimo 12 >