< Masalimo 119 >
1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Bienheureux ceux qui sont sans tache dans la voie, qui marchent dans le Seigneur.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Bienheureux ceux qui étudient ses témoignages; ils le recherchent de tout leur cœur.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Car ceux qui opèrent l’ iniquité n’ont pas marché dans ses voies.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Vous avez ordonné que vos commandements soient gardés très exactement.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Plût à Dieu que toutes mes voies soient dirigées pour garder vos justifications!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Alors je ne serai point confondu, quand je fixerai mes yeux sur vos commandements.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Je vous louerai dans la droiture de mon cœur, parce que j’ai appris les jugements de votre justice.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Je garderai vos justifications: ne m’abandonnez pas entièrement.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Comment un jeune homme corrigera-t-il sa voie? en gardant vos paroles.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Je vous ai recherché de tout mon cœur, ne me repoussez pas de vos commandements.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
C’est dans mon cœur que j’ai caché vos paroles, afin que je ne pèche point contre vous.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Vous êtes béni, Seigneur, enseignez-moi vos justifications.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
J’ai prononcé de mes lèvres tous les jugements de votre bouche.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Dans la voie de vos témoignages, je me suis plu comme dans toutes les richesses.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Je m’exercerai dans vos commandements, et je considérerai vos voies.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Je méditerai sur vos justifications, je n’oublierai pas vos paroles.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Donnez son salaire à votre serviteur, rendez-moi la vie, et je garderai vos paroles.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Dévoilez mes yeux, et je considérerai les merveilles de votre loi.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Moi je suis étranger sur la terre; ne me cachez point vos commandements.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Mon âme a désiré ardemment vos justifications, en tout temps.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Vous avez réprimandé des superbes, maudit ceux qui s’écartent de vos commandements.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Ôtez de moi l’opprobre et le mépris, parce que j’ai recherché vos témoignages.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Car des princes se sont assis, et contre moi ils parlaient; mais votre serviteur s’exerçait sur vos justices.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Car vos témoignages sont ma méditation, et mon conseil, vos justifications.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Mon âme s’est collée à la terre: vivifiez-moi selon votre parole.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Je vous ai dénoncé mes voies, et vous m’avez exaucé; enseignez-moi vos justifications.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Instruisez-moi de la voie de vos commandements, et je m’exercerai dans vos merveilles.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Mon âme s’est assoupie d’ennui; fortifiez-moi par vos paroles.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Écartez de moi la voie de l’iniquité, et en vertu de votre loi, ayez pitié de moi.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
J’ai choisi la voie de la vérité: je n’ai pas oublié vos jugements.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Je me suis attaché à vos témoignages. Seigneur, ne me confondez point.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
J’ai couru dans la voie de vos commandements, lorsque vous avez dilaté mon cœur.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Imposez-moi une loi, Seigneur, la voie de vos justifications, et je la rechercherai toujours.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Donnez-moi l’intelligence, et j’étudierai votre loi, et je la garderai dans tout mon cœur.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Conduisez-moi dans le sentier de vos commandements, parce que c’est ce que j’ai voulu.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Inclinez mon cœur vers vos témoignages, et non vers l’avarice.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Détournez mes yeux, afin qu’ils ne voient pas la vanité: faites-moi vivre dans vos sentiers.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Établissez votre parole dans votre serviteur, par votre crainte.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Détruisez mon opprobre que j’ai appréhendé: vos jugements sont doux.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Voilà que j’ai désiré vos commandements: par votre justice, vivifiez-moi.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Et vienne sur moi votre miséricorde, Seigneur, et votre salut selon votre parole.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Et je répondrai à ceux qui m’outragent, un mot: c’est que j’ai espéré dans vos jugements.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Et n’ôtez pas entièrement de ma bouche la parole de vérité, parce qu’en vos jugements j’ai beaucoup espéré.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Et je garderai votre loi toujours, dans les siècles et dans les siècles des siècles.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Je marchais au large, parce que j’ai recherché vos commandements.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Et je parlais de vos témoignages en présence des rois, et je n’étais pas confondu.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Et je méditais sur vos commandements, que j’ai toujours aimés.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Et j’ai levé mes mains vers vos commandements, que j’ai toujours aimés, et je m’exerçais dans vos justifications.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
