< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Alleluia. ALEPH. Beati immaculati in via: qui ambulant in lege Domini.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Beati, qui scrutantur testimonia eius: in toto corde exquirunt eum.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Non enim qui operantur iniquitatem, in viis eius ambulaverunt.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Tu mandasti mandata tua custodiri nimis.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Utinam dirigantur viæ meæ, ad custodiendas iustificationes tuas.
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Tunc non confundar, cum perspexero in omnibus mandatis tuis.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Confitebor tibi in directione cordis: in eo quod didici iudicia iustitiæ tuæ.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Iustificationes tuas custodiam: non me derelinquas usquequaque.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
BETH. In quo corrigit adolescentior viam suam? in custodiendo sermones tuos.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
In toto corde meo exquisivi te: ne repellas me a mandatis tuis.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
In corde meo abscondi eloquia tua: ut non peccem tibi.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Benedictus es Domine: doce me iustificationes tuas.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
In labiis meis, pronunciavi omnia iudicia oris tui.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
In via testimoniorum tuorum delectatus sum, sicut in omnibus divitiis.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
In mandatis tuis exercebor: et considerabo vias tuas.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
In iustificationibus tuis meditabor: non obliviscar sermones tuos.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
GHIMEL. Retribue servo tuo, vivifica me: et custodiam sermones tuos.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Revela oculos meos: et considerabo mirabilia de lege tua.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Incola ego sum in terra: non abscondas a me mandata tua.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Concupivit anima mea desiderare iustificationes tuas, in omni tempore.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Increpasti superbos: maledicti qui declinant a mandatis tuis.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Aufer a me opprobrium, et contemptum: quia testimonia tua exquisivi.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Etenim sederunt principes, et adversum me loquebantur: servus autem tuus exercebatur in iustificationibus tuis.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Nam et testimonia tua meditatio mea est: et consilium meum iustificationes tuæ.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
DALETH. Adhæsit pavimento anima mea: vivifica me secundum verbum tuum.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Vias meas enunciavi, et exaudisti me: doce me iustificationes tuas.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Viam iustificationum tuarum instrue me: et exercebor in mirabilibus tuis.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Dormitavit anima mea præ tædio: confirma me in verbis tuis.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Viam iniquitatis amove a me: et de lege tua miserere mei.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Viam veritatis elegi: iudicia tua non sum oblitus.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Adhæsi testimoniis tuis Domine: noli me confundere.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Viam mandatorum tuorum cucurri, cum dilatasti cor meum.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
HE. Legem pone mihi Domine viam iustificationum tuarum: et exquiram eam semper.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Da mihi intellectum, et scrutabor legem tuam: et custodiam illam in toto corde meo.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Deduc me in semitam mandatorum tuorum: quia ipsam volui.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Inclina cor meum in testimonia tua: et non in avaritiam.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Averte oculos meos ne videant vanitatem: in via tua vivifica me.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Statue servo tuo eloquium tuum, in timore tuo.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Amputa opprobrium meum, quod suspicatus sum: quia iudicia tua iucunda.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Ecce concupivi mandata tua: in æquitate tua vivifica me.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
VAU. Et veniat super me misericordia tua Domine: salutare tuum secundum eloquium tuum.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Et respondebo exprobrantibus mihi verbum: quia speravi in sermonibus tuis.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Et ne auferas de ore meo verbum veritatis usquequaque: quia in iudiciis tuis supersperavi.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Et custodiam legem tuam semper: in sæculum et in sæculum sæculi.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Et ambulabam in latitudine: quia mandata tua exquisivi.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Et loquebar in testimoniis tuis in conspectu regum: et non confundebar.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Et meditabar in mandatis tuis, quæ dilexi.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Et levavi manus meas ad mandata tua, quæ dilexi: et exercebar in iustificationibus tuis.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
ZAIN. Memor esto verbi tui servo tuo, in quo mihi spem dedisti.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Hæc me consolata est in humilitate mea: quia eloquium tuum vivificavit me.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Superbi inique agebant usquequaque: a lege autem tua non declinavi.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Memor fui iudiciorum tuorum a sæculo Domine: et consolatus sum.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Defectio tenuit me, pro peccatoribus derelinquentibus legem tuam.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Cantabiles mihi erant iustificationes tuæ, in loco peregrinationis meæ.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Memor fui nocte nominis tui Domine: et custodivi legem tuam.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Hæc facta est mihi: quia iustificationes tuas exquisivi.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
