< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Wohl denen, deren Weg unsträflich ist, die da wandeln nach dem Gesetze des HERRN!
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Wohl denen, die seine Zeugnisse beobachten, die ihn von ganzem Herzen suchen,
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
die auch kein Unrecht getan haben, die auf seinen Wegen gegangen sind!
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Du hast deine Befehle gegeben, daß man sie fleißig beobachte.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
O daß meine Wege dahin zielten, deine Satzungen zu befolgen!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Dann werde ich nicht zuschanden, wenn ich auf alle deine Gebote sehe.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Ich werde dir mit aufrichtigem Herzen danken, wenn ich die Verordnungen deiner Gerechtigkeit lerne.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Deine Satzungen will ich befolgen; verlaß mich nicht ganz und gar!
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Wie wird ein Jüngling seinen Weg unsträflich gehen? Wenn er sich hält nach deinem Wort!
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Ich habe dich von ganzem Herzen gesucht; laß mich nicht abirren von deinen Geboten!
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Ich habe dein Wort in meinem Herzen geborgen, auf daß ich nicht an dir sündige.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Gelobt seist du, o HERR! Lehre mich deine Satzungen.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Mit meinen Lippen zähle ich alle Verordnungen deines Mundes auf.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Ich freue mich des Weges deiner Zeugnisse, wie über lauter Reichtümer.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Ich will über deine Wege nachsinnen und auf deine Pfade achten.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Ich habe meine Lust an deinen Satzungen und vergesse deines Wortes nicht.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Gewähre deinem Knecht, daß ich lebe und dein Wort befolge!
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Öffne meine Augen, daß ich erblicke die Wunder in deinem Gesetz!
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Ich bin ein Gast auf Erden; verbirg deine Gebote nicht vor mir!
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Meine Seele ist zermalmt vor Sehnsucht nach deinen Verordnungen allezeit.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Du hast die Übermütigen gescholten, die Verfluchten, welche von deinen Geboten abirren.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Wälze Schimpf und Schande von mir ab; denn ich habe deine Zeugnisse bewahrt!
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Sogar Fürsten sitzen und bereden sich wider mich; aber dein Knecht sinnt über deine Satzungen.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Ja, deine Zeugnisse sind meine Freude; sie sind meine Ratgeber.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Meine Seele klebt am Staube; belebe mich nach deiner Verheißung!
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Ich habe meine Wege erzählt, und du hast mir geantwortet; lehre mich deine Satzungen!
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Laß mich den Weg deiner Befehle verstehen und deine Wunder betrachten!
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Meine Seele weint vor Kummer; richte mich auf nach deinem Wort!
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Entferne von mir den falschen Weg und begnadige mich mit deinem Gesetz!
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Ich habe den Weg der Wahrheit erwählt und deine Verordnungen vor mich hingestellt.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
HERR, ich hange an deinen Zeugnissen; laß mich nicht zuschanden werden!
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Ich laufe den Weg deiner Gebote; denn du machst meinem Herzen Raum.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Zeige mir, HERR, den Weg deiner Satzungen, daß ich ihn bewahre bis ans Ende.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Unterweise mich, so will ich dein Gesetz bewahren und es von ganzem Herzen befolgen.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Laß mich wandeln auf dem Pfad deiner Gebote; denn ich habe Lust daran.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Neige mein Herz zu deinen Zeugnissen und nicht zur Habsucht!
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Wende meine Augen ab, daß sie nicht nach Eitlem sehen; erquicke mich auf deinen Wegen!
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Erfülle an deinem Knechte deine Verheißung, die denen gilt, die dich fürchten.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Wende die Beschimpfung von mir ab, die ich fürchte; denn deine Verordnungen sind gut!
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Siehe, ich sehne mich nach deinen Befehlen; erquicke mich durch deine Gerechtigkeit!
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Deine Gnade, o HERR, komme über mich, dein Heil nach deinem Wort!
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Damit ich dem antworten kann, der mich schmäht; denn ich verlasse mich auf dein Wort.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Und entziehe nicht allzusehr meinem Munde das Wort der Wahrheit; denn ich harre auf deine Verordnungen!
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Und ich will dein Gesetz stets bewahren, immer und ewiglich.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Und ich möchte auf weitem Raum wandeln; denn ich habe deine Befehle erforscht.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Und ich will von deinen Zeugnissen reden vor Königen und mich nicht schämen.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Und ich will mich an deinen Befehlen vergnügen; denn ich liebe sie.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Und ich will meine Hände nach deinen Befehlen ausstrecken, weil ich sie liebe, und will nachdenken über deine Satzungen.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Gedenke des Wortes an deinen Knecht, auf welches du mich hoffen ließest!
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Das ist mein Trost in meinem Elend, daß dein Wort mich erquickt.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Die Übermütigen haben mich arg verspottet; dennoch bin ich von deinem Gesetz nicht abgewichen.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Ich gedachte deiner Verordnungen, HERR, die von Ewigkeit her sind, und das tröstete mich.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Zornglut hat mich ergriffen wegen der Gottlosen, die dein Gesetz verlassen.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Deine Satzungen sind meine Lieder geworden im Hause meiner Wallfahrt.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
HERR, des Nachts habe ich an deinen Namen gedacht und dein Gesetz bewahrt.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Das ist mir zuteil geworden, daß ich deine Befehle befolgen darf.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Ich sage: Das ist mein Teil, o HERR, die Beobachtung deiner Worte!
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Ich flehe von ganzem Herzen um deine Gunst: Sei mir gnädig, wie du verheißen hast!
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Als ich meine Wege überlegte, wandte ich meine Füße zu deinen Zeugnissen.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Ich habe mich beeilt und nicht gesäumt, deine Gebote zu befolgen.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Als die Schlingen der Gottlosen mich umgaben, vergaß ich deines Gesetzes nicht.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Mitten in der Nacht stehe ich auf, dir zu danken für die Verordnungen deiner Gerechtigkeit.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Ich bin verbunden mit allen, die dich fürchten, und die deine Befehle befolgen.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
HERR, die Erde ist voll deiner Gnade; lehre mich deine Satzungen!
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Du hast deinem Knechte wohlgetan, o HERR, nach deinem Wort.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Lehre mich rechte Einsicht und Verständnis; denn ich vertraue deinen Befehlen.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Ehe ich gedemütigt ward, irrte ich, nun aber befolge ich dein Wort.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Du bist gut und wohltätig; lehre mich deine Satzungen!
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Die Stolzen haben mich mit Lügen besudelt; ich beobachte von ganzem Herzen deine Befehle.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Ihr Herz ist stumpf wie von Fett; ich aber vergnüge mich an deinem Gesetz.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Es war gut für mich, daß ich gedemütigt wurde, auf daß ich deine Satzungen lernte.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Das Gesetz deines Mundes ist besser für mich als Tausende von Gold und Silberstücken.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Deine Hände haben mich gemacht und bereitet; gib mir Verstand, daß ich deine Befehle lerne!
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Die dich fürchten, werden mich sehen und sich freuen, daß ich auf dein Wort gewartet habe.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
HERR, ich weiß, daß deine Verordnungen gerecht sind und daß du mich in Treue gedemütigt hast.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Laß doch deine Gnade mir zum Trost gereichen, wie du deinem Knechte zugesagt hast!
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Laß mir deine Barmherzigkeit widerfahren, daß ich lebe! Denn dein Gesetz ist meine Lust.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Laß die Stolzen zuschanden werden, weil sie mir mit Lügen Unrecht getan; ich aber denke über deine Befehle nach.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Mir wird zufallen, wer dich fürchtet und deine Zeugnisse anerkennt.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Mein Herz soll sich gänzlich an deine Satzungen halten, damit ich nicht zuschanden werde.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Meine Seele schmachtet nach deinem Heil; ich harre auf dein Wort.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Meine Augen schmachten nach deinem Wort und fragen: Wann wirst du mich trösten?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Bin ich auch geworden wie ein Schlauch im Rauch, so habe ich doch deiner Satzungen nicht vergessen.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Wieviel sind noch der Tage deines Knechtes? Wann willst du an meinen Verfolgern das Urteil vollziehen?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Die Übermütigen haben mir Gruben gegraben, sie, die sich nicht nach deinem Gesetze richten.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Alle deine Gebote sind Wahrheit; sie aber verfolgen mich mit Lügen; hilf mir!
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Sie hätten mich fast umgebracht auf Erden; dennoch verließ ich deine Befehle nicht.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Erhalte mich am Leben nach deiner Gnade, so will ich die Zeugnisse deines Mundes bewahren.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Auf ewig, o HERR, steht dein Wort im Himmel fest;
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
von einem Geschlecht zum andern währt deine Treue! Du hast die Erde gegründet, und sie steht;
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
nach deinen Ordnungen stehen sie noch heute; denn es muß dir alles dienen!
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Wäre dein Gesetz nicht meine Lust gewesen, so wäre ich vergangen in meinem Elend.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Ich will deine Befehle auf ewig nicht vergessen; denn durch sie hast du mich belebt.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Ich bin dein; rette mich, denn ich habe deine Befehle gesucht!
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Die Gottlosen lauern mir auf, um mich zu verderben; aber ich merke auf deine Zeugnisse.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Von aller Vollkommenheit habe ich ein Ende gesehen; aber dein Gebot ist unbeschränkt.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Wie habe ich dein Gesetz so lieb! Ich denke darüber nach den ganzen Tag.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Dein Gebot macht mich weiser als meine Feinde; denn es bleibt ewiglich bei mir.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Ich bin verständiger geworden als alle meine Lehrer, denn deine Zeugnisse sind mein Sinnen.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Ich bin einsichtiger als die Alten; denn ich achte auf deine Befehle.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Von allen schlechten Wegen habe ich meine Füße abgehalten, um dein Wort zu befolgen.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Von deinen Verordnungen bin ich nicht abgewichen; denn du hast mich gelehrt.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Wie süß ist deine Rede meinem Gaumen, mehr denn Honig meinem Mund!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Von deinen Befehlen werde ich verständig; darum hasse ich jeden Lügenpfad.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Dein Wort ist meines Fußes Leuchte und ein Licht für meinen Pfad.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Ich habe geschworen und werde es halten, daß ich die Verordnungen deiner Gerechtigkeit bewahren will.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Ich bin tief gebeugt; HERR, erquicke mich nach deinem Wort!
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
HERR, laß dir wohlgefallen die freiwilligen Opfer meines Mundes und lehre mich deine Verordnungen!
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Meine Seele ist beständig in meiner Hand, und ich vergesse deines Gesetzes nicht.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Die Gottlosen haben mir eine Schlinge gelegt; aber ich bin von deinen Befehlen nicht abgeirrt.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Deine Zeugnisse sind mein ewiges Erbe; denn sie sind meines Herzens Wonne.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Ich habe mein Herz geneigt, deine Satzungen auf ewig zu erfüllen.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Ich hasse die Unentschiedenen; aber dein Gesetz habe ich lieb.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Du bist mein Schirm und mein Schild; ich harre auf dein Wort.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Weichet von mir, ihr Übeltäter, daß ich die Gebote meines Gottes befolge!
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Unterstütze mich nach deiner Verheißung, daß ich lebe und nicht zuschanden werde mit meiner Hoffnung!
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Stärke du mich, so ist mir geholfen und ich werde mich an deinen Satzungen stets ergötzen!
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Du wirst alle zu leicht erfinden, die von deinen Satzungen abweichen; denn eitel Betrug ist ihre Täuschung.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Wie Schlacken räumst du alle Gottlosen von der Erde fort; darum liebe ich deine Zeugnisse.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Mein Fleisch schaudert aus Furcht vor dir, und ich habe Ehrfurcht vor deinen Verordnungen!
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Ich habe Recht und Gerechtigkeit geübt; überlaß mich nicht meinen Unterdrückern!
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Stehe ein zum Besten deines Knechtes, daß mich die Übermütigen nicht unterdrücken!
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Meine Augen schmachten nach deinem Heil und nach dem Wort deiner Gerechtigkeit.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Handle mit deinem Knecht nach deiner Gnade und lehre mich deine Satzungen!
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Ich bin dein Knecht; unterweise mich, daß ich deine Zeugnisse verstehe!
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Es ist Zeit, daß der HERR handle; sie haben dein Gesetz gebrochen!
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Darum liebe ich deine Befehle mehr als Gold und als feines Gold;
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
darum lobe ich mir alle deine Gebote und hasse jeden trügerischen Pfad.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Wunderbar sind deine Zeugnisse; darum bewahrt sie meine Seele.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Die Erschließung deiner Worte erleuchtet und macht die Einfältigen verständig.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Begierig öffne ich meinen Mund; denn mich verlangt nach deinen Befehlen.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Wende dich zu mir und sei mir gnädig nach dem Rechte derer, die deinen Namen lieben.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Mache meine Schritte fest durch dein Wort und laß kein Unrecht über mich herrschen!
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Erlöse mich von der Bedrückung durch Menschen, so will ich deine Befehle befolgen!
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Laß dein Angesicht leuchten über deinen Knecht und lehre mich deine Satzungen!
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Tränenströme fließen aus meinen Augen, weil man dein Gesetz nicht befolgt.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
HERR, du bist gerecht, und deine Verordnungen sind richtig!
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Du hast deine Zeugnisse gerecht und sehr treu abgefaßt.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Mein Eifer hat mich verzehrt, weil meine Feinde deine Worte vergessen haben.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Deine Rede ist wohlgeläutert, und dein Knecht hat sie lieb.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Ich bin gering und verachtet; deine Befehle habe ich nicht vergessen.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Deine Gerechtigkeit ist auf ewig gerecht, und dein Gesetz ist Wahrheit.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Angst und Not haben mich betroffen; aber deine Befehle sind meine Lust.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Deine Zeugnisse sind auf ewig gerecht; unterweise mich, so werde ich leben!
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Ich rufe von ganzem Herzen: HERR, erhöre mich; deine Satzungen will ich befolgen!
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Ich rufe zu dir; errette mich, so will ich deine Zeugnisse bewahren!
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Vor der Morgendämmerung komme ich und schreie; ich harre auf dein Wort.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Meine Augen kommen den Nachtwachen zuvor, daß ich über deine Reden nachdenke.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Höre meine Stimme nach deiner Gnade, o HERR, erquicke mich nach deinem Recht!
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Die dem Laster nachjagen, sind nah; von deinem Gesetz sind sie fern.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Du bist nahe, o HERR, und alle deine Gebote sind wahr.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Längst weiß ich aus deinen Zeugnissen, daß du sie auf ewig gegründet hast.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Siehe mein Elend an und errette mich; denn ich habe deines Gesetzes nicht vergessen!
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Führe meine Sache und erlöse mich; erquicke mich durch dein Wort!
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Das Heil ist fern von den Gottlosen; denn sie fragen nicht nach deinen Satzungen.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Deine Barmherzigkeit ist groß, o HERR; erquicke mich nach deinen Verordnungen!
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Meiner Verfolger und Widersacher sind viele; dennoch habe ich mich nicht von deinen Zeugnissen abgewandt.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Wenn ich die Abtrünnigen ansehe, so ekelt mir, weil sie dein Wort nicht beachten.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Siehe, ich liebe deine Befehle; o HERR, erquicke mich nach deiner Gnade!
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Die Summe deines Wortes ist Wahrheit, und alle Verordnungen deiner Gerechtigkeit bleiben ewig.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Fürsten verfolgen mich ohne Ursache; aber vor deinem Wort fürchtet sich mein Herz.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Ich freue mich über dein Wort wie einer, der große Beute findet.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Ich hasse Lügen und habe Greuel daran; aber dein Gesetz habe ich lieb.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Ich lobe dich des Tages siebenmal wegen der Ordnungen deiner Gerechtigkeit.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Großen Frieden haben, die dein Gesetz lieben, und nichts bringt sie zu Fall.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Ich warte auf dein Heil, o HERR, und erfülle deine Befehle.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Meine Seele bewahrt deine Zeugnisse und liebt sie sehr.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Ich habe deine Befehle und deine Zeugnisse bewahrt; denn alle meine Wege sind vor dir.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
HERR, laß mein Schreien vor dich kommen; unterweise mich nach deinem Wort!
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Laß mein Flehen vor dich kommen; errette mich nach deiner Verheißung!
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Meine Lippen sollen überfließen von Lob, wenn du mich deine Satzungen lehrst.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Meine Zunge soll deine Rede singen; denn alle deine Gebote sind gerecht.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Deine Hand komme mir zu Hilfe; denn ich habe deine Befehle erwählt.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Ich habe Verlangen nach deinem Heil, o HERR, und dein Gesetz ist meine Lust.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Meine Seele soll leben und dich loben, und deine Verordnungen seien meine Hilfe!
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Ich bin verirrt wie ein verlorenes Schaf; suche deinen Knecht! Denn deine Gebote habe ich nicht vergessen!

< Masalimo 119 >