< Masalimo 119 >
1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Salige äro de som utan vank lefva, de som i Herrans lag vandra.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Salige äro de som hans vittnesbörd hålla; de som af allo hjerta söka honom.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Ty de som på hans vägom vandra, de göra intet ondt.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Du hafver budit, att hålla dina befallningar fliteliga.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
O! att mitt lif hölle dina rätter med fullt allvar.
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
När jag skådar uppå all din bud, så kommer jag icke på skam.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Jag tackar dig af rätt hjerta, att du lärer mig dina rättfärdighets rätter.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Dina rätter vill jag hålla; öfvergif mig dock aldrig.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Huru skall en yngling sin väg ostraffeliga gå? När han håller sig efter din ord.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Jag söker dig af allo hjerta; Låt mig icke fela om din bud.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Jag behåller din ord i mitt hjerta, på det jag icke skall synda emot dig.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Lofvad vare du, Herre; lär mig dina rätter.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Jag vill med mina läppar förtälja alla dins muns rätter.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Jag fröjdar mig af dins vittnesbörds väg, såsom af allahanda rikedomar.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Jag talar det du befallt hafver, och ser på dina vägar.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Jag hafver lust till dina rätter, och förgäter icke din ord.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Gör väl med din tjenare, att jag må lefva och hålla din ord.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Öppna mig ögonen, att jag må se under i din lag.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Jag är en gäst på jordene; fördölj icke din bud för mig.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Min själ är all sönderkrossad för trängtans skull, efter dina rätter alltid.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Du näpser de stolta; förbannade äro de som vika ifrå din bud.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Vänd ifrå mig försmädelse och föraktelse; ty jag håller din vittnesbörd.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Sitta ock Förstarna och tala emot mig; men din tjenare talar om dina rätter.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Jag hafver lust till din vittnesbörd; de äro mine rådgifvare.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Min själ ligger i stoft; vederqvick mig efter ditt ord.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Jag förtäljer mina vägar, och du bönhörer mig; lär mig dina rätter.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Undervisa mig dina befallningars väg, så vill jag tala om din under.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Jag grämer mig så att hjertat mig försmäktas; styrk mig efter ditt ord.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Vänd ifrå mig den falska vägen, och unna mig din lag.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Jag hafver utvalt sanningenes väg; dina rätter hafver jag mig föresatt.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Jag håller mig intill din vittnesbörd; Herre, låt mig icke på skam komma.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
När du mitt hjerta tröstar, så löper jag dins buds väg.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Lär mig, Herre, dina rätters väg, att jag må bevara dem intill ändan.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Undervisa mig, att jag må bevara din lag, och hålla dem af allo hjerta.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
För mig in på din buds stig, ty jag hafver der lust till.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Böj mitt hjerta till din vittnesbörd, och icke till girighet.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Vänd bort min ögon, att de icke se efter onyttig läro; utan vederqvick mig på dinom väg.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Låt din tjenare hålla din bud stadeliga för din ord, att jag må frukta dig.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Vänd ifrå mig den försmädelse, som jag fruktar; ty dine rätter äro lustige.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Si, jag begärar dina befallningar; vederqvick mig med dine rättfärdighet.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Herre, låt mig vederfaras dina nåd; dina hjelp efter ditt ord;
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Att jag mina lastare svara må; ty jag förlåter mig uppå ditt ord.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Och tag ju icke ifrå minom mun sanningenes ord; ty jag hoppas uppå dina rätter.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Jag vill hålla din lag allstädes, alltid och evinnerliga.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Och jag vandrar i glädje; ty jag söker dina befallningar.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Jag talar om din vittnesbörd inför Konungar, och blyges intet;
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Och hafver lust till din bud, och de äro mig käre;
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Och lyfter mina händer upp till din bud, de mig kär äro; och talar om dina rätter.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Tänk dinom tjenare uppå ditt ord, på hvilket du låter mig hoppas.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Det är min tröst i mitt elände; ty ditt ord vederqvicker mig.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
De stolte hafva deras gabberi af mig; likväl viker jag icke ifrå din lag.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Herre, när jag tänker, huru du af verldenes begynnelse dömt hafver, så varder jag tröstad.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Jag brinner innan, för de ogudaktiges skull, som din lag öfvergifva.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Dine rätter äro min visa i mino huse.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Herre, jag tänker om nattena på ditt Namn, och håller din lag.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Det är min skatt, att jag dina befallningar håller.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Jag hafver sagt, Herre: Det skall mitt arf vara, att jag dina vägar håller.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Jag beder inför ditt ansigte af allo hjerta; var mig nådelig efter ditt ord.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Jag betraktar mina vägar, och vänder mina fötter till din vittnesbörd.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Jag skyndar mig, och dröjer intet, till att hålla din bud.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