HETH. Portio mea Domine, dixi custodire legem tuam.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Deprecatus sum faciem tuam in toto corde meo: miserere mei secundum eloquium tuum.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Cogitavi vias meas: et converti pedes meos in testimonia tua.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Paratus sum, et non sum turbatus: ut custodiam mandata tua.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Funes peccatorum circumplexi sunt me: et legem tuam non sum oblitus.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Media nocte surgebam ad confitendum tibi, super iudicia iustificationis tuæ.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Particeps ego sum omnium timentium te: et custodientium mandata tua.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Misericordia tua Domine plena est terra: iustificationes tuas doce me.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
TETH. Bonitatem fecisti cum servo tuo Domine, secundum verbum tuum.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Bonitatem, et disciplinam, et scientiam doce me: quia mandatis tuis credidi.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Priusquam humiliarer ego deliqui: propterea eloquium tuum custodivi.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Bonus es tu: et in bonitate tua doce me iustificationes tuas.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Multiplicata est super me iniquitas superborum: ego autem in toto corde meo scrutabor mandata tua.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Coagulatum est sicut lac cor eorum: ego vero legem tuam meditatus sum.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Bonum mihi quia humiliasti me: ut discam iustificationes tuas.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Bonum mihi lex oris tui, super millia auri, et argenti.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
IOD. Manus tuæ fecerunt me, et plasmaverunt me: da mihi intellectum, et discam mandata tua.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Qui timent te videbunt me, et lætabuntur: quia in verba tua supersperavi.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Cognovi Domine quia æquitas iudicia tua: et in veritate tua humiliasti me.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Fiat misericordia tua ut consoletur me, secundum eloquium tuum servo tuo.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Veniant mihi miserationes tuæ, et vivam: quia lex tua meditatio mea est.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Confundantur superbi, quia iniuste iniquitatem fecerunt in me: ego autem exercebor in mandatis tuis.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Convertantur mihi timentes te: et qui noverunt testimonia tua.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Fiat cor meum immaculatum in iustificationibus tuis, ut non confundar.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
CAPH. Defecit in salutare tuum anima mea: et in verbum tuum supersperavi.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Defecerunt oculi mei in eloquium tuum, dicentes: Quando consolaberis me?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Quia factus sum sicut uter in pruina: iustificationes tuas non sum oblitus.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Quot sunt dies servi tui: quando facies de persequentibus me iudicium?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Narraverunt mihi iniqui fabulationes: sed non ut lex tua.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Omnia mandata tua veritas: inique persecuti sunt me, adiuva me.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Paulominus consummaverunt me in terra: ego autem non dereliqui mandata tua.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Secundum misericordiam tuam vivifica me: et custodiam testimonia oris tui.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
LAMED. In æternum Domine, verbum tuum permanet in cælo.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
In generationem et generationem veritas tua: fundasti terram, et permanet.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Ordinatione tua perseverat dies: quoniam omnia serviunt tibi.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Nisi quod lex tua meditatio mea est: tunc forte periissem in humilitate mea.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
In æternum non obliviscar iustificationes tuas: quia in ipsis vivificasti me.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Tuus sum ego, salvum me fac: quoniam iustificationes tuas exquisivi.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Me expectaverunt peccatores ut perderent me: testimonia tua intellexi.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Omnis consummationis vidi finem: latum mandatum tuum nimis.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
MEM. Quomodo dilexi legem tuam Domine? tota die meditatio mea est.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Super inimicos meos prudentem me fecisti mandato tuo: quia in æternum mihi est.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Super omnes docentes me intellexi: quia testimonia tua meditatio mea est.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Super senes intellexi: quia mandata tua quæsivi.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Ab omni via mala prohibui pedes meos: ut custodiam verba tua.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
A iudiciis tuis non declinavi: quia tu legem posuisti mihi.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Quam dulcia faucibus meis eloquia tua, super mel ori meo!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
A mandatis tuis intellexi: propterea odivi omnem viam iniquitatis.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
NUN. Lucerna pedibus meis verbum tuum, et lumen semitis meis.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Iuravi, et statui custodire iudicia iustitiæ tuæ.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Humiliatus sum usquequaque Domine: vivifica me secundum verbum tuum.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Voluntaria oris mei beneplacita fac Domine: et iudicia tua doce me.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Anima mea in manibus meis semper: et legem tuam non sum oblitus.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Posuerunt peccatores laqueum mihi: et de mandatis tuis non erravi.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Hereditate acquisivi testimonia tua in æternum: quia exultatio cordis mei sunt.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Inclinavi cor meum ad faciendas iustificationes tuas in æternum, propter retributionem.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
SAMECH. Iniquos odio habui: et legem tuam dilexi.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Adiutor, et susceptor meus es tu: et in verbum tuum supersperavi.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Declinate a me maligni: et scrutabor mandata Dei mei.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Suscipe me secundum eloquium tuum, et vivam: et non confundas me ab expectatione mea.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Adiuva me, et salvus ero: et meditabor in iustificationibus tuis semper.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Sprevisti omnes discedentes a iudiciis tuis: quia iniusta cogitatio eorum.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Prævaricantes reputavi omnes peccatores terræ: ideo dilexi testimonia tua.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Confige timore tuo carnes meas: a iudiciis enim tuis timui.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
