< Masalimo 119 >
1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
alleluia aleph beati inmaculati in via qui ambulant in lege Domini
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
beati qui scrutantur testimonia eius in toto corde exquirent eum
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
non enim qui operantur iniquitatem in viis eius ambulaverunt
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
tu mandasti mandata tua custodire nimis
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
utinam dirigantur viae meae ad custodiendas iustificationes tuas
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
tunc non confundar cum perspexero in omnibus mandatis tuis
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
confitebor tibi in directione cordis in eo quod didici iudicia iustitiae tuae
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
iustificationes tuas custodiam non me derelinquas usquequaque
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
beth in quo corriget adulescentior viam suam in custodiendo sermones tuos
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
in toto corde meo exquisivi te non repellas me a mandatis tuis
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
in corde meo abscondi eloquia tua ut non peccem tibi
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
benedictus es Domine doce me iustificationes tuas
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
in labiis meis pronuntiavi omnia iudicia oris tui
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
in via testimoniorum tuorum delectatus sum sicut in omnibus divitiis
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
in mandatis tuis exercebor et considerabo vias tuas
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
in iustificationibus tuis meditabor non obliviscar sermones tuos
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
gimel retribue servo tuo vivifica me et custodiam sermones tuos
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
revela oculos meos et considerabo mirabilia de lege tua
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
incola ego sum in terra non abscondas a me mandata tua
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
concupivit anima mea desiderare iustificationes tuas in omni tempore
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
increpasti superbos maledicti qui declinant a mandatis tuis
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
aufer a me obprobrium et contemptum quia testimonia tua exquisivi
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
etenim sederunt principes et adversum me loquebantur servus autem tuus exercebatur in iustificationibus tuis
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
nam et testimonia tua meditatio mea et consilium meum iustificationes tuae
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
deleth adhesit pavimento anima mea vivifica me secundum verbum tuum
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
vias meas enuntiavi et exaudisti me doce me iustificationes tuas
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
viam iustificationum tuarum instrue me et exercebor in mirabilibus tuis
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
dormitavit anima mea prae taedio confirma me in verbis tuis
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
viam iniquitatis amove a me et lege tua miserere mei
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
viam veritatis elegi iudicia tua non sum oblitus
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
adhesi testimoniis tuis Domine noli me confundere
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
viam mandatorum tuorum cucurri cum dilatasti cor meum
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
he legem pone mihi Domine viam iustificationum tuarum et exquiram eam semper
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
da mihi intellectum et scrutabor legem tuam et custodiam illam in toto corde meo
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
deduc me in semita mandatorum tuorum quia ipsam volui
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
inclina cor meum in testimonia tua et non in avaritiam
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
averte oculos meos ne videant vanitatem in via tua vivifica me
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
statue servo tuo eloquium tuum in timore tuo
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
amputa obprobrium meum quod suspicatus sum quia iudicia tua iucunda
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
ecce concupivi mandata tua in aequitate tua vivifica me
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
vav et veniat super me misericordia tua Domine salutare tuum secundum eloquium tuum
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
et respondebo exprobrantibus mihi verbum quia speravi in sermonibus tuis
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
et ne auferas de ore meo verbum veritatis usquequaque quia in iudiciis tuis supersperavi
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
et custodiam legem tuam semper in saeculum et in saeculum saeculi
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
et ambulabam in latitudine quia mandata tua exquisivi
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
et loquebar in testimoniis tuis in conspectu regum et non confundebar
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
et meditabar in mandatis tuis quae dilexi
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
et levavi manus meas ad mandata quae dilexi et exercebar in iustificationibus tuis
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
zai memor esto verbi tui servo tuo in quo mihi spem dedisti
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
haec me consolata est in humilitate mea quia eloquium tuum vivificavit me
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
superbi inique agebant usquequaque a lege autem tua non declinavi
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
memor fui iudiciorum tuorum a saeculo Domine et consolatus sum
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
defectio tenuit me prae peccatoribus derelinquentibus legem tuam
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
cantabiles mihi erant iustificationes tuae in loco peregrinationis meae
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
memor fui in nocte nominis tui Domine et custodivi legem tuam
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
haec facta est mihi quia iustificationes tuas exquisivi
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
heth portio mea Dominus dixi custodire legem tuam
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
deprecatus sum faciem tuam in toto corde meo miserere mei secundum eloquium tuum
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
cogitavi vias meas et avertisti pedes meos in testimonia tua
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