ZAIN. Souvenez-vous de votre parole à votre serviteur, par laquelle vous m’avez donné de l’espérance.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Ce qui m’a consolé dans mon humiliation, c’est que votre parole m’a donné la vie.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Des superbes agissaient avec une extrême iniquité, mais de votre loi je ne me suis pas écarté.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Je me suis souvenu, Seigneur, de vos jugements, qui sont dès avant les siècles, et j’ai été consolé.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
La défaillance s’est emparée de moi, à cause des pécheurs qui abandonnent votre loi.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
L’objet de mes chants était vos justifications, dans le lieu de mon pèlerinage.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Je me suis souvenu durant la nuit de votre nom. Seigneur, et j’ai gardé votre loi.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Cela m’est arrivé, parce que j’ai recherché vos justifications.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Ma part, Seigneur, je l’ai dit, c’est de garder votre loi.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
J’ai imploré votre face en tout mon cœur: ayez pitié de moi selon votre parole.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
J’ai songé à mes voies, et j’ai tourné mes pieds vers vos témoignages.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Je suis prêt, et je ne suis pas troublé; en sorte que je garderai vos commandements.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Les liens des pécheurs m’ont enveloppé; mais je n’ai point oublié votre loi.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Au milieu de la nuit, je me levais pour vous louer sur les jugements de votre justification.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Je suis aussi en société avec tous ceux qui vous craignent, et qui gardent vos commandements.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
De votre miséricorde. Seigneur, la terre est pleine. Enseignez-moi vos justifications.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Vous avez usé de bonté envers votre serviteur, ô Seigneur, selon votre parole.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Enseignez-moi la bonté, et la discipline, et la science, parce que j’ai cru à vos commandements.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Avant que je fusse humilié, j’ai péché; c’est pour cela que j’ai gardé votre parole.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Vous êtes bon, vous, et dans votre bonté enseignez-moi vos justifications.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Elle s’est multipliée contre moi, l’iniquité des superbes; mais moi en tout mon cœur j’étudierai vos commandements.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Leur cœur s’est coagulé comme du lait; mais moi j’ai médité votre loi.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Il m’est bon que vous m’ayez humilié, afin de m’apprendre vos justifications.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
La loi de votre bouche est bonne pour moi au dessus des miniers d’or et d’argent.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Vos mains m’ont fait et m’ont formé; donnez-moi l’intelligence, afin que j’apprenne vos commandements.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Ceux qui vous craignent me verront, et se réjouiront, parce qu’en vos paroles j’ai espéré.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
J’ai reconnu, Seigneur, que vos jugements sont équité, et que c’est dans votre vérité que vous m’avez humilié.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Qu’elle se montre, votre miséricorde, afin qu’elle me console, selon votre parole à votre serviteur.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Viennent sur moi vos bontés, et je vivrai, parce que votre loi est ma méditation.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Qu’ils soient confondus, les superbes, parce qu’injustement ils ont commis l’iniquité contre moi: pour moi, je m’exercerai dans vos commandements.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Qu’ils se tournent vers moi, ceux qui vous craignent et qui connaissent vos témoignages.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Devienne mon cœur sans tache dans vos justifications, afin que je ne sois pas confondu.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Mon âme a défailli dans l’attente de votre salut, et en votre parole j’ai beaucoup espéré.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Mes yeux ont défailli dans l’attente de votre parole, disant: Quand me consolerez-vous?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Parce que je suis devenu comme une outre dans la gelée: je n’ai pas oublié vos justifications.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Quel est le nombre de jours de votre serviteur? quand ferez-vous justice de ceux qui me persécutent?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Des hommes iniques m’ont raconté des choses fabuleuses, mais ce n’est pas comme votre loi.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Tous vos commandements sont vérité: iniquement ils m’ont persécuté, venez à mon aide.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Ils m’ont presque anéanti sur la terre; mais moi je n’ai pas abandonné vos commandements.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Selon votre miséricorde, rendez-moi la vie, et je garderai les témoignages de votre bouche.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Éternellement, Seigneur, votre parole demeure dans le ciel.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