De ogudaktigas rote beröfvar mig; men jag förgäter intet din lag.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Om midnatt står jag upp, till att tacka dig för dina rättfärdighets rätter.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Jag håller mig till alla dem som frukta dig, och dina befallningar hålla.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Herre, jorden är full af dine godhet; lär mig dina rätter.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Du gör dinom tjenare godt, Herre, efter ditt ord.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Lär mig goda seder och förståndighet; ty jag tror dinom budom.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Förr än jag späkt vardt, for jag vill; men nu håller jag ditt ord.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Du äst mild och god; lär mig dina rätter.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
De stolte dikta lögn öfver mig; men jag håller dina befallningar af allt hjerta.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Deras hjerta är fett vordet, såsom flott; men jag hafver lust till din lag.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Det är mig ljuft att du hafver späkt mig, att jag må lära dina rätter.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Dins muns lag är mig täckare, än mång tusend stycke guld och silfver.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Din hand hafver gjort och beredt mig; undervisa mig, att jag må lära din bud.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
De som dig frukta, de se mig, och glädja sig; ty jag hoppas uppå din ord.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Herre, jag vet att dina domar äro rätte, och du hafver troliga späkt mig.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Din nåd vare min tröst, såsom du dinom tjenare lofvat hafver.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Låt mig vederfaras dina barmhertighet, att jag må lefva; ty jag hafver lust till din lag.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Ack! att de stolte måtte komma på skam, som mig med lögn nedertrycka; men jag talar om dina befallningar.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Ack! att de måtte hålla sig till mig, som dig frukta, och känna din vittnesbörd.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Mitt hjerta blifve rättsinnigt i dinom rättom, att jag icke på skam kommer.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Min själ trängtar efter dina salighet; jag hoppas uppå ditt ord.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Min ögon trängta efter ditt ord, och säga: När vill du trösta mig?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Ty jag är såsom en lägel i rök; dina rätter förgäter jag icke.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Huru länge skall din tjenare bida? När vill du dom hålla öfver mina förföljare?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
De stolte grafva mig gropar, hvilka intet äro efter din lag.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Dine bud äro alltsamman sanning; de förfölja mig med lögn, hjelp mig.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
De hade fulltnär förgjort mig på jordene; men jag öfvergifver icke dina befallningar.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Vederqvick mig genom dina nåd, att jag må hålla dins muns vittnesbörd.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Herre, ditt ord blifver evinnerliga, så vidt som himmelen är.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Din sanning varar i evighet; du hafver tillredt jordena, och hon blifver ståndandes.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Det blifver dagliga efter ditt ord; ty all ting måste tjena dig.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Om din lag icke hade min tröst varit, så vore jag förgången i mitt elände.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Jag vill aldrig förgäta dina befallningar; ty du vederqvicker mig med dem.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Jag är din, hjelp mig; ty jag söker dina befallningar.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
De ogudaktige vakta uppå mig, att de måga förgöra mig; men jag aktar uppå din vittnesbörd,
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Jag hafver på all ting en ända sett; men ditt bud är varaktigt.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Huru hafver jag din lag så kär; dageliga talar jag derom.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Du gör mig med ditt bud visare, än mina fiender äro; ty det är evinnerliga min skatt.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Jag är lärdare, än alle mine lärare; ty din vittnesbörd äro mitt tal.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Jag är förståndigare, än de gamle; ty jag håller dina befallningar.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Jag förtager minom fotom alla onda vägar, att jag må hålla din ord.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Jag viker icke ifrå dina rätter; ty du lärer mig.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Din ord äro minom mun sötare än hannog.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Ditt ord gör mig förståndigan; derföre hatar jag alla falska vägar.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Ditt ord är mina fötters lykta, och ett ljus på minom vägom.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Jag svär, och vill hållat, att jag dina rättfärdighets rätter hålla vill.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Jag är svårliga plågad; Herre, vederqvick mig efter ditt ord.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Låt dig behaga, Herre, mins muns välviljoga offer, och lär mig dina rätter.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Jag bär mina själ i mina händer alltid, och jag förgäter icke din lag.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
De ogudaktige sätta mig snaror; men jag far icke vill ifrå dina befallningar.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Din vittnesbörd äro mitt eviga arf; ty de äro mins hjertas fröjd.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Jag böjer mitt hjerta till att göra efter dina rätter alltid och evinnerliga.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Jag hatar de ostadiga andar, och älskar din lag.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Du äst mitt beskärm och sköld; jag hoppas uppå ditt ord.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Viker ifrå mig, I onde; jag vill hålla min Guds bud.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Uppehåll mig igenom ditt ord, att jag må lefva; och låt mig icke på skam komma med mitt hopp.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Stärk mig, att jag må blifva salig; så vill jag alltid lust hafva till dina rätter.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Du förtrampar alla dem som villa gå om dina rätter; ty deras bedrägeri är alltsammans lögn.