paratus sum et non sum turbatus ut custodiam mandata tua
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
funes peccatorum circumplexi sunt me et legem tuam non sum oblitus
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
media nocte surgebam ad confitendum tibi super iudicia iustificationis tuae
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
particeps ego sum omnium timentium te et custodientium mandata tua
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
misericordia Domini plena est terra iustificationes tuas doce me
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
teth bonitatem fecisti cum servo tuo Domine secundum verbum tuum
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
bonitatem et disciplinam et scientiam doce me quia mandatis tuis credidi
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
priusquam humiliarer ego deliqui propterea eloquium tuum custodivi
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
bonus es tu et in bonitate tua doce me iustificationes tuas
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
multiplicata est super me iniquitas superborum ego autem in toto corde scrutabor mandata tua
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
coagulatum est sicut lac cor eorum ego vero legem tuam meditatus sum
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
bonum mihi quia humiliasti me ut discam iustificationes tuas
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
bonum mihi lex oris tui super milia auri et argenti
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
ioth manus tuae fecerunt me et plasmaverunt me da mihi intellectum et discam mandata tua
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
qui timent te videbunt me et laetabuntur quia in verba tua supersperavi
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
cognovi Domine quia aequitas iudicia tua et veritate humiliasti me
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
fiat misericordia tua ut consoletur me secundum eloquium tuum servo tuo
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
veniant mihi miserationes tuae et vivam quia lex tua meditatio mea est
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
confundantur superbi quia iniuste iniquitatem fecerunt in me ego autem exercebor in mandatis tuis
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
convertantur mihi timentes te et qui noverunt testimonia tua
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
fiat cor meum inmaculatum in iustificationibus tuis ut non confundar
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
caf defecit in salutare tuum anima mea in verbum tuum supersperavi
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
defecerunt oculi mei in eloquium tuum dicentes quando consolaberis me
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
quia factus sum sicut uter in pruina iustificationes tuas non sum oblitus
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
quot sunt dies servo tuo quando facies de persequentibus me iudicium
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
narraverunt mihi iniqui fabulationes sed non ut lex tua
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
omnia mandata tua veritas inique persecuti sunt me adiuva me
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
paulo minus consummaverunt me in terra ego autem non dereliqui mandata tua
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
secundum misericordiam tuam vivifica me et custodiam testimonia oris tui
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
lamed in aeternum Domine verbum tuum permanet in caelo
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
in generationem et generationem veritas tua fundasti terram et permanet
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
ordinatione tua perseverat dies quoniam omnia serviunt tibi
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
nisi quod lex tua meditatio mea est tunc forte perissem in humilitate mea
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
in aeternum non obliviscar iustificationes tuas quia in ipsis vivificasti me
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
tuus sum ego salvum me fac quoniam iustificationes tuas exquisivi
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
me expectaverunt peccatores ut perderent me testimonia tua intellexi
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
omni consummationi vidi finem latum mandatum tuum nimis
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
mem quomodo dilexi legem tuam tota die meditatio mea est
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
super inimicos meos prudentem me fecisti mandato tuo quia in aeternum mihi est
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
super omnes docentes me intellexi quia testimonia tua meditatio mea est
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
super senes intellexi quia mandata tua quaesivi
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
ab omni via mala prohibui pedes meos ut custodiam verba tua
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
a iudiciis tuis non declinavi quia tu legem posuisti mihi
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
quam dulcia faucibus meis eloquia tua super mel ori meo
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
a mandatis tuis intellexi propterea odivi omnem viam iniquitatis
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
nun lucerna pedibus meis verbum tuum et lumen semitis meis
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
iuravi et statui custodire iudicia iustitiae tuae
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
humiliatus sum usquequaque Domine vivifica me secundum verbum tuum
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
voluntaria oris mei beneplacita fac Domine et iudicia tua doce me
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
anima mea in manibus meis semper et legem tuam non sum oblitus
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
posuerunt peccatores laqueum mihi et de mandatis tuis non erravi
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
hereditate adquisivi testimonia tua in aeternum quia exultatio cordis mei sunt
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
inclinavi cor meum ad faciendas iustificationes tuas in aeternum propter retributionem
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
samech iniquos odio habui et legem tuam dilexi
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
adiutor meus et susceptor meus es tu in verbum tuum supersperavi
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
declinate a me maligni et scrutabor mandata Dei mei
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
suscipe me secundum eloquium tuum et vivam et non confundas me ab expectatione mea
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
adiuva me et salvus ero et meditabor in iustificationibus tuis semper
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
