< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Berbahagialah orang yang hidupnya tidak bercela dan taat kepada hukum-hukum TUHAN.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Berbahagialah orang yang mengikuti perintah-Nya, dan dengan segenap hati berusaha mengenal TUHAN.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Berbahagialah orang yang hidup menurut kehendak TUHAN, dan tidak melakukan kejahatan.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Engkau memberi kami hukum-Mu, ya TUHAN, supaya kami melakukannya dengan setia.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Semoga aku dengan hati teguh mengikuti peraturan-peraturan-Mu.
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Jika aku memperhatikan semua perintah-Mu, maka aku tak akan dipermalukan.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Bila aku mempelajari keputusan-Mu yang adil, aku memuji Engkau dengan setulus hati.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Aku mau mentaati hukum-Mu, janganlah sekali-kali meninggalkan aku.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Orang muda dapat menjaga hidupnya tak bercela kalau ia hidup menurut perintah-Mu.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Dengan sepenuh hati aku berusaha mengenal Engkau, jangan biarkan aku menyimpang dari perintah-Mu.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Ajaran-Mu kusimpan dalam hatiku, supaya aku jangan berdosa terhadap-Mu.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Aku memuji Engkau, ya TUHAN, ajarilah aku ketetapan-Mu.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Dengan nyaring aku memaklumkan semua hukum yang Kauberikan.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Aku gembira mengikuti perintah-perintah-Mu, seperti memiliki segala macam harta.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Aku mau mempelajari keputusan-keputusan-Mu, dan memperhatikan petunjuk-petunjuk-Mu.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Ketetapan-Mu membuat aku senang; ajaran-Mu takkan kulupakan.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Kiranya Engkau bermurah hati kepada hamba-Mu ini, supaya aku tetap hidup dan mentaati ajaran-Mu.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Bukalah mataku supaya aku melihat ajaran yang mengagumkan dalam hukum-Mu.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Hanya untuk sementara aku tinggal di dunia, janganlah menyembunyikan hukum-Mu daripadaku.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Hatiku sakit menanggung rindu, aku ingin mengetahui hukum-Mu setiap waktu.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Engkau menegur orang yang sombong, dan mengutuk orang yang menyimpang dari perintah-Mu.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Bebaskanlah aku dari penghinaan dan celaan mereka, sebab aku melakukan peraturan-Mu.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Sekalipun para penguasa berkomplot melawan aku, hamba-Mu ini akan merenungkan ketetapan-Mu.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Peraturan-peraturan-Mu menjadi penasihatku yang menyenangkan hatiku.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Aku berbaring dalam debu; pulihkanlah hidupku menurut janji-Mu.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Aku mengakui perbuatanku, lalu Engkau menjawab aku; ajarilah aku ketetapan-Mu.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Tolonglah aku memahami hukum-hukum-Mu, ajaran-Mu yang mengagumkan akan kurenungkan.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Jiwaku hancur luluh ditimpa kesusahan, kuatkanlah aku sesuai dengan janji-Mu.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Jauhkanlah aku dari jalan yang sesat, karena kebaikan-Mu, ajarilah aku hukum-Mu.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Aku telah memilih untuk taat, perintah-Mu selalu kuingat-ingat.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Aku telah mengikuti peraturan-peraturan-Mu, ya TUHAN, jangan biarkan aku mendapat malu.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Dengan senang aku akan mematuhi perintah-Mu, sebab Engkau membuat aku lebih mengerti.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
TUHAN, ajarilah aku arti ketetapan-ketetapan-Mu, supaya aku mengikutinya sampai akhir.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Buatlah aku mengerti hukum-Mu supaya kutaati, dan kulakukan dengan sepenuh hati.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Semoga aku berpegang teguh pada perintah-Mu, karena itulah kesukaanku.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Berilah aku hasrat untuk mentaati peraturan-Mu, melebihi keinginan menjadi kaya.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Jagalah aku supaya jangan mengejar yang sia-sia, berilah aku hidup menurut kehendak-Mu.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Teguhkanlah kepada hamba-Mu ini janji-Mu, yang Kauberikan kepada orang yang taat kepada-Mu.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Jauhkanlah penghinaan yang kutakuti, karena sungguh baiklah hukum-Mu.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Berilah aku hidup baru, sebab Engkau adil, aku berhasrat mentaati keputusan-keputusan-Mu.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Ya TUHAN, tunjukkanlah betapa Engkau mengasihi aku, selamatkanlah aku sesuai dengan janji-Mu.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Maka dapatlah aku menjawab orang yang menghina aku, sebab aku mengandalkan perkataan-Mu.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Tolonglah aku untuk selalu mengatakan yang benar, sebab aku berharap pada keputusan-Mu.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Aku mau berpegang pada hukum-Mu, untuk selama-lamanya.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Maka aku akan hidup dengan bebas, karena berusaha mematuhi ajaran-Mu.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Peraturan-Mu akan kuwartakan kepada raja-raja, dan aku tak akan mendapat malu.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Kesenanganku ialah melakukan perintah-Mu, sebab aku mencintainya.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Aku menghormati dan mencintai perintah-Mu, ketetapan-Mu akan kurenungkan.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Ingatlah janji-Mu kepada hamba-Mu ini, janji yang memberi harapan kepadaku.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Inilah yang menghibur aku dalam penderitaanku, bahwa janji-Mu itu memberi aku hidup.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Orang sombong sangat menghina aku, tetapi aku tidak menyimpang dari hukum-Mu.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Aku ingat akan hukum-Mu yang ada sejak dahulu, maka terhiburlah hatiku, ya TUHAN.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Aku sangat marah kepada orang jahat, karena mereka meninggalkan hukum-Mu.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Selama hidupku yang singkat di bumi, ketetapan-Mu kujadikan lagu-lagu pujian.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Di waktu malam kuingat pada-Mu, ya TUHAN, hukum-Mu tetap kupegang.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Aku mendapatkan kebahagiaan dalam mentaati perintah-perintah-Mu.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Engkau saja yang kuinginkan, ya TUHAN, aku berjanji akan melakukan ajaran-Mu.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Dengan segenap hati aku mohon belas kasih-Mu, kasihanilah aku sesuai dengan janji-Mu.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Aku telah memikirkan kelakuanku, dan berjanji akan mentaati peraturan-Mu.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Aku bergegas-gegas dan tidak menunggu untuk menjalankan perintah-Mu.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Orang jahat memasang jaring bagiku, tetapi aku tidak melupakan hukum-Mu.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Tengah malam aku bangun hendak memuji Engkau, karena keputusan-keputusan yang adil.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Aku bersahabat dengan semua orang takwa, semua orang yang melakukan perintah-Mu.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Bumi penuh dengan kasih-Mu, ya TUHAN, ajarilah aku ketetapan-ketetapan-M
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Engkau telah memenuhi janji-Mu, ya TUHAN, dan berbuat baik kepada hamba-Mu.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Berilah aku hikmat dan pengetahuan, sebab aku percaya kepada perintah-perintah-Mu.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Sebelum dihukum, aku menyimpang, sekarang aku berpegang pada perintah-Mu.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Sebab Engkau baik dan berbuat baik, ajarilah aku ketetapan-ketetapan-Mu.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Orang sombong memfitnah aku, tapi aku dengan sepenuh hati mentaati keputusan-Mu.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Orang-orang itu tidak mengerti, tetapi bagiku hukum-Mu menyenangkan hati.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Memang baiklah Engkau menghukum aku, supaya aku mengenal ketetapan-ketetapan-Mu.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Bagiku hukum-Mu lebih berharga dari semua emas dan perak di dunia.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Engkaulah yang menjadikan dan membentuk aku, berilah aku pengertian untuk belajar perintah-perintah-Mu.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Orang takwa akan senang bila melihat aku, sebab aku berharap pada janji-Mu.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Aku tahu bahwa keputusan-Mu adil ya TUHAN, Engkau telah menghukum aku karena kesetiaan-Mu.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Semoga kasih-Mu menjadi penghiburanku, sesuai dengan janji-Mu kepada hamba-Mu.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Kasihanilah aku, maka aku tetap hidup, karena hukum-Mu menyenangkan hatiku.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Biarlah orang sombong menjadi malu karena telah memfitnah aku, tetapi aku akan merenungkan perintah-perintah-Mu.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Semoga orang takwa datang kepadaku, semua yang mengenal peraturan-peraturan-Mu.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Semoga hatiku tidak menyimpang dari ketetapan-Mu, supaya aku jangan mendapat malu.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Hatiku sangat rindu akan keselamatan daripada-Mu; aku mengharapkan janji-Mu.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Mataku letih menanti Engkau memenuhi janji-Mu, aku berkata, "Kapan Engkau akan menghibur aku?"