AIN. Feci iudicium et iustitiam: non tradas me calumniantibus me.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Suscipe servum tuum in bonum: non calumnientur me superbi.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Oculi mei defecerunt in salutare tuum: et in eloquium iustitiæ tuæ.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Fac cum servo tuo secundum misericordiam tuam: et iustificationes tuas doce me.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Servus tuus sum ego: da mihi intellectum, ut sciam testimonia tua.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Tempus faciendi Domine: dissipaverunt legem tuam.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Ideo dilexi mandata tua, super aurum et topazion.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Propterea ad omnia mandata tua dirigebar: omnem viam iniquam odio habui.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
PHE. Mirabilia testimonia tua: ideo scrutata est ea anima mea.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Declaratio sermonum tuorum illuminat: et intellectum dat parvulis.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Os meum aperui, et attraxi spiritum: quia mandata tua desiderabam.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Aspice in me, et miserere mei, secundum iudicium diligentium nomen tuum.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Gressus meos dirige secundum eloquium tuum: et non dominetur mei omnis iniustitia.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Redime me a calumniis hominum: ut custodiam mandata tua.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Faciem tuam illumina super servum tuum: et doce me iustificationes tuas.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Exitus aquarum deduxerunt oculi mei: quia non custodierunt legem tuam.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
SADE. Iustus es Domine: et rectum iudicium tuum.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Mandasti iustitiam testimonia tua: et veritatem tuam nimis.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Tabescere me fecit zelus meus: quia obliti sunt verba tua inimici mei.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Ignitum eloquium tuum vehementer: et servus tuus dilexit illud.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Adolescentulus sum ego, et contemptus: iustificationes tuas non sum oblitus.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Iustitia tua, iustitia in æternum: et lex tua veritas.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Tribulatio, et angustia invenerunt me: mandata tua meditatio mea est.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Æquitas testimonia tua in æternum: intellectum da mihi, et vivam.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
COPH. Clamavi in toto corde meo, exaudi me Domine: iustificationes tuas requiram.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Clamavi ad te, salvum me fac: ut custodiam mandata tua.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Præveni in maturitate, et clamavi: quia in verba tua supersperavi.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Prævenerunt oculi mei ad te diluculo: ut meditarer eloquia tua.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Vocem meam audi secundum misericordiam tuam Domine: et secundum iudicium tuum vivifica me.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Appropinquaverunt persequentes me iniquitati: a lege autem tua longe facti sunt.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Prope es tu Domine: et omnes viæ tuæ veritas.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Initio cognovi de testimoniis tuis: quia in æternum fundasti ea.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
RES. Vide humilitatem meam, et eripe me: quia legem tuam non sum oblitus.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Iudica iudicium meum, et redime me: propter eloquium tuum vivifica me.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Longe a peccatoribus salus: quia iustificationes tuas non exquisierunt.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Misericordiæ tuæ multæ Domine: secundum iudicium tuum vivifica me.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Multi qui persequuntur me, et tribulant me: a testimoniis tuis non declinavi.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Vidi prævaricantes, et tabescebam: quia eloquia tua non custodierunt.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Vide quoniam mandata tua dilexi Domine: in misericordia tua vivifica me.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Principium verborum tuorum, veritas: in æternum omnia iudicia iustitiæ tuæ.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
SIN. Principes persecuti sunt me gratis: et a verbis tuis formidavit cor meum.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Lætabor ego super eloquia tua: sicut qui invenit spolia multa.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Iniquitatem odio habui, et abominatus sum: legem autem tuam dilexi.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Septies in die laudem dixi tibi, super iudicia iustitiæ tuæ.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Pax multa diligentibus legem tuam: et non est illis scandalum.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Expectabam salutare tuum Domine: et mandata tua dilexi.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Custodivit anima mea testimonia tua: et dilexit ea vehementer.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Servavi mandata tua, et testimonia tua: quia omnes viæ meæ in conspectu tuo.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
TAU. Appropinquet deprecatio mea in conspectu tuo Domine: iuxta eloquium tuum da mihi intellectum.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Intret postulatio mea in conspectu tuo: secundum eloquium tuum eripe me.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Eructabunt labia mea hymnum, cum docueris me iustificationes tuas.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Pronunciabit lingua mea eloquium tuum: quia omnia mandata tua æquitas.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Fiat manus tua ut salvet me: quoniam mandata tua elegi.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Concupivi salutare tuum Domine: et lex tua meditatio mea est.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Vivet anima mea, et laudabit te: et iudicia tua adiuvabunt me.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Erravi, sicut ovis, quæ periit: quære servum tuum, quia mandata tua non sum oblitus.

< Masalimo 119 >