À toutes les générations passe votre vérité: vous avez fondé la terre, et elle demeure stable.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Par votre ordre persévère le jour, parce que toutes choses vous sont assujetties.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Si ce n’était que votre loi est ma méditation, j’aurais peut-être péri dans mon humiliation.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Éternellement je n’oublierai pas vos justifications, parce que c’est par elles-mêmes que vous m’avez rendu la vie.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
C’est à vous que j’appartiens, sauvez-moi; parce que j’ai recherché vos justifications.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Des pécheurs m’ont attendu, afin de me perdre; mais j’ai compris vos témoignages.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
J’ai vu la fin de toute perfection: votre commandement est étendu infiniment.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Comme j’ai toujours aimé votre loi, Seigneur, tout le jour elle est ma méditation.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Vous m’avez rendu plus prudent que mes ennemis par votre commandement, parce qu’il est pour jamais avec moi.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
J’ai été plus intelligent que tous ceux qui m’instruisaient, parce que vos témoignages sont ma méditation.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
J’ai été plus intelligent que les vieillards, parce que j’ai recherché vos commandements.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
De toute mauvaise voie j’ai détourné mes pieds, afin que je garde votre parole.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
De vos jugements je ne me suis point écarté, parce que c’est vous qui m’avez prescrit une loi.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Que vos paroles sont douces à ma gorge, plus douces que le miel à ma bouche!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Par vos commandements j’ai acquis de l’intelligence: c’est pour cela que j’ai haï toute voie d’iniquité.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
C’est une lampe à mes pieds que votre parole, et une lumière dans mes sentiers.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
J’ai juré, et j’ai résolu de garder les jugements de votre justice.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
J’ai été extrêmement humilié, Seigneur, rendez-moi la vie selon votre parole.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Ayez pour agréables les hommages volontaires de ma bouche, Seigneur, et enseignez-moi vos jugements.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Mon âme est toujours en mes mains, et je n’ai pas oublié votre loi.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Des pécheurs m’ont tendu un piège, et je n’ai point erré loin de vos commandements.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
C’est en héritage que j’ai acquis pour jamais vos témoignages, parce qu’ils sont l’exultation de mon cœur.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
J’ai incliné mon cœur à accomplir pour jamais vos justifications, à cause de la récompense.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
J’ai eu en haine les hommes iniques, et j’ai aimé votre loi.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Mon aide et mon soutien, c’est vous, et en votre parole j’ai beaucoup espéré.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Éloignez-vous de moi, méchants, et j’étudierai les commandements de mon Dieu.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Soutenez-moi selon votre parole, et je vivrai, et ne me confondez pas dans mon attente.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Aidez-moi, et je serai sauvé; et je méditerai toujours sur vos justifications.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Vous avez méprisé tous ceux qui s’éloignent de vos jugements, parce que leur pensée est injuste.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
J’ai regardé comme prévariquant tous les pécheurs de la terre: c’est pourquoi j’ai aimé vos témoignages.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Transpercez mes chairs de votre crainte; à la vue de vos jugements j’ai craint.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
J’ai fait jugement et justice; ne me livrez pas à ceux qui me calomnient.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Protégez votre serviteur pour le bien, que les superbes ne me calomnient point.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mes yeux ont défailli dans l’attente de votre salut, et dans l’attente de la parole de votre justice.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Agissez avec votre serviteur selon votre miséricorde, et enseignez-moi vos justifications.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Je suis votre serviteur, moi, donnez-moi l’intelligence, afin que je connaisse vos témoignages.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Il est temps d’agir. Seigneur, ils ont dissipé votre loi.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
C’est pour cela que j’ai aimé votre loi au-dessus de l’or et de la topaze.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
C’est pour cela que je me dirigeais vers tous vos commandements, et que j’ai eu toute voie inique en haine.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Admirables sont vos témoignages; c’est pour cela que mon âme les a étudiés.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
La manifestation de vos paroles illumine, elle donne l’intelligence aux petits.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