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Kulitku lisut seperti kantong anggur yang usang, tetapi ketetapan-Mu tidak kulupakan.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Sampai kapan hamba-Mu harus bersabar? Kapan Engkau akan menghukum orang-orang yang mengejar aku?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Orang yang tidak mentaati hukum-Mu, telah menggali lubang untuk menjebak aku.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Semua hukum-Mu dapat diandalkan, tolonglah aku, sebab aku dikejar tanpa alasan.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Hampir saja mereka berhasil membunuh aku, tetapi aku tidak mengabaikan perintah-Mu.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Selamatkanlah aku sebab Engkau tetap mengasihi, supaya aku dapat mentaati hukum-Mu.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
TUHAN, sabda-Mu teguh selama-lamanya, kekal abadi di surga.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Kesetiaan-Mu bertahan sepanjang zaman, Engkau menegakkan bumi sehingga tetap ada.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Semua yang ada sekarang, ada karena perintah-Mu, sebab mereka semua adalah hamba-hamba-Mu.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Sekiranya hukum-Mu bukan sumber kegembiraanku, pasti aku sudah mati dalam sengsaraku.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Selamanya aku takkan mengabaikan perintah-Mu, sebab dengan itu Engkau menghidupkan aku.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Selamatkanlah aku, sebab aku ini milik-Mu, aku sudah berusaha mentaati keputusan-Mu.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Orang jahat menunggu hendak membunuh aku, tetapi aku mau memperhatikan hukum-Mu.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Kulihat bahwa yang sempurna pun terbatas, hanya perintah-Mulah yang sempurna.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Betapa kucintai hukum-Mu; aku merenungkannya sepanjang hari.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Aku selalu ingat kepada perintah-Mu, yang membuat aku lebih bijaksana dari musuh-musuhku.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Pengertianku melebihi pengertian guru-guruku, karena aku merenungkan perintah-perintah-Mu.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Aku lebih paham dari orang-orang tua, sebab aku memegang keputusan-keputusan-Mu.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Kuhindari segala kelakuan jahat, supaya aku taat kepada ajaran-Mu.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Aku tidak mengabaikan hukum-Mu, sebab Engkaulah yang mengajar aku.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Alangkah manisnya perkataan-Mu, rasanya lebih manis dari madu!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Hukum-hukum-Mu memberi aku pengertian, sehingga aku membenci kelakuan yang curang.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Sabda-Mu adalah pelita bagi langkahku, cahaya untuk menerangi jalanku.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Yang kujanjikan dengan sumpah akan kutepati, untuk berpegang pada keputusan-Mu yang adil.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Aku sangat sengsara, ya TUHAN, jagalah hidupku sesuai dengan janji-Mu.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Terimalah doa syukurku, ya TUHAN, dan ajarilah aku hukum-hukum-Mu.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Aku selalu mempertaruhkan nyawaku, tetapi aku tidak melupakan hukum-Mu.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Orang jahat memasang perangkap bagiku, tetapi aku tidak menyimpang dari keputusan-Mu.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Perintah-Mu adalah pusakaku untuk selamanya, yang membuat hatiku gembira.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Aku berhasrat mentaati ketetapan-Mu sampai akhir hidupku.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Aku mencintai hukum-hukum-Mu, kubenci orang yang tidak sepenuhnya setia kepada-Mu.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Engkaulah pembela dan pelindungku, aku berharap pada janji-Mu.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Hai orang jahat, menjauhlah dari aku! Aku mau mentaati perintah Allahku.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Kuatkanlah aku sesuai dengan janji-Mu agar aku hidup, jangan biarkan aku dikecewakan dalam harapanku.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Topanglah aku supaya aku selamat, dan selalu memperhatikan perintah-Mu.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Engkau menolak orang yang menyimpang dari ketetapan-Mu, sia-sia saja tipu muslihat mereka.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Semua orang jahat Kauanggap sebagai sampah, sebab itu aku mencintai peraturan-peraturan-Mu.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Aku gemetar karena takut kepada-Mu, hatiku gentar terhadap keputusan-Mu.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Aku sudah melakukan yang adil dan benar, janganlah menyerahkan aku ke tangan lawan.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Berjanjilah bahwa Engkau akan menolong aku, jangan biarkan aku ditindas orang-orang angkuh.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mataku pedih menunggu bantuan-Mu yang menyelamatkan, kunantikan pembebasan yang Kaujanjikan.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Perlakukanlah aku sesuai dengan kasih-Mu, dan ajarlah aku ketetapan-Mu.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Aku hamba-Mu, buatlah aku mengerti, supaya aku memahami perintah-Mu.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
