< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Heureux ceux dont la voie est intègre, qui suivent la Loi de l’Eternel!
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Heureux ceux qui respectent ses statuts, le recherchent de tout leur cœur,
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
qui, se gardant bien de commettre aucune injustice, marchent dans ses voies!
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Tu as promulgué tes ordonnances, pour qu’on les observe strictement.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Ah! puissent mes pas être fermes, pour que j’observe tes préceptes!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Alors, je ne serai point déçu, en portant mes regards sur tous tes commandements.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Je te rendrai grâce en toute droiture de cœur, en m’instruisant des règles de ta justice.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Tes statuts, je les observerai: ne m’abandonne en aucun temps.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Comment le jeune homme rendra-t-il pure sa conduite? En se conformant à tes paroles.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
De tout mon cœur je m’enquiers de toi, ne me laisse pas dévier de tes prescriptions.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
En mon sein j’ai déposé tes instructions, pour ne pas faillir à ton égard.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Béni sois-tu, ô Eternel! Enseigne-moi tes préceptes.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
De mes lèvres je proclame toutes les règles sorties de ta bouche.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Dans le chemin tracé par tes témoignages je trouve ma joie, comme si c’était le comble de la richesse.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Je m’entretiens de tes commandements, et je contemple tes voies.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Je me délecte de tes préceptes, et n’oublie point tes paroles.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Accorde tes bienfaits à ton serviteur, pour que je vive et observe tes paroles.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Dessille-moi les yeux, pour que je puisse contempler les merveilles issues de ta Loi.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Je suis un simple étranger sur la terre, ne me tiens pas cachés tes commandements.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Mon âme est travaillée du désir de tes règlements, à toute époque.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Toi, tu réprouves les arrogants maudits, qui se fourvoient loin de tes commandements.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Affranchis-moi de la honte et du mépris, car je respecte tes témoignages.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Dussent même les grands prendre siège et déblatérer contre moi, ton serviteur méditera tes lois.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Oui, tes témoignages sont mes délices, mes meilleurs conseillers.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Mon âme est collée à la poussière, conserve-moi en vie, suivant ta parole.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
J’Ai exposé ma conduite, et tu m’as répondu; enseigne-moi tes lois.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Laisse-moi comprendre le chemin de tes préceptes, et je réfléchirai à tes merveilles.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Mon âme, de chagrin, se fond en larmes, redresse-moi, selon ta parole.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Eloigne de moi le chemin du mensonge, gratifie-moi de ta Loi.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
J’Ai choisi la voie de la fidélité, placé tes règles sous mes regards.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Je suis attaché à tes statuts, Seigneur, ne m’inflige aucune déception.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Je suivrai avec empressement le chemin de tes préceptes, car tu élargis mon cœur.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Enseigne-moi le chemin de tes préceptes, je veux en suivre les traces.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Donne-moi l’intelligence pour que je garde ta loi et l’observe de tout mon cœur.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Dirige-moi dans le sentier de tes commandements, car j’y trouve ma satisfaction.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Incline mon cœur vers tes vérités, et non vers un vain lucre.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Détourne mes yeux de la vue des choses frivoles, fais-moi vivre dans tes voies.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Accomplis ton dire en faveur de ton serviteur, car il amène à te révérer.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Ecarte de moi la honte que je redoute, car tes jugements sont précieux.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Voici, j’ai la passion de tes préceptes, fais-moi vivre par ta justice.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Que tes bontