< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Heureux ceux dont la conduite est intègre, Et qui suivent la loi de l'Éternel!
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Heureux ceux qui obéissent à ses enseignements, Qui le recherchent de tout leur coeur,
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Et qui ne commettent pas d'iniquité, Mais qui marchent dans les voies de l'Éternel!...
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Tu as donné tes commandements, ô Dieu, Pour qu'on les observe avec soin.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Daigne diriger ma conduite, Afin que j'observe tes préceptes!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Alors je n'aurai point à rougir, Quand je fixerai les regards sur tous tes commandements.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Je te célébrerai dans la droiture de mon coeur. Quand j'aurai appris tes justes jugements.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Je veux observer tes préceptes; Ne m'abandonne pas entièrement!
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Comment le jeune homme rendra-t-il pure sa conduite? C'est en restant fidèle à ta parole.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Je te cherche de tout mon coeur; Ne permets pas que je m'égare loin de tes commandements!
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
J'ai serré ta parole dans mon coeur. Afin de ne pas pécher contre toi.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Béni sois-tu, ô Éternel! Enseigne-moi tes préceptes.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Mes lèvres énumèrent Tous les jugements que ta bouche a prononcés.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Je trouve autant de joie à suivre tes enseignements, Qu'à posséder tous les trésors du monde.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Je méditerai tes commandements, Et je fixerai mes regards sur tes sentiers.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Je ferai mes délices de tes préceptes, Et je n'oublierai point tes paroles.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Accorde ce bienfait à ton serviteur: que je vive. Et que je garde ta parole!
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Dessille mes yeux. Afin que je contemple les merveilles de ta loi.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Je suis étranger sur la terre; Ne me cache pas tes commandements!
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Mon âme est consumée par l'amour Que lui inspirent tes lois, en tout temps.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Tu menaces les orgueilleux, Ces maudits qui s'écartent de tes commandements.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Éloigne de moi l'opprobre et le mépris; Car j'obéis à tes enseignements.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Les puissants eux-mêmes se sont assis, Et ils ont parlé contre moi; Mais ton serviteur médite tes préceptes.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Oui, tes enseignements font mes délices: Ils sont mes meilleurs conseillers.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Mon âme est abattue dans la poussière; Fais-moi revivre, selon ta parole!
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Je t'ai fait connaître ma conduite, et tu m'as approuvé; Enseigne-moi tes préceptes.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Montre-moi la voie que tu m'ordonnes de suivre. Et je méditerai tes merveilles.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Mon âme attristée se fond en larmes; Relève-moi, selon ta parole!
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Éloigne-moi de la voie du mensonge; Accorde-moi comme une grâce la connaissance de ta loi!
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
J'ai choisi la voie de la fidélité; J'ai mis tes jugements devant mes yeux.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Je me suis attaché à tes enseignements: Éternel, ne me rends pas confus!
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Je m'élancerai dans la voie de tes commandements, Quand tu auras mis mon coeur au large.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Éternel, apprends-moi à suivre tes préceptes, Et je les observerai jusqu'à la fin.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Donne-moi l'intelligence, et j'observerai ta loi: Je la pratiquerai de tout mon coeur.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Conduis-moi dans les sentiers de tes commandements; Car mon bonheur est de les suivre.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Incline mon coeur vers tes enseignements. Et non pas vers le gain.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Détourne mes yeux de la contemplation des choses vaines; Que je trouve la vie en marchant dans tes voies.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Accomplis envers ton serviteur ta promesse: Tu l’as donnée pour qu’on te craigne.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Détourne de moi l'opprobre que je redoute; Car tes jugements sont pleins de bonté.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
J'ai un ardent amour pour tes commandements! Fais-moi revivre par ta justice!
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Éternel, que tes bontés et ton salut Descendent sur moi, selon ta promesse!
