< Masalimo 119 >
1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Bienaventurados los perfectos de camino: los que andan en la ley de Jehová.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Bienaventurados los que guardan sus testimonios; y con todo el corazón le buscan.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Ítem, los que no hacen iniquidad, andan en sus caminos.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Tú encargaste tus mandamientos, que sean muy guardados.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
¡Ojalá fuesen ordenados mis caminos a guardar tus estatutos!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Entonces no sería yo avergonzado, cuando mirase en todos tus mandamientos.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Alabarte he con rectitud de corazón, cuando aprendiere los juicios de tu justicia.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Tus estatutos guardaré: no me dejes enteramente.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
¿Con qué limpiará el mozo su camino? cuando guardare tu palabra.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Con todo mi corazón te he buscado: no me dejes errar de tus mandamientos.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
En mi corazón he guardado tus dichos, para no pecar contra ti.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Bendito tú, o! Jehová, enséñame tus estatutos.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Con mis labios he contado todos los juicios de tu boca.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
En el camino de tus testimonios me he regocijado, como sobre toda riqueza.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
En tus mandamientos meditaré; y consideraré tus caminos.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
En tus estatutos me recrearé: no me olvidaré de tus palabras.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Haz este bien a tu siervo; que viva, y guarde tu palabra.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Destapa mis ojos; y miraré las maravillas de tu ley.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Advenedizo soy yo en la tierra: no encubras de mi tus mandamientos.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Quebrantada está mi alma de desear tus juicios todo el tiempo.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Destruiste a los soberbios malditos, que yerran de tus mandamientos.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Aparta de mí oprobio y menosprecio; porque tus testimonios he guardado.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Príncipes también se asentaron, y hablaron contra mí: meditando tu siervo en tus estatutos.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
También tus testimonios son mis delicias: los varones de mi consejo.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Apegóse con el polvo mi alma: vivifícame según tu palabra.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Mis caminos te conté, y respondísteme: enséñame tus estatutos.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
El camino de tus mandamientos házme entender; y meditaré en tus maravillas.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Mi alma se destila de ansia: confírmame según tu palabra.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Camino de mentira aparta de mí: y de tu ley házme misericordia.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
El camino de la verdad escogí: tus juicios he puesto delante de mí.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Allegádome he a tus testimonios, o! Jehová, no me avergüences.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Por el camino de tus mandamientos correré: cuando ensanchares mi corazón.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Enséñame, o! Jehová, el camino de tus estatutos; y guardarle he hasta el fin.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Dáme entendimiento, y guardaré tu ley; y guardarla he de todo corazón.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Guíame por la senda de tus mandamientos; porque en ella tengo mi verdad.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Inclina mi corazón a tus testimonios: y no a avaricia.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Aparta mis ojos, que no vean la vanidad: avívame en tu camino.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Confirma tu palabra a tu siervo, que te teme.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Quita de mí el oprobio que he temido; porque buenos son tus juicios.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
He aquí yo he codiciado tus mandamientos: en tu justicia avívame.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Y véngame tu misericordia, o! Jehová: tu salud, conforme a tu dicho.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Y daré por respuesta a mi avergonzador, que en tu palabra he confiado.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Y no quites de mi boca palabra de verdad en ningún tiempo; porque a tu juicio espero.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Y guardaré tu ley siempre, por siglo y siglo.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Y andaré en anchura, porque busqué tus mandamientos.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Y hablaré de tus testimonios delante de los reyes; y no me avergonzaré.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Y deleitarme he en tus mandamientos, que amé.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Y alzaré mis manos a tus mandamientos, que amé; y meditaré en tus estatutos.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Acuérdate de la palabra dada a tu siervo: en la cual me has hecho esperar.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Esta es mi consolación en mi aflicción; porque tu dicho me vivificó.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Los soberbios se burlaron mucho de mí: de tu ley no me he apartado.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Acordéme, o! Jehová, de tus juicios antiguos, y me consolé.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Temblor me tomó a causa de los impíos, que dejan tu ley.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Canciones me son tus estatutos en la casa de mis peregrinaciones.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Acordéme en la noche de tu nombre, o! Jehová, y guardé tu ley.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Esto tuve, porque guardaba tus mandamientos.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Mi porción, o! Jehová, dije, será guardar tus palabras.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
En tu presencia supliqué de todo corazón: ten misericordia de mí según tu dicho.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Consideré mis caminos, y torné mis pies a tus testimonios.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Apresuréme, y no me detuve, a guardar tus mandamientos.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Compañías de impíos me han saqueado: mas no me he olvidado de tu ley.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
