< Masalimo 119 >
1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Wamebarikiwa wale ambao njia zao hazina lawama, waenendao katika sheria ya Yahwe.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Wamebarikiwa wale wazishikao amri zake thabiti, wamtafutao kwa moyo wao wote.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Hawatendi makosa; wanaenenda katika njia zake.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Wewe umetuamuru kuyashika maagizo yako ili tuyachunguze kwa umakini.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Oh, ningependa njia zangu ziwe thabiti nizitii amri zako!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Ndipo sitaaibika nizifikiripo amri zako zote.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Nitakushukuru wewe kwa unyofu wangu wa moyo nijifunzapo amri za haki yako.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Nitazitii amri zako; usiniache peke yangu. BETH.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Ni jinsi gani kijana aweza kuendelea kuishi katika njia yake ya utakatifu? Ni kwa kulitii neno lako.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Kwa moyo wangu wote ninakutafuta wewe; Usiniache nipotee mbali na maagizo yako.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Moyoni mwangu nimeliweka neno lako ili nisije nikakutenda dhambi.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Umetukuka, Yahwe; unifundishe amri zako.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Kwa kinywa changu nimetangaza amri ya haki yako yote ambayo umeifunua.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Ninafurahi katika njia ya amri za agano lako zaidi kuliko katika utajiri.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Nitayatafakari maagizo yako na kuzitilia maanani njia zako.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Ninafurahia katika amri zako; sitalisahau neno lako. GIMEL.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Uwe mwema kwa mtumishi wako ili niweze kuishi na kulishika neno lako.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Ufungue macho yangu ili niweze kuona mambo ya ajabu katika sheria yako.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Mimi ni mgeni katika nchi; usizifiche amri zako mbali nami.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Moyo wangu unauma kwa kutamani sana kuzijua amri zako za haki wakati wote.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Wewe huwakemea wenye kiburi, waliolaaniwa, wanao tanga-tanga mbali na amri zako.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Uniokoe dhidi ya aibu na udhalilishaji, maana nimezitii amri za agano lako.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Ingawa watawala wanapanga njama na kunikashfu, mtumishi wako huzitafakali amri zako.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Amri za agano lako ni furaha yangu, na washauri wangu. DALETH.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Uhai wangu unashikamana na mavumbi! nipe uhai kwa neno lako.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Nilikuambia mapito yangu, na ulinijibu; nifundishe sheria zako.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Unifahamishe njia ya maagizo yako, ili niweze kutafakari juu ya mafundisho yako ya ajabu.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Nimelemewa na huzuni! Nitie nguvu kwa neno lako.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Uiondoe kwangu njia ya udanganyifu; kwa wema wako unifundishe sheria yako.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Nimechagua njia ya uaminifu; siku zote nimeweka amri za haki yako mbele yangu.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Ninashikamana na amri za agano lako; Yahwe, usiniache niaibike.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Nitakimbia katika njia ya amri zako, kwa sababu wausukuma moyo wangu kufanya hivyo. HE
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Unifundishe, Yahwe, njia za sheria yako, nami nitazishika hadi mwisho.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Unipe uelewa, nami nitazishika sheria zako; nitazitii kwa moyo wangu wote.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Uniongoze katika njia ya amri zako, maana ninafurahi kuenenda katika hizo.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Uelekeze moyo wangu kuzielekea amari za agano lako na uniweke mbali na matendo yasiyo haki tena.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Uyageuze macho yangu dhidi ya kutazama mambo yasiyofaa; unihuishe katika njia zako.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Umtendee mtumishi wako ahadi ambayo uliifanya kwa wale wanaokuheshimu wewe.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Uniondolee shutumu niiogopayo, maana hukumu zako za haki ni njema.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Tazama, nimeyatamani maagizo yako; unihuishe katika haki yako. VAV.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Ee Yahwe, unipe upendo wako usiokwisha na wokovu wako kulingana na ahadi yako;
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