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Alors je saurai comment répondre à celui qui m'outrage; Car je me confie en ta parole.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Ne me refuse pas entièrement la faveur De rendre témoignage à la vérité; Car je mets mon attente en tes jugements.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Alors j'observerai ta loi constamment. Sans l'abandonner jamais.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Je marcherai d'un pas libre; Car j'ai à coeur de suivre tes commandements.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Je proclamerai tes volontés devant les rois. Et je n'en aurai aucune honte.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Je ferai mes délices de tes commandements: Ils sont l'objet de mon amour.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
J'élèverai mes mains vers tes commandements que j'aime. Et je méditerai tes préceptes.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Souviens-toi de la parole donnée à ton serviteur C'est sur elle que tu as fondé mon espérance.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Ce qui me console dans mon affliction, C'est que ta parole me rend la vie.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Des orgueilleux me couvrent de railleries; Mais je ne m'écarte pas de ta loi.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Je me rappelle tes jugements d'autrefois, ô Éternel, Et j'y trouve ma consolation.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
L'indignation me saisit, à cause des méchants Qui abandonnent ta loi.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Tes préceptes sont le sujet de mes cantiques, Dans la maison où j'habite en étranger.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
La nuit, je me rappelle ton nom, ô Éternel, Et j'observe ta loi.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Le bien qui m'est échu en partage. C'est de garder tes commandements.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Tu es ma part, ô Éternel. C'est pourquoi j'ai promis de garder tes paroles.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Je t'ai imploré de tout mon coeur: Aie pitié de moi, selon ta promesse!
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
J'ai fait l'examen de ma conduite, Et j'ai dirigé mes pas dans la voie de tes enseignements.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Je me hâte, je ne diffère point D'observer tes commandements.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Les pièges des méchants m'ont environné; Je n'ai point oublié ta loi.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Au milieu de la nuit, je me lève pour te célébrer, A cause de tes justes jugements.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Je suis le compagnon de tous ceux qui te craignent Et qui observent tes commandements.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Éternel, la terre est pleine de ta bonté! Enseigne-moi tes préceptes.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Tu as fait du bien à ton serviteur, Éternel, selon ta parole.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Donne-moi un sens droit, ainsi que la vraie sagesse; Car j'ai foi en tes commandements.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Avant d'être affligé, je m'égarais; Mais, maintenant, j'observe ta parole.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Tu es bon, et tu manifestes ta bonté: Enseigne-moi tes préceptes.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Des orgueilleux ont ourdi contre moi des mensonges; Mais moi, j'obéis de tout mon coeur à tes ordres.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Leur coeur est épaissi comme de la graisse; Moi, je trouve mes délices dans ta loi.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Il m'est bon d'avoir été affligé: C'est ainsi que j'ai appris à connaître ta volonté.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Les enseignements de ta bouche sont plus précieux pour moi Que des milliers de pièces d'or et d'argent.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Toi dont les mains m'ont formé et créé, Donne-moi l'intelligence, afin que je puisse apprendre tes lois.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Ceux qui te craignent me verront, et ils se réjouiront; Car j'espère en ta parole.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Je sais, ô Éternel, que tes jugements ne sont que justice: C'est dans ta fidélité que tu m'as affligé.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Que ta bonté soit donc ma consolation. Comme tu l'as promis à ton serviteur.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Que tes compassions s'étendent sur moi, et je vivrai; Car ta loi fait mes délices.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Que les orgueilleux soient confus. Eux qui m'oppriment sans motif; Et moi, je méditerai tes commandements.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Qu'ils reviennent à moi, ceux qui te craignent Et qui connaissent tes enseignements!
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Que mon coeur soit sincèrement attaché à tes préceptes, Afin que je n'aie pas à rougir de honte!
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Mon âme languit après son salut; J'espère en ta parole.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Mes yeux se consument dans l'attente de ta promesse; Je dis: «Quand me consoleras-tu?»
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Je suis comme une outre dans un nuage de fumée; Mais je n'oublie pas tes préceptes.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Combien courte est la vie de ton serviteur! Quand donc feras-tu justice de ceux qui me persécutent?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Les orgueilleux ont creusé des pièges sous mes pas; Car jamais ils n'agissent selon ta loi.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Tous tes commandements témoignent de ta fidélité. Mes ennemis me persécutent sans motif; aide-moi!