sprevisti omnes discedentes a iustitiis tuis quia iniusta cogitatio eorum
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
praevaricantes reputavi omnes peccatores terrae ideo dilexi testimonia tua
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
confige timore tuo carnes meas a iudiciis enim tuis timui
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
ain feci iudicium et iustitiam non tradas me calumniantibus me
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
suscipe servum tuum in bonum non calumnientur me superbi
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
oculi mei defecerunt in salutare tuum et in eloquium iustitiae tuae
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
fac cum servo tuo secundum misericordiam tuam et iustificationes tuas doce me
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
servus tuus sum ego da mihi intellectum et sciam testimonia tua
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
tempus faciendi Domino dissipaverunt legem tuam
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
ideo dilexi mandata tua super aurum et topazion
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
propterea ad omnia mandata tua dirigebar omnem viam iniquam odio habui
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
fe mirabilia testimonia tua ideo scrutata est ea anima mea
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
declaratio sermonum tuorum inluminat et intellectum dat parvulis
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
os meum aperui et adtraxi spiritum quia mandata tua desiderabam
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
aspice in me et miserere mei secundum iudicium diligentium nomen tuum
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
gressus meos dirige secundum eloquium tuum et non dominetur mei omnis iniustitia
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
redime me a calumniis hominum et custodiam mandata tua
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
faciem tuam inlumina super servum tuum et doce me iustificationes tuas
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
exitus aquarum deduxerunt oculi mei quia non custodierunt legem tuam
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
sade iustus es Domine et rectum iudicium tuum
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
mandasti iustitiam testimonia tua et veritatem tuam nimis
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
tabescere me fecit zelus meus quia obliti sunt verba tua inimici mei
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
ignitum eloquium tuum vehementer et servus tuus dilexit illud
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
adulescentulus sum ego et contemptus iustificationes tuas non sum oblitus
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
iustitia tua iustitia in aeternum et lex tua veritas
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
tribulatio et angustia invenerunt me mandata tua meditatio mea
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
aequitas testimonia tua in aeternum intellectum da mihi et vivam
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
cof clamavi in toto corde exaudi me Domine iustificationes tuas requiram
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
clamavi te salvum me fac et custodiam mandata tua
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
praeveni in maturitate et clamavi in verba tua supersperavi
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
praevenerunt oculi mei ad diluculum ut meditarer eloquia tua
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
vocem meam audi secundum misericordiam tuam Domine secundum iudicium tuum vivifica me
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
adpropinquaverunt persequentes me iniquitate a lege autem tua longe facti sunt
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
prope es tu Domine et omnes viae tuae veritas
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
initio cognovi de testimoniis tuis quia in aeternum fundasti ea
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
res vide humilitatem meam et eripe me quia legem tuam non sum oblitus
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
iudica iudicium meum et redime me propter eloquium tuum vivifica me
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
longe a peccatoribus salus quia iustificationes tuas non exquisierunt
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
misericordiae tuae multae Domine secundum iudicia tua vivifica me
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
multi qui persequuntur me et tribulant me a testimoniis tuis non declinavi
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
vidi praevaricantes et tabescebam quia eloquia tua non custodierunt
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
vide quoniam mandata tua dilexi Domine in misericordia tua vivifica me
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
principium verborum tuorum veritas et in aeternum omnia iudicia iustitiae tuae
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
sen principes persecuti sunt me gratis et a verbis tuis formidavit cor meum
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
laetabor ego super eloquia tua sicut qui invenit spolia multa
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
iniquitatem odio habui et abominatus sum legem autem tuam dilexi
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
septies in die laudem dixi tibi super iudicia iustitiae tuae
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
pax multa diligentibus legem tuam et non est illis scandalum
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
expectabam salutare tuum Domine et mandata tua dilexi
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
custodivit anima mea testimonia tua et dilexi ea vehementer
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
servavi mandata tua et testimonia tua quia omnes viae meae in conspectu tuo
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
thau adpropinquet deprecatio mea in conspectu tuo Domine iuxta eloquium tuum da mihi intellectum
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
intret postulatio mea in conspectu tuo secundum eloquium tuum eripe me
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
eructabunt labia mea hymnum cum docueris me iustificationes tuas
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
pronuntiabit lingua mea eloquium tuum quia omnia mandata tua aequitas
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
fiat manus tua ut salvet me quoniam mandata tua elegi
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
concupivi salutare tuum Domine et lex tua meditatio mea
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
vivet anima mea et laudabit te et iudicia tua adiuvabunt me
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
erravi sicut ovis quae periit quaere servum tuum quia mandata tua non sum oblitus