ndipo nitakuwa na jibu kwa ajili ya yule anayenidhihaki.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Usiliondoe neno la kweli mdomoni mwangu, maana nimesubiri kwa ajili ya amri zako za haki.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Nitazitii sheria zako siku zote, milele na milele.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Nitaenenda salama, maana ninayatafuta maagizo yako.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Nitazinena amri zako thabiti mbele ya wafalme nami sitaaibika.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Ninafurahia katika amri zako, nizipendazo sana.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Nitaziinulia mikono yangu amri zako, nizipendazo; nitazitafakari sheria zako. ZAYIN.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Kumbuka ahadi yako kwa mtumishi wako kwa sababu umenipa tumaini.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Hii ni faraja yangu katika mateso: kuwa ahadi yako imeniweka hai.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Wenye kiburi wamenicheka, lakini sijaiacha sheria yako.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Nimezitafakari amri zako za haki tangu zamani, Yahwe, nami ninajifariji mwenyewe.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Hasira kali imenishikilia kwa sababu ya waovu wanaoikataa sheria yako.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Sheria zako zimekuwa nyimbo zangu katika nyumba ninayoishi kwa muda.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Ninalifikiria jina lako wakati wa usiku, Yahwe, na kuzishika sheria zako.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Hili limekuwa zoezi langu kwa sababu nimeyatii maagizo yako. HETH.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Yahwe ni sehemu yangu; nimeamua kuyatii maneno yake.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Kwa bidii ninaomba neema yako kwa moyo wangu wote; unihurumie, kama neno lako lilivyo ahidi.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Nilizichunguza njia zangu na kugeuzia miguu yangu kwenye amri za agano lako.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Naharakisha na sichelewi kuzishika amri zako.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Kamba za waovu zimenifunga; nami sijaisahau sheria yako.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Katikati ya usiku ninaamka kukushukuru wewe kwa sababu ya amri za haki yako.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Ninaurafiki na wale wanao kuabudu wewe, wale wote watiio maagizo yako.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Yahwe, nchi, imejaa uaminifu wa agano lako; unifundishe sheria zako. TETH.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Wewe umemtendea mema mtumishi wako, Yahwe, sawasawa na neno lako.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Unifundishe utambuzi sahihi na uelewa, kwa kuwa nimeamini katika amri zako.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Kabla sijateswa nilipotea, lakini sasa nimelitii neno lako.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Wewe ni mwema, na ndiye yule utendaye mema; unifundishe sheria zako.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Wenye kiburi wamenichafua kwa uongo, lakini niliyashika maagizo yako kwa moyo wangu wote.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Mioyo yao ni migumu, lakini ninafurahia katika sheria yako.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Ni vizuri kwangu kuwa nimeteseka ili niweze kujifunza sheria zako.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Maagizo yatokayo kinywani mwako ni ya thamani zaidi kwangu kuliko maelfu ya vipande vya dhahabu na fedha. YOD.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Mikono yako imeniumba na kunitengeneza; unipe uelewa ili niweze kujifunza amri zako.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Wale wanao kucha wewe watafurahi wanionapo kwa sababu ninapata tumaini katika neno lako.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Ninajua, Yahwe, kuwa amri zako ni za haki, na kuwa katika uaminifu ulinitesa.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Agano lako aminifu na linifariji, kama ulivyomwahidi mtumishi wako.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Unihurumie ili niweze kuishi, kwa maana sheria yako ni furaha yangu.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Wenye kiburi na waaibishwe, maana wamenitukana; bali mimi nitayatafakari maagizo yako.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Wale wote wanao kucha wewe na wanigeukie, wale wazijuao amri za agano lako.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Moyo wangu uwe mkamilifu pamoja na heshima kwa sheria zako ili nisiaibike. KAPH.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Ninazimia kwa kutamani sana kuwa wewe unaweza kuniokoa! Ninamatumaini katika neno lako.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Macho yangu yanatamani sana kuiona ahadi yako; ni lini utanifariji mimi?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Kwa maana nimekuwa kama kiriba katika moshi; sisahau sheria zako.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Ni kwa muda gani gani mtumishi wako atalazimika kuyavumilia haya; ni lini utawahukumu wale wanaonitesa?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Wenye kiburi wamenichimbia shimo, wasiotii sheria yako.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Amri zako zote ni za kuaminika; wale watu walinitesa bila ya haki; unisaidie.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