A media noche me levantaré a alabarte sobre los juicios de tu justicia.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Compañero soy yo a todos los que te temieren; y guardaren tus mandamientos.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
De tu misericordia, o! Jehová, está llena la tierra: tus estatutos enséñame.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Bien has hecho con tu siervo, o! Jehová, conforme a tu palabra.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Bondad de sentido, y sabiduría enséñame, porque a tus mandamientos he creído.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Antes que fuera humillado, yo erraba: mas ahora tu palabra guardo.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Bueno eres tú, y bienhechor: enséñame tus estatutos.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Compusieron sobre mí mentira los soberbios: mas yo de todo corazón guardaré tus mandamientos.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Engrosóse su corazón como sebo: mas yo en tu ley me he deleitado.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Bueno me es haber sido humillado, para que aprenda tus estatutos.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Mejor me es la ley de tu boca, que millares de oro y de plata.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Tus manos me hicieron, y me compusieron: házme entender, y aprenderé tus mandamientos.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Los que te temen, me verán, y se alegrarán; porque a tu palabra he esperado.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Conozco, o! Jehová, que tus juicios son justicia, y que con verdad me afligiste.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Sea ahora tu misericordia para consolarme, conforme a lo que has dicho a tu siervo.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Vénganme tus misericordias, y viva; porque tu ley es mis delicias.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Sean avergonzados los soberbios, porque sin causa me han calumniado: yo empero meditaré en tus mandamientos.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Tórnense a mí los que te temen, y saben tus testimonios.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Sea mi corazón perfecto en tus estatutos; porque no sea avergonzado.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Desfalleció de deseo mi alma por tu salud, esperando a tu palabra.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Desfallecieron mis ojos por tu dicho, diciendo: ¿Cuándo me consolarás?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Porque estoy como el odre al humo: mas no he olvidado tus estatutos.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
¿Cuántos son los días de tu siervo? ¿cuándo harás juicio contra los que me persiguen?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Los soberbios me han cavado hoyos: mas no según tu ley.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Todos tus mandamientos son verdad, sin causa me persiguen, ayúdame.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Casi me han consumido por tierra: mas yo no he dejado tus mandamientos.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Conforme a tu misericordia vivifícame; y guardaré los testimonios de tu boca.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Para siempre, o! Jehová, permanece tu palabra en los cielos.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Por generación y generación es tu verdad: tú afirmaste la tierra, y persevera.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Por tu ordenación perseveran hasta hoy; porque todas ellas son tus siervos.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Si tu ley no hubiese sido mis delicias, ya hubiera perecido en mi aflicción.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Nunca jamás me olvidaré de tus mandamientos; porque con ellos me has vivificado.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Tuyo soy yo, guárdame; porque tus mandamientos he buscado.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Los impíos me han aguardado para destruirme: mas yo entenderé en tus testimonios.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
A toda perfección he visto fin: ancho es tu mandamiento en gran manera.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
¡Cuánto he amado tu ley! todo el día ella es mi meditación.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Más que mis enemigos me has hecho sabio con tus mandamientos; porque me son eternos.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Más que todos mis enseñadores he entendido; porque tus testimonios han sido mi meditación.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Más que los viejos he entendido: porque he guardado tus mandamientos.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
De todo mal camino detuve mis pies, para guardar tu palabra.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
De tus juicios no me aparté; porque tú me enseñaste.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
¡Cuán dulces han sido a mi paladar tus palabras! más que la miel a mi boca.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
De tus mandamientos, he adquirido entendimiento; por tanto he aborrecido todo camino de mentira.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Lámpara es a mis pies tu palabra, y lumbre a mi camino.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Juré, y afirmé, de guardar los juicios de tu justicia.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Afligido estoy en gran manera, o! Jehová: vivifícame conforme a tu palabra.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Los sacrificios voluntarios de mi boca, ruégote, o! Jehová, que te sean agradables; y enséñame tus juicios.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Mi alma está en mi palma de continuo: mas de tu ley no me he olvidado.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Los impíos me pusieron lazo: empero yo no me desvié de tus mandamientos.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Por heredad he tomado tus testimonios para siempre; porque son el gozo de mi corazón.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Mi corazón incliné a hacer tus estatutos de continuo hasta el fin.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Las cautelas aborrezco, y tu ley he amado.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Mi escondedero y mi escudo eres tú, a tu palabra he esperado.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Apartáos de mí los malignos, y guardaré los mandamientos de mi Dios.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Susténtame conforme a tu palabra, y viviré, y no me avergüences de mi esperanza.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Sosténme, y seré salvo; y deleitarme he en tus estatutos siempre.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Tú atropellaste a todos los que yerran de tus estatutos; porque mentira es su engaño.