J’ai ouvert ma bouche, et j’ai attiré l’air, parce que je désirais vos commandements.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Jetez un regard sur moi, et ayez pitié de moi, selon votre équité à l’égard de ceux qui aiment votre nom.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Dirigez mes pas selon votre parole, qu’aucune injustice ne me domine.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Délivrez-moi des calomnies des hommes, afin que je garde vos justifications.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Faites briller la lumière de votre face sur votre serviteur, et enseignez-moi vos justifications.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Mes yeux ont fait couler des cours d’eaux, parce qu’ils ont violé votre loi.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Vous êtes juste, Seigneur, et droit est votre jugement.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Vous avez établi la justice, vos témoignages et votre vérité très solidement.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Mon zèle m’a fait sécher, parce que mes ennemis ont oublié vos paroles.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Votre parole a été très éprouvée par le feu, et votre serviteur l’a aimée.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Je suis jeune et méprisé, mais je n’ai pas oublié vos justifications.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Votre justice est justice éternellement, et votre loi vérité.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
La tribulation et l’angoisse m’ont atteint, vos commandements, c’est ma méditation.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Vos témoignages sont équités éternellement: donnez-moi l’intelligence et je vivrai.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
J’ai crié en tout mon cœur, exaucez-moi. Seigneur, je rechercherai vos justifications.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
J’ai crié vers vous, sauvez-moi, afin que je garde vos commandements.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Je me suis hâté de bonne heure, et j’ai crié, parce qu’en vos paroles j’ai beaucoup espéré.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Mes yeux vous ont prévenu dès le point du jour, afin que je méditasse vos paroles.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Écoutez ma voix selon votre miséricorde, Seigneur, et selon votre jugement donnez-moi la vie.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Ils se sont approchés de l’iniquité, ceux qui me persécutent, et ils se sont éloignés de votre loi.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Vous êtes proche, vous, Seigneur, et toutes vos voies sont vérité.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Dès le commencement j’ai reconnu touchant vos témoignages, que vous les avez fondés pour l’éternité.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Voyez mon humiliation, et délivrez-moi, parce que je n’ai pas oublié votre loi.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Jugez mon jugement et rachetez-moi: à cause de votre parole, donnez-moi la vie.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Loin des pécheurs est le salut, parce qu’ils n’ont pas recherché vos justifications.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Vos miséricordes sont nombreuses, Seigneur: selon votre jugement donnez-moi la vie.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Nombreux sont ceux qui me persécutent et qui me tourmentent; mais je ne me suis point détourné de vos témoignages,
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
J’ai vu des prévariquants et j’ai séché, parce qu’ils n’ont pas gardé vos paroles.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Voyez que j’ai aimé vos commandements, Seigneur: dans votre miséricorde donnez-moi la vie.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Le principe de vos paroles est vérité: éternels sont tous les jugements de votre justice.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Des princes m’ont persécuté gratuitement, et mon cœur a redouté vos paroles.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Pour moi, je me réjouirai dans vos paroles, comme celui qui a trouvé de grandes dépouilles.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
J’ai eu l’iniquité en haine et en abomination; mais j’ai aimé votre loi.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Sept fois le jour, je vous ai adressé une louange, sur les jugements de votre justice.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Paix abondante pour ceux qui aiment votre loi; il n’y a pas pour eux de scandale.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
J’attendais votre salut, Seigneur, et j’ai aimé vos commandements.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Mon âme a gardé vos témoignages, et elle les a aimés ardemment.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
J’ai observé vos commandements et vos témoignages, parce que toutes mes voies sont en votre présence.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Que ma supplication approche de votre présence. Seigneur; selon votre parole donnez-moi l’intelligence.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Que ma demande pénètre en votre présence, selon votre parole délivrez-moi.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Mes lèvres feront retentir un hymne, lorsque vous m’aurez enseigné vos justifications.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Ma langue publiera votre parole, parce que tous vos commandements sont équité.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Que votre main soit sur moi pour me sauver, parce que j’ai fait choix de vos commandements.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
J’ai désiré votre salut, Seigneur, et votre loi est ma méditation.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Mon âme vivra, et vous louera, et vos jugements me viendront en aide.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
J’ai erré comme une brebis qui s’est perdue: cherchez votre serviteur, parce que je n’ai pas oublié vos commandements.