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Du bortkastar alla ogudaktiga på jordene som slagg; derföre älskar jag din vittnesbörd.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Jag fruktar mig för dig, så att mitt kött skälfver; och förskräcker mig for dina rätter.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Jag aktar uppå rätt och rättfärdighet; öfvergif mig icke dem som mig öfvervåld göra vilja.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Beskärma du din tjenare, och tröst honom, att de stolte icke göra mig öfvervåld.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mina ögon trängta efter dina salighet, och efter dine rättfärdighets ord.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Handla med dinom tjenare efter dina nåd; och lär mig dina rätter.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Jag är din tjenare; undervisa mig, att jag må känna din vittnesbörd.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Det är tid, att Herren gör der något till; de hafva omintetgjort din lag.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Derföre älskar jag din bud, öfver guld och öfver fint guld.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Derföre håller jag rätt fram i alla dina befallningar; jag hatar allan falskan väg.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Underliga äro din vittnesbörd, derföre håller dem min själ.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
När ditt ord uppenbaradt varder, så fröjdar det, och gör de enfaldiga visa.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Jag öppnar min mun, och begärar din bud; ty mig längtar efter dem.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Vänd dig till mig, och var mig nådelig, såsom du plägar göra dem som ditt Namn älska.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Låt min gång viss vara i dino orde, och låt ingen orätt öfver mig råda.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Förlös mig ifrå menniskors orätt; så vill jag hålla dina befallningar.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Låt ditt ansigte lysa öfver din tjenare, och lär mig dina rätter.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Mine ögon flyta med vatten, att man icke håller din lag.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Herre, du äst rättfärdig, och rätt är ditt ord.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Du hafver dina rättfärdighets vittnesbörd, och sanningena hårdeliga budit.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Jag hafver när harmats till döds, att mine ovänner hafva din ord förgätit.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Ditt ord är väl bepröfvadt, och din tjenare hafver det kärt.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Jag är ringa och föraktad; men jag förgäter icke dina befallningar.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Din rättfärdighet är en evig rättfärdighet, och din lag är sanning.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Ångest och nöd hafva drabbat uppå mig; men jag hafver lust till din bud.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Dins vittnesbörds rättfärdighet är evig; undervisa mig, så lefver jag.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Jag ropar af allo hjerta, bönhör mig, Herre, att jag må hålla dina rätter.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Jag ropar till dig, hjelp mig, att jag må hålla din vittnesbörd.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Jag kommer bittida, och ropar; uppå ditt ord hoppas jag.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Jag vakar bittida upp, att jag må handla om din ord.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Hör mina röst efter dina nåde: Herre, vederqvick mig efter dina rätter.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Mine arge förföljare vilja till mig, och äro långt ifrå din lag.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Herre, du äst hardt när, och din bud äro alltsamman sanning.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Men jag vet det långt tillförene, att du din vittnesbörd evinnerliga grundat hafver.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Se uppå mitt elände, och fräls mig; hjelp mig ut; förty jag förgäter icke din lag.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Uträtta min sak, och förlossa mig; vederqvick mig igenom ditt ord.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Saligheten är långt ifrå de ogudaktiga; ty de akta intet dina rätter.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Herre, din barmhertighet är stor; vederqvick mig efter dina rätter.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Mine förföljare och ovänner äro månge; men jag viker icke ifrå din vittnesbörd.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Jag ser de föraktare, och det gör mig ondt, att de icke hålla din ord.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Si, jag älskar dina befallningar; Herre, vederqvick mig efter din nåd.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Ditt ord hafver af begynnelsen varit sanning; alle dine rättfärdighets rätter vara evinnerliga.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Förstarna förfölja mig utan sak, och mitt hjerta fruktar sig för din ord.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Jag gläder mig öfver din ord, såsom en den stort byte får.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Lögnene är jag hätsk, och stygges dervid, men din lag hafver jag kär.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Jag lofvar dig sju resor om dagen, för dine rättfärdighets rätters skull.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Stor frid hafva de som din lag älska, och de skola icke stappla.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Herre, jag väntar efter din salighet, och gör efter din bud.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Min själ håller din vittnesbörd, och hafver dem mycket kär.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Jag håller dina befallningar, och dina vittnesbörder; ty alle mine vägar äro för dig.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Herre, låt min klagan för dig komma; undervisa mig efter ditt ord.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Låt mina bön komma för dig; fräls mig efter ditt ord.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Mine läppar skola lofva, när du lärer mig dina rätter.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Min tunga skall tala om ditt ord; ty all din bud äro rätt.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Låt dina hand vara mig biståndiga; ty jag hafver utkorat dina befallningar.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Herre, jag längtar efter din salighet, och hafver lust till din lag.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Låt mina själ lefva, att hon må lofva dig, och dine rätter hjelpa mig.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Jag är såsom ett villfarande och borttappadt får; sök din tjenare, ty jag förgäter icke din bud.