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Encore un peu, et ils me faisaient disparaître de la terre! Mais je n'abandonne pas tes commandements.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Fais-moi revivre, toi qui es plein de bonté. Et j'obéirai aux enseignements de ta bouche.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Éternel, ta parole subsiste à jamais dans les cieux;
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Ta fidélité dure d'âge en âge! Tu as fondé la terre, et elle demeure ferme.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Tout subsiste aujourd'hui selon tes lois; Car toutes choses te servent.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Si ta loi n'eût fait mes délices. J'aurais déjà péri dans ma misère.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Jamais je n'oublierai tes commandements; Car c'est par eux que tu m'as fait revivre.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Je suis à toi, sauve-moi; Car je m'applique à suivre tes commandements.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Les méchants m'ont épié pour me faire périr; Mais je suis attentif à tes enseignements.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
J'ai vu des bornes à tout ce qui est parfait; Mais ta loi est d'une étendue sans fin.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Combien j'aime ta loi! Tout le jour, je m'applique à la méditer.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Tes commandements me rendent plus sage Que mes ennemis, Parce qu'ils sont toujours présents à mon esprit.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
J'ai surpassé en sagesse tous ceux qui m'avaient instruit; Car tes enseignements sont l'objet de mes méditations.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Je suis plus intelligent que les vieillards eux-mêmes; Car j'ai gardé tes commandements.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
J'ai détourné mes pas de tout mauvais chemin, Afin d'observer ta parole.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Je ne m'écarte point de tes lois, Parce que c'est toi qui m'as instruit.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Combien tes paroles sont douces à mon palais, Plus douces que le miel à ma bouche!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Tes commandements m'instruisent; C'est pourquoi je hais tous les sentiers trompeurs.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Ta parole est un flambeau qui guide mes pas, Une lumière sur mon sentier.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
J'ai juré — et je tiendrai ma promesse. — D'observer tes justes lois.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Je suis extrêmement affligé: Éternel, fais-moi revivre, selon ta parole!
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Agrée les chants de louange Que t'offre ma bouche, ô Eternel, Et enseigne-moi tes commandements!
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Ma vie est continuellement en danger; Mais je n'oublie point ta loi.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Les méchants m'ont tendu des pièges; Mais je ne me suis pas écarté de tes commandements.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Tes enseignements sont pour toujours mon héritage; Ils sont la joie de mon coeur.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
J'ai rendu mon coeur docile à l'observation de tes préceptes, Pour toujours, jusqu'à la fin.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Je hais les hommes au coeur double; Mais j'aime ta loi.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Tu es mon refuge et mon bouclier; J'espère en ta parole.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Retirez-vous de moi, méchants! Je veux garder les commandements de mon Dieu.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Soutiens-moi, selon ta promesse, Afin que je vive, Et ne me fais pas rougir d'avoir mis en toi mon espérance!
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Soutiens-moi: je serai sauvé. Et j'aurai toujours les yeux sur tes préceptes!
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Tu traites avec mépris tous ceux qui s'écartent de tes lois; Car toutes leurs machinations sont frappées d'impuissance.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Tu rejettes, comme de l'écume. Tous les méchants de la terre. C'est pourquoi j'aime tes enseignements.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Ma chair tremble de frayeur en ta présence. Et je crains tes jugements.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
J'ai pratiqué ce qui est droit et juste; Ne m'abandonne pas à mes oppresseurs!
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Prends sous ta garde le bonheur de ton serviteur; Que les orgueilleux ne m'oppriment pas!
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mes yeux se consument dans l'attente de ton salut Et de tes promesses, ô Dieu juste.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Agis envers ton serviteur selon ta bonté, Et enseigne-moi tes préceptes.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Je suis ton serviteur; donne-moi l'intelligence, Afin que je puisse comprendre tes enseignements.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Le temps est venu d'agir en ta faveur, ô Éternel; Car on viole ta loi.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
C'est pourquoi j'aime tes commandements Plus que l'or, même que l'or fin.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Ainsi je proclame que tous tes commandements sont droits, Et je hais tout sentier trompeur.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Tes enseignements sont admirables; Aussi mon âme les met-elle en pratique.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Tes paroles sont une révélation qui éclaire; Elles donnent de l'intelligence aux simples.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
J'ouvre la bouche et je soupire; Car j'ai un grand amour pour tes commandements.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Regarde-moi et prends pitié de moi, Comme tu le fais pour ceux qui aiment ton nom.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Que ta parole affermisse mes pas. Et ne permets point que le péché domine sur moi.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Délivre-moi de l'oppression des hommes. Afin que j'observe tes commandements!