karibu kunifanya nifikie mwisho juu ya nchi hii, lakini siyakatai maagizo yako.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Kwa upendo wako thabiti, uniweke hai, ili niweze kuzitii amri zako. LAMEDH.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Yahwe, neno lako linasimama milele; neno lako limefanywa imara mbinguni.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Uaminifu wako wadumu kwa ajili ya vizazi vyote; umeiimarisha nchi, nayo inadumu.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Vitu yote yaliendelea mpaka leo hii, kama vile ulivyosema katika amri zako za haki, maana vitu vyote ni watumishi wako.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Kama sheria yako isingekuwa furaha yangu, ningeangamia katika mateso yangu.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Sitayasahau kamwe maagizo yako, maana kupitia hayo umeniweka hai.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Mimi ni wako, kwa maana ninayatafuta maagizo yao.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Waovu hujiandaa kuniangamiza, lakini nitatafuta kuzielewa amri za agano lako.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Nimeona kuwa kila kitu kina mipaka, lakini amri zako ni pana, zaidi ya mipaka. MEM.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Oh ni jinsi gani naipenda sheria yako! Ni tafakari yangu mchana kutwa.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Amri zako hunifanya mwenye hekima kuliko adui zangu, maana amri zako siku zote ziko pamoja nami.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Ninauelewa zaidi kuliko walimu wangu wote, kwa maana ninazitafakari amri za agano lako.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Ninaelewa kuliko wale wanaonizidi umri; hii ni kwa sababu nimeyashika maagizo yako.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Nimeiepusha miguu yangu na kila njia ya uovu ili niweze kulitii neno lako.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Sijaenda kinyume na amri zako za haki, kwa maana wewe umenifundisha.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Ni jinsi gani maneno yako ni matamu kwenye majaribu yangu, naam, matamu kuliko asali kinywani mwangu!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Kupitia maagizo yako ninapata utambuzi; kwa hiyo kila njia isiyo ya kweli.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Neno lako ni taa ya mguu miguu yangu na mwanga wa njia yangu.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Nimeapa na nimethibitisha, kuwa nitazitii amri za haki yako.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Nimeteswa sana; uniweke hai, Yahwe, kama ulivyoahidi katika neno lako.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Yahwe, tafadhali pokea dhabihu yangu ya hiari ya kinywa changu, na unifundishe amri zako za haki.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Uhai wangu ziku zote uko mkononi mwangu, lakini bado sisahau sheria yako.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Waovu wamenitegea mtego, lakini sijapotea mbali na maagizo yako.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Nimezifanya amri za agano lako kama urithi wangu milele, maana hizo ni furaha ya moyo wangu.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Moyo wangu umewekwa kuzitii sheria zako milele mpaka mwisho kabisa. SAMEKH.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Ninawachukia watu wa kusita-sita, lakini naipenda sheria yako.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Wewe ni ficho langu na ngao yangu; nalingoja neno lako.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Ondokeni kwangu, ninyi mtendao uovu, ili niweze kuzitii amri za Mungu wangu.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Uniwezeshe kwa neno lako ili niweze kuishi na nisiaibike na matumaini yangu.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Unisaidie, nami nitakuwa salama; siki zote nitazitafakari sheria zako.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Wewe huwakataa wale wote wapoteao mbali na sheria zako, maana watu hao ni wadanganyifu na si wakuaminika.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Wewe huwaondoa waovu wa nchi kama takataka; kwa hiyo ninazipenda amri zako thabiti.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Mwili wangu hutetemeka kwa hofu yako, na ninaziogopa amri za haki yako. AYIN.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Ninafanya kilicho sahihi na haki; usiniache kwa watesi wangu.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Uwe mdhamini wa ustawi wa mtumishi wako; usiwaache wenye kiburi wanionee.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Macho yangu yanachoka kwa kuusubiri wokovu wako na neno lako la haki.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Mwoneshe mtumishi wako uaminifu wa agano lako, na unifundishe sheria zako.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Mimi ni mtumishi wako; unipe uelewa ili niweze kuzijua amri za agano lako.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Ni wakati wa Yahwe kutenda, kwa maana watu wamevunja sheria yako.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Hakika ninazipenda amri zako kuliko dhahabu, naam, kuliko dhahabu safi.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Hivyo ninayafuata maagizo yako yote kwa makini, na ninachukia kila njia ya uongo. PE.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Sheria zako ni za ajabu, ndiyo sababu ninazitii.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Ufafanuzi wa maneno yako huleta nuru; na kumpa ufahamu mjinga.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Ninafungua kinywa changu na kutweta, maana ninazitamani amri zako.