TUHAN, sudah tiba saatnya Engkau bertindak, sebab orang-orang melanggar hukum-Mu.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Perintah-perintah-Mu kucintai melebihi emas, melebihi emas murni.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Sebab itu aku hidup sesuai dengan semua petunjuk-Mu; kelakuan yang serong kubenci.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Peraturan-peraturan-Mu sungguh mengagumkan, maka kutaati dengan sepenuh hati.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Bila dijelaskan, ajaran-Mu memberi terang, memberi pengertian kepada orang sederhana.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Napasku terengah-engah, karena merindukan perintah-Mu.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Berpalinglah kepadaku dan kasihanilah aku, seperti Kaukasihani orang yang mencintai-Mu.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Teguhkanlah langkahku sesuai dengan janji-Mu, jangan biarkan aku dikuasai kejahatan.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Bebaskanlah aku dari orang-orang yang menindas aku, supaya aku dapat mentaati peraturan-Mu.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Berkatilah aku dengan kehadiran-Mu, dan ajarilah aku ketetapan-Mu.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Air mataku mengalir seperti sungai, karena hukum-Mu tidak ditaati.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Engkau adil, ya TUHAN, semua hukum-Mu tepat.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Perintah-perintah yang Kauberikan adil dan dapat diandalkan.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Kemarahanku membara dalam diriku karena musuhku melupakan ajaran-Mu.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Janji-Mu teguh dan dapat dipercaya, aku sangat mencintainya.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Aku ini kecil dan hina, tetapi aku tidak mengabaikan ajaran-Mu.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Keadilan-Mu bertahan selama-lamanya, dan hukum-Mu selalu benar.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Aku ditimpa kesesakan dan kesusahan, tetapi ketetapan-Mu menggembirakan hatiku.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Peraturan-Mu selalu adil; berilah aku pengertian supaya aku hidup.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Dengan segenap hati aku berseru kepada-Mu; jawablah aku ya TUHAN, aku mau mentaati perintah-Mu.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Aku berseru kepada-Mu; selamatkanlah aku, aku mau berpegang pada peraturan-Mu.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Pagi-pagi aku bangun dan berseru minta tolong; aku berharap kepada janji-Mu.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Sepanjang malam aku berjaga, untuk merenungkan ajaran-Mu.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Dengarlah aku karena kasih-Mu, ya TUHAN, jagalah hidupku karena keadilan-Mu.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Orang yang mengejar aku sudah dekat, mereka bermaksud jahat dan tidak mengindahkan hukum-Mu.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Tetapi Engkau dekat, ya TUHAN, segala perintah-Mu benar.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Sejak dahulu aku tahu dari ajaran-ajaran-Mu, bahwa Engkau menetapkannya untuk selama-lamanya.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Lihatlah penderitaanku dan selamatkanlah aku, sebab aku tidak mengabaikan hukum-Mu.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Belalah perkaraku dan bebaskanlah aku; selamatkanlah aku sesuai dengan janji-Mu.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Orang jahat tak akan diselamatkan, karena tidak mentaati ketetapan-Mu.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Sungguh besar belas kasihan-Mu, ya TUHAN, selamatkanlah aku sesuai dengan keadilan-Mu.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Banyak orang memusuhi dan mengejar aku, tapi aku tidak mengabaikan peraturan-Mu.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Aku benci melihat pengkhianat-pengkhianat itu, sebab mereka tidak mengikuti ajaran-Mu.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Lihatlah betapa aku mencintai perintah-Mu, ya TUHAN, selamatkanlah aku karena kasih-Mu.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Semua sabda-Mu benar, segala hukum-Mu yang adil tetap selama-lamanya.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Orang-orang berkuasa mengejar aku tanpa alasan, tetapi hanya hukum-Mu yang kutakuti.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Janji-Mu membuat aku gembira, seperti seorang yang menemukan harta.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Segala dusta kubenci, tetapi hukum-Mu kucintai.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Aku terus-menerus bersyukur kepada-Mu, karena hukum-Mu yang adil.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Orang yang mencintai hukum-Mu aman dan tentram, tak ada yang dapat merintangi mereka.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Aku menunggu keselamatan daripada-Mu, TUHAN, perintah-perintah-Mu kulakukan.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Aku mentaati peraturan-peraturan-Mu, dan mencintainya dengan segenap hati.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Aku mematuhi perintah dan petunjuk-Mu, sebab Engkau melihat segala perbuatanku.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Semoga seruanku sampai kepada-Mu, ya TUHAN, berilah aku pengertian, sesuai dengan janji-Mu.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Biarlah permohonanku sampai kepada-Mu, selamatkanlah aku sesuai dengan janji-Mu.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Aku mau memuji Engkau selalu, sebab Engkau mengajar aku ketetapan-Mu.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Aku ingin menyanyi tentang janji-Mu, sebab segala perintah-Mu adil.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Semoga Engkau selalu rela menolong aku, sebab aku memilih untuk mengikuti peraturan-Mu.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Hatiku merindukan keselamatan daripada-Mu, hukum-Mu menggembirakan hatiku.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Biarlah aku hidup, supaya aku memuji Engkau, semoga ketetapan-ketetapan menolong aku.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Aku sesat seperti domba yang hilang, maka datanglah, dan carilah hamba-Mu ini, sebab aku tidak mengabaikan perintah-perintah-Mu.

< Masalimo 119 >