< Masalimo 12 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
Til Sangmesteren. Efter den ottende. En Salme af David.
2 Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
HERRE, hjælp, thi de fromme er borte, svundet er Troskab blandt Menneskens Børn;
3 Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
de taler Løgn, den ene til den anden, med svigefulde Læber og tvedelt Hjerte.
4 Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
Hver svigefuld Læbe udrydde HERREN, den Tunge, der taler store Ord,
5 “Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
dem, som siger: »Vor Tunge gør os stærke, vore Læber er med os, hvo er vor Herre?«
6 Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
»For armes Nød og fattiges Suk vil jeg nu staa op«, siger HERREN, »jeg frelser den, som man blæser ad.«
7 Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
HERRENS Ord er rene Ord, det pure, syvfold lutrede Sølv.
8 Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.
HERRE, du vogter os, værner os evigt mod denne Slægt. De gudløse færdes frit overalt, naar Skarn ophøjes blandt Menneskens Børn.