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Unigeukie na unihurumie, kama ufanyavyo siku zote kwa wale walipendao jina lako.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Uziongoze hatua zangu kwa neno lako; usiruhusu dhambi yeyote initawale.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Unikomboe dhidi ya wanadamu waonevu ili niyatii maagizo yako.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Uso wako umwangazie mtumishi wako, na unifundishe sheria zako.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Mito ya machozi yatiririka kutoka machoni pangu kwa sababu watu hawaitii sheria yako. TSADHE.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Wewe ni mwenye haki, Yahwe, na amri zako ni haki.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Umezipa amri za agano lako haki na uaminifu.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Hasira imeniangamiza kwa sababu adui zangu husahau maneno yako.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Neno lako limepimwa sana, naye mtumishi wako analipenda.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Sina umuhimu na ninadharauliwa, lakini bado siyasahau maagizo yako.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Hukumu yako ni ya haki milele, na sheria yako ni ya kuaminika.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Japo dhiki na taabu vimenipata, amri zako bado ni furaha yangu.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Amri za agano lako ni za haki milele; unipe uelewa ili niweze kuishi. QOPH.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Nililia kwa moyo wangu wote, “Unijibu, Yahwe, nitazishika sheria zako.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Ninakuita wewe; uniokoe, nami nitazitii amri za agano lako.”
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
NInaamka asubuhi kabla jua halijachomoza na kulia kwa ajili ya msaada.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Ninatumaini katika maneno yako. Macho yangu yako wazi usiku kucha ili niweze kutafakari juu ya neno lako.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Sikia sauti yangu katika uaminifu wa agano lako; uniweke hai, Yahwe, kama ulivyoahidi katika amri zako za haki.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Wale wanaonitesa wananikaribia, lakini wako mbali na sheria yako.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Wewe uko karibu, Yahwe, na amri zako ni za kuaminika.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Muda mrefu uliopita nilijifunza kutoka katika amri za agano lako ulizoziweka katika mahali pa milele. RESH.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Uyatazame mateso yangu na unisaidie, maana siisahau sheria yako.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Unitetee na kunikomboa; unihifadhi, kama ulivyo ahidi katika neno lako.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Wokovu uko mbali na waovu, maana hawazipendi amri zako.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Matendo yako ya huruma ni makuu, Yahwe; uniweke hai; kama ufanyavyo siku zote.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Watesi wangu na adui zangu ni wengi, lakini bado sijaenda mbali na amri za agano lako.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Nimewaona wasaliti wakitia kinyaa kwa sababu hawalishiki neno lako.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Tazama jinsi niyapendavyo maagizo yako; uniweke hai, Yahwe, kama ulivyoahidi katika uaminifu wa agano lako.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Kiini cha neno lako ni kweli; kila mmoja mwenye amri za haki hudumu milele. SHIN.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Wakuu hunitesa bila sababu; moyo wangu hutetemeka, ukiogopa kutolitii neno lako.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Ninalifurahia neno lako kama apataye nyara nyingi.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Ninachukia na kudharau uongo, lakini naipenda sheria yako.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Mara saba kwa siku ninakusifu wewe kwa sababu ya amri zako za haki.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Wana amani nyingi, waipendao sheria yako; hakuna cha kuwatia mashakani.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Naungoja wokovu wako, Yahwe, na ninatii amri zako.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Ninazishika amri zako thabiti, na ninazipenda sana.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Ninayashika maagizo yako na amri zako thabiti, kwa maana unajua kila kitu nifanyacho. TAV.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Sikia kilio changu, Yahwe; unipe uelewa wa neno lako.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Maombi yangu yaje mbele zako; unisaidie, kama ulivyoahidi katika neno lako.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Midomo yangu na imwage sifa, maana wewe unanifundisha sheria zako.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Ulimi wangu na uimbe kuhusu neno lako, maana amri zako zote ni za haki.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Mkono wako unisaidie, maana nimechagua maagizo yako.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Ninautamani wokovu wako, Yahwe, na sheria yako ni furaha yangu.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Naomba niishi na nikusifu wewe, na amri zako za haki zinisaidie.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Nimetanga-tanga kama kondoo aliyepotea; mtafute mtumishi wako, kwa maana sijazisahau amri zako.