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Fais resplendir ta face sur ton serviteur, Et enseigne-moi tes préceptes!
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Des ruisseaux de larmes coulent de mes yeux. Parce que personne n'observe ta loi.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Tu es juste, ô Éternel, Et tes jugements sont droits.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Tu prescris avec force, dans tes enseignements, La justice et la fidélité.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Mon zèle me consume, Parce que mes ennemis ont oublié tes paroles.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Ta parole est parfaitement pure; Aussi est-elle chère à ton serviteur.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Je suis petit et méprisé; Mais je n'oublie pas tes commandements.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Ta justice est une justice éternelle, Et ta loi n'est que vérité.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
La détresse et l'angoisse m'ont atteint; Mais tes commandements font mes délices.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Tes enseignements sont éternellement justes; Donne-m'en l'intelligence, afin que je vive!
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Je t'invoque de tout mon coeur; réponds-moi, ô Éternel, Et je garderai tes préceptes.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Je crie vers toi; sauve-moi, Et je suivrai tes enseignements.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Je devance l'aurore, et je t'invoque: Je mets mon espoir en ta parole.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Mes yeux devancent les veilles de la nuit, Pour méditer ta promesse.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Dans ta bonté, ô Éternel, écoute ma voix; Dans ta justice, fais-moi revivre!
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Les voilà près de moi, ceux qui se précipitent dans le crime Et qui se détournent de ta loi.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Mais toi aussi, ô Éternel, tu t'approches de moi. Et tous tes commandements m'assurent de ta fidélité.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Depuis longtemps j'ai appris à connaître tes enseignements; Car tu les as établis pour toujours.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Regarde mon affliction, et délivre-moi; Car je n'ai pas oublié ta loi.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Défends ma cause, et délivre-moi; Fais-moi revivre, selon ta promesse!
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Le salut est loin des méchants. Parce qu'ils ne se soucient pas de tes préceptes.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Tes compassions sont en grand nombre, ô Éternel: Fais-moi revivre, suivant les arrêts de ta justice!
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Mes persécuteurs et mes adversaires sont nombreux; Mais je ne me détourne pas de tes enseignements.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
J'ai vu les infidèles, et j'en ai horreur: Ils n'observent pas ta parole.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Vois combien j'aime tes commandements; Éternel, fais-moi revivre, dans ta bonté!
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Ta parole tout entière n'est que vérité, Et tous les arrêts de ta justice sont éternels.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Les grands m'ont persécuté sans motif; Mais mon coeur n'a craint que tes paroles.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Je me réjouis de ta promesse. Comme celui qui a trouvé un grand trésor.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Je hais, j'ai en horreur le mensonge. Et j'aime ta loi.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Je te loue sept fois le jour. Pour les arrêts de ta justice.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Grande est la paix de ceux qui aiment ta loi: Rien ne peut les faire chanceler.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Éternel, j'attends ta délivrance, Et je pratique tes commandements.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Mon âme obéit à tes enseignements, Et je les aime d'un grand amour.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
J'observe tes commandements et tes lois; Car toute ma conduite est présente à tes yeux.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Éternel, que mon cri parvienne jusqu'à toi! Donne-moi l'intelligence, conformément à ta parole!
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Que ma supplication s'élève jusqu'à toi! Délivre-moi, suivant ta promesse!
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Mes lèvres proclameront ta louange, Quand tu m'auras enseigné tes préceptes.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Ma langue célébrera ta parole; Car tous tes commandements sont justes.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Étends ta main pour me venir en aide; Car je veux obéir à tes commandements.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Je soupire après ton salut, ô Éternel, Et ta loi fait mes délices.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Que mon âme vive, afin qu'elle te loue, Et que tes jugements soient mon appui!
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Je suis errant comme une brebis perdue: Viens à la recherche de ton serviteur! Car je n'ai pas oublié tes commandements!

< Masalimo 119 >