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Como escorias hiciste deshacer a todos los impíos de la tierra: por tanto yo he amado tus testimonios.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Mi carne se ha erizado de temor de ti; y de tus juicios he tenido miedo.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Juicio y justicia he hecho: no me dejes a mis opresores.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Responde por tu siervo para bien: no me hagan violencia los soberbios.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mis ojos desfallecieron por tu salud, y por el dicho de tu justicia.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Haz con tu siervo según tu misericordia; y enséñame tus estatutos.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Tu siervo soy yo; dáme entendimiento, para que sepa tus testimonios.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Tiempo es de hacer, o! Jehová: disipado han tu ley.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Por tanto yo he amado tus mandamientos más que el oro, y más que el oro muy puro.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Por tanto todos los mandamientos de todas las cosas estimé rectos: todo camino de mentira aborrecí.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Maravillosos son tus testimonios; por tanto los ha guardado mi alma.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
El principio de tus palabras alumbra: hace entender a los simples.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Mi boca abrí y suspiré; porque deseaba tus mandamientos.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Mira a mí, y ten misericordia de mí: como acostumbras con los que aman tu nombre.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Ordena mis pasos con tu palabra; y ninguna iniquidad se enseñoree de mí.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Redímeme de la violencia de los hombres; y guardaré tus mandamientos.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Haz que tu rostro resplandezca sobre tu siervo; y enséñame tus estatutos.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Ríos de aguas descendieron de mis ojos; porque no guardaban tu ley.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Justo eres tú, o! Jehová, y rectos tus juicios.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Encargáste la justicia, es a saber, tus testimonios, y tu verdad.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Mi zelo me ha consumido; porque mis enemigos se olvidaron de tus palabras.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Afinada es tu palabra en gran manera; y tu siervo la ama.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Pequeño soy yo y desechado: mas no me he olvidado de tus mandamientos.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Tu justicia es justicia eterna; y tu ley verdad.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Aflicción y angustia me hallaron: mas tus mandamientos fueron mis delicias.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Justicia eterna son tus testimonios: dáme entendimiento, y viviré.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Clamé con todo mi corazón: respóndeme Jehová, y guardaré tus estatutos.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Clamé a ti; sálvame, y guardaré tus testimonios.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Previne al alba y clamé, esperé tu palabra.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Previnieron mis ojos las veladas, para meditar en tus palabras.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Oye mi voz conforme a tu misericordia, o! Jehová: vivifícame conforme a tu juicio.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Acercáronse los que me persiguen a la maldad: alejáronse de tu ley.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Cercano estás tú, Jehová, y todos tus mandamientos son verdad.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Ya ha mucho que he entendido de tus mandamientos, que para siempre los fundaste.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Mira mi aflicción, y escápame; porque de tu ley no me he olvidado,
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Pleitea mi pleito, y redímeme: vivifícame con tu palabra.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Lejos está de los impíos la salud; porque no buscan tus estatutos.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Muchas son tus misericordias, o! Jehová: vivifícame conforme a tus juicios.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Muchos son mis persiguidores y mis enemigos; mas de tus testimonios no me he apartado.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Veía a los prevaricadores, y carcomíame; porque no guardaban tus palabras.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Mira, o! Jehová, que amo tus mandamientos: vivifícame conforme a tu misericordia.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
El principio de tu palabra es verdad; y eterno todo juicio de tu justicia.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Príncipes me han perseguido sin causa: mas de tus palabras tuvo miedo mi corazón.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Regocíjome yo sobre tu palabra, como el que halla muchos despojos.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
La mentira aborrezco, y abomino; tu ley amo.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Siete veces al día te alabo sobre los juicios de tu justicia.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Mucha paz tienen los que aman tu ley; y no hay para ellos tropezón.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Tu salud he esperado, o! Jehová; y tus mandamientos he practicado.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Mi alma ha guardado tus testimonios; y en gran manera los he amado.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Guardado he tus mandamientos, y tus testimonios; porque todos mis caminos están delante de ti.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Acérquese mi clamor delante de ti, o! Jehová: dáme entendimiento conforme a tu palabra.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Venga mi oración delante de ti: escápame conforme a tu dicho.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Mis labios rebosarán alabanza, cuando me enseñares tus estatutos.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Hablará mi lengua tus palabras; porque todos tus mandamientos son justicia.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Sea tu mano en mi socorro; porque tus mandamientos he escogido.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Deseado he tu salud, o! Jehová; y tu ley es mis delicias.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Viva mi alma, y alábete; y tus juicios me ayuden.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Yo me perdí, como oveja que se pierde: busca a tu siervo, porque no me he olvidado de tus mandamientos.