< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Wohl denen, deren Weg unsträflich ist, die nach dem Gesetze Jahwes wandeln.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Wohl denen, die seine Zeugnisse beachten, ihn von ganzem Herzen suchen,
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
auch keinen Frevel verübt haben, sondern auf seinen Wegen gewandelt sind.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Du hast deine Befehle verordnet, daß man sie eifrig beobachten soll.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Möchte doch mein Wandel fest sein, daß ich deine Satzungen beobachte.
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Dann werde ich nicht zu Schanden werden, wenn ich auf alle deine Gebote blicke.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Ich will dich mit redlichem Herzen preisen, wenn ich deine gerechten Ordnungen erlerne.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Deine Satzungen will ich beobachten: verlaß mich nicht völlig!
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Wodurch kann ein Jüngling seinen Pfad rein erhalten? Indem er deine Satzungen beobachtet gemäß deinem Worte.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Von ganzem Herzen suche ich dich: laß mich nicht abirren von deinen Geboten!
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
In meinem Herzen berge ich dein Wort, damit ich mich nicht an dir versündige.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Gepriesen seist du, Jahwe; lehre mich deine Satzungen!
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Mit meinen Lippen verkünde ich alle Ordnungen deines Mundes.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
An dem Wege, den deine Zeugnisse gebieten, freue ich mich wie über irgend welchen Reichtum.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Über deine Befehle will ich sinnen und deine Pfade betrachten.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
An deinen Satzungen will ich mich ergötzen, dein Wort nicht vergessen.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Thue deinem Knechte wohl, daß ich lebe, so will ich dein Wort beobachten.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Decke meine Augen auf, damit ich erschaue Wunder aus deinem Gesetz.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Ein Gast bin ich auf Erden; verbirg deine Gebote nicht vor mir.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Meine Seele reibt sich auf vor Verlangen nach deinen Ordnungen zu jeder Zeit.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Du hast die verfluchten Übermütigen bedroht, die von deinen Geboten abirrten.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Wälze Schmach und Verachtung von mir ab, denn ich habe deine Zeugnisse beachtet.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Haben auch Fürsten sich hingesetzt, sich wider mich beredet - dein Knecht sinnt über deine Satzungen nach.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Ja, deine Zeugnisse sind mein Ergötzen, deine Befehle sind meine Berater.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Meine Seele klebt am Staube; belebe mich gemäß deinem Worte.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Ich erzählte meine Wege, da erhörtest du mich; lehre mich deine Satzungen.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Laß mich den Weg, den deine Befehle gebieten, verstehen, so will ich über deine Wunder nachsinnen.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Meine Seele thränt vor Kummer; richte mich auf gemäß deinem Worte.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Den Weg der Lüge halte fern von mir und begnadige mich mit deinem Gesetze.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Den Weg der Treue habe ich erwählt, deine Ordnungen vor mich hingestellt.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Ich hänge an deinen Zeugnissen; Jahwe, laß mich nicht zu Schanden werden!
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Den Weg deiner Gebote will ich laufen, denn du machst mir das Herz weit.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Lehre mich, Jahwe, den Weg deiner Satzungen, damit ich ihn bis zuletzt beachte.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Laß mich einsichtig werden, damit ich dein Gesetz beachte und von ganzem Herzen halte.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Laß mich auf dem Pfade deiner Gebote einhergehen, denn an ihm habe ich Gefallen.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Neige mein Herz deinen Zeugnissen zu und nicht dem ungerechten Gewinn.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Ziehe meine Augen davon ab, daß sie nach Eitlem schauen; belebe mich auf deinen Wegen.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Erfülle deinem Knechte deine Verheißung, die der Furcht vor dir gegeben ist.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Laß die Schmach, die ich fürchte, an mir vorübergehen; denn deine Ordnungen sind gut.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Fürwahr, mich verlangt nach deinen Befehlen; belebe mich durch deine Gerechtigkeit.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Mögen deine Gnadenerweisungen, Jahwe, über mich kommen, dein Heil gemäß deiner Verheißung,
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
daß ich dem, der mich lästert, etwas antworten kann; denn ich vertraue auf dein Wort.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Und entziehe meinem Munde nicht völlig das Wort der Wahrheit, denn auf deine Gerichte harre ich.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Und ich will dein Gesetz beständig beobachten, immer und ewig,
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
so werde ich in weitem Raume wandeln, denn ich habe deine Befehle gesucht.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Und ich will von deinen Zeugnissen vor Königen reden und mich nicht schämen.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Ich ergötze mich an deinen Geboten, die ich lieb gewonnen habe.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Und ich erhebe meine Hände zu deinen Geboten, die ich lieb gewonnen, und will nachsinnen über deine Satzungen.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Gedenke des Worts an deinen Knecht, dieweil du mich harren ließest.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Das ist mein Trost in meinem Elend, daß mich dein Wort neu belebte.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Übermütige haben mich gar sehr verspottet; von deinem Gesetze bin ich nicht abgewichen.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Ich gedachte deiner Gerichte von Uralters her, Jahwe, da tröstete ich mich.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Zornglut hat mich erfaßt wegen der Gottlosen, die dein Gesetz verlassen.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Anlaß zu Lobpreis wurden mir deine Satzungen da, wo ich als Fremdling weile.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Ich gedachte des Nachts an deinen Namen, Jahwe, und beobachtete dein Gesetz.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Solches ward mir zu teil, denn ich habe deine Befehle beachtet.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Ich sprach: Mein Teil ist, Jahwe, deine Worte zu beobachten.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Von ganzem Herzen habe ich deine Gunst gesucht; sei mir gnädig gemäß deiner Verheißung.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Ich überdachte meine Wege und lenkte meine Füße deinen Zeugnissen zu.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Ich eilte und zauderte nicht, deine Gebote zu beobachten.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Die Stricke der Gottlosen umgaben mich; dein Gesetz habe ich nicht vergessen.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Mitten in der Nacht erhebe ich mich, dir wegen deiner gerechten Ordnungen zu danken.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Ich bin ein Genosse aller derer, die dich fürchten und deine Befehle beobachten.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Von deiner Gnade, Jahwe, ist die Erde voll; lehre mich deine Satzungen.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Du hast deinem Knechte Gutes erwiesen, Jahwe, gemäß deinem Worte.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Rechte Einsicht und Erkenntnis lehre mich, denn ich vertraue auf deine Gebote.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Bevor ich gedemütigt ward, ging ich irre, nun aber beobachte ich dein Wort.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Gütig bist du und thust wohl; lehre mich deine Satzungen.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Die Übermütigen haben mir Lüge angedichtet; ich aber beachte von ganzem Herzen deine Befehle.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Stumpf wie Fett ist ihr Sinn; ich aber ergötze mich an deinem Gesetze.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Es war heilsam für mich, daß ich gedemütigt ward, damit ich deine Satzungen lernte.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Das Gesetz deines Mundes ist köstlicher für mich, als Tausende Goldes und Silbers.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Deine Hände haben mich geschaffen und bereiteten mich; laß mich einsichtig werden, damit ich deine Gebote lerne.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Die dich fürchten, werden mich sehen und sich freuen, denn ich harre auf dein Wort.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Ich weiß, Jahwe, daß deine Gerichte gerecht sind, und daß du in Treue mich gedemütigt hast.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Möchte doch deine Gnade dienen, mich zu trösten, nach deiner Verheißung an deinen Knecht.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Möchte dein Erbarmen über mich kommen, daß ich lebe, denn dein Gesetz ist mein Ergötzen.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Laß die Übermütigen zu Schanden werden, weil sie mich ohne Grund gebeugt haben; ich sinne nach über deine Befehle.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Mir mögen sich zuwenden, die dich fürchten und die deine Zeugnisse kennen.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Möge mein Herz in deinen Satzungen unsträflich sein, damit ich nicht zu Schanden werde.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Meine Seele schmachtet nach deinem Heil; ich harre auf dein Wort.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Meine Augen schmachten nach deinem Wort und fragen: “Wann wirst du mich trösten?”
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Denn ich gleiche einem Schlauch im Rauche; deine Satzungen habe ich nicht vergessen.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Wie viel sind der Lebenstage deines Knechts? Wann wirst du an meinen Verfolgern das Gericht vollstrecken?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Die Übermütigen haben mir Gruben gegraben, sie, die deinem Gesetze nicht entsprechen.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Alle deine Gebote sind Wahrheit. Ohne Grund verfolgen sie mich: hilf mir!
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Gar leicht hätten sie mich auf Erden aufgerieben, obgleich ich von deinen Befehlen nicht gelassen habe.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Gemäß deiner Gnade erhalte mich am Leben, damit ich das Zeugnis deines Mundes beobachte.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Auf ewig, Jahwe, steht dein Wort im Himmel fest.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Durch alle Geschlechter währt deine Treue; du hast die Erde hingestellt und sie blieb stehen.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Nach deinen Ordnungen stehen sie noch heut, denn das alles sind deine Diener.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Wenn nicht dein Gesetz mein Ergötzen gewesen wäre, so wäre ich vergangen in meinem Elend.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Nimmermehr will ich deine Befehle vergessen, denn durch sie hast du mich am Leben erhalten.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Dein bin ich, hilf mir! denn ich suche deine Befehle.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Die Gottlosen haben auf mich gelauert, mich umzubringen. Ich merke auf deine Zeugnisse.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Von allem sonstigen Umfang habe ich ein Ende gesehen: überaus weitreichend ist dein Gebot.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Wie liebe ich dein Gesetz! Allezeit ist es mein Sinnen.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Dein Gebot macht mich weiser, als es meine Feinde sind, denn es ist für immer mein.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Ich bin klüger als alle, die mich gelehrt haben, denn deine Zeugnisse sind mein Sinnen.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Ich bin einsichtiger als Greise, denn ich beachte deine Befehle.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Von jedem schlimmen Pfade hielt ich meine Füße zurück, um dein Wort zu beobachten.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Von deinen Ordnungen wich ich nicht, denn du unterwiesest mich.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Wie süß sind meinem Gaumen deine Verheißungen, süßer als Honig meinem Munde.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Durch deine Befehle werde ich einsichtig, darum hasse ich jeden Lügenpfad.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Dein Wort ist meines Fußes Leuchte und ein Licht für meinen Pfad.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Ich habe geschworen und hielt es, deine gerechten Ordnungen zu beobachten.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Ich bin schwer gebeugt; Jahwe, belebe mich nach deinem Worte.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Laß dir, Jahwe, die freiwilligen Opfer meines Mundes gefallen und lehre mich deine Ordnungen.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Ich trage mein Leben beständig in meiner Hand und habe dein Gesetz nicht vergessen.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Die Gottlosen haben mir eine Schlinge gelegt, und von deinen Befehlen bin ich nicht abgeirrt.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Ich habe deine Zeugnisse für immer zum Besitz erhalten, denn sie sind die Wonne meines Herzens.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Ich neige mein Herz dazu, nach deinen Satzungen zu thun, für immer, bis zuletzt.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Zwiespältige hasse ich und dein Gesetz habe ich lieb.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Du bist mein Schirm und mein Schild, auf dein Wort harre ich.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Weicht von mir, ihr Bösewichter, daß ich die Gebote meines Gottes beachte.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Stütze mich deiner Verheißung gemäß, daß ich lebe, und laß mich mit meiner Hoffnung nicht zu Schanden werden.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Stärke mich, daß mir geholfen werde, so will ich mich an deinen Satzungen beständig ergötzen.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Du verwirfst alle, die sich von deinen Satzungen verirren, denn fruchtlos ist ihr Trügen.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Für Schlacken erachtest du alle Gottlosen auf Erden; darum liebe ich deine Zeugnisse.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Mein Leib schaudert aus Furcht vor dir, und ich bange vor deinen Gerichten.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Ich habe Recht und Gerechtigkeit geübt; überlasse mich nicht meinen Unterdrückern.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Tritt für deinen Knecht zu seinem Heile ein; laß die Übermütigen mich nicht unterdrücken.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Meine Augen schmachten nach deiner Hilfe und nach deinem gerechten Spruche.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Verfahre mit deinem Knechte deiner Gnade gemäß und lehre mich deine Satzungen.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Dein Knecht bin ich; laß mich einsichtig werden, damit ich deine Zeugnisse erkenne.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Zeit ist's zu handeln für Jahwe; sie haben dein Gesetz gebrochen.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Darum liebe ich deine Gebote mehr als Gold und als Feingold.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Darum halte ich alle deine Befehle für recht; jeden Lügenpfad hasse ich.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Wunderbar sind deine Zeugnisse; darum hat sie meine Seele beachtet.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Das Thor deiner Worte leuchtet, macht die Einfältigen verständig.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Ich sperre meinen Mund auf und lechze, denn mich verlangt nach deinen Geboten.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Wende dich zu mir und sei mir gnädig, nach dem Rechte derer, die deinen Namen lieben.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Festige meine Tritte in deinem Wort und laß keinerlei Böses über mich herrschen.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Erlöse mich von Menschenbedrückung, damit ich deine Befehle halte.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Laß deinem Knechte dein Antlitz leuchten und lehre mich deine Satzungen.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Von Wasserbächen strömten meine Augen über, weil sie dein Gesetz nicht beobachtet haben.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Du bist gerecht, Jahwe, und deine Ordnungen sind recht.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Du hast in Gerechtigkeit deine Zeugnisse geboten und in Treue überaus.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Mich hat mein Eifer verzehrt, weil meine Bedränger deine Worte vergaßen.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Dein Wort ist überaus geläutert, und dein Knecht hat es lieb.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Ich bin klein und verachtet; deine Befehle vergaß ich nicht.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Deine Gerechtigkeit ist Gerechtigkeit für immer, und dein Gesetz ist Wahrheit.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Not und Drangsal haben mich betroffen; deine Gebote sind mein Ergötzen.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Gerechtigkeit sind deine Zeugnisse für immer; laß mich einsichtig werden, damit ich lebe.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Ich rufe von ganzem Herzen: Erhöre mich, Jahwe! Deine Satzungen will ich beachten.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Ich rufe dich, hilf mir, damit ich deine Satzungen beobachte.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Ich komme der Morgendämmerung zuvor und schreie, indem ich harre auf dein Wort.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Meine Augen kommen den Nachtwachen zuvor, um über dein Wort nachzusinnen.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Höre meine Stimme gemäß deiner Gnade; Jahwe, deinen Ordnungen gemäß belebe mich.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Nahe sind, die mich mit Arglist verfolgen, sich von deinem Gesetze fernhalten;
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
aber du bist nahe, Jahwe, und alle deine Gebote sind Wahrheit.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Von längst her weiß ich aus deinen Zeugnissen, daß du sie für ewig gegründet hast.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Siehe mein Elend und reiße mich heraus, denn dein Gesetz vergaß ich nicht.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Führe meine Sache und erlöse mich; deiner Verheißung gemäß belebe mich.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Den Gottlosen bleibt die Hilfe fern, denn sie fragen nichts nach deinen Satzungen.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Deine Barmherzigkeit ist groß, Jahwe; deinen Ordnungen gemäß belebe mich.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Zahlreich sind meine Verfolger und Bedränger; von deinen Zeugnissen wich ich nicht ab.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Ich gewahrte Abtrünnige und empfand Ekel - solche, die dein Wort nicht beobachteten.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Sieh, daß ich deine Befehle liebe; Jahwe, deiner Gnade gemäß belebe mich.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Die Summe deines Worts ist Treue, und auf ewig währt alle deine gerechte Ordnung.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Fürsten verfolgen mich ohne Ursache, und vor deinem Worte bebt mein Herz.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Ich bin erfreut über deine Verheißung wie einer, der große Beute fand.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Lüge hasse und verabscheue ich; dein Gesetz habe ich lieb.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Siebenmal des Tages preise ich dich wegen deiner gerechten Ordnungen.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Großes Heil wird denen, die dein Gesetz lieb haben, und es giebt für sie keinen Anstoß.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Ich hoffe auf deine Hilfe, Jahwe; habe ich doch nach deinen Geboten gethan.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Meine Seele hat deine Zeugnisse beobachtet, und ich gewann sie überaus lieb.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Ich habe deine Befehle und deine Zeugnisse beobachtet, denn alle meine Wege sind dir gegenwärtig.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Mein Jammern komme nahe vor dein Angesicht, Jahwe; deinem Worte gemäß laß mich einsichtig werden.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Mein Flehen komme vor dein Angesicht; deiner Verheißung gemäß errette mich.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Meine Lippen sollen Lobpreis ausströmen, denn du lehrst mich deine Satzungen.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Meine Zunge soll von deinem Worte singen, denn alle deine Gebote sind Gerechtigkeit.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Möge deine Hand bereit sein, mir zu helfen, denn deine Befehle habe ich erwählt.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Mich verlangt nach deiner Hilfe, Jahwe, und dein Gesetz ist mein Ergötzen.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Möge meine Seele leben, daß sie dich preise, und deine Gerichte mögen mir helfen.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Ich gehe in der Irre: wie ein verlorenes Schaf suche deinen Knecht; denn deine Gebote vergaß ich nicht.

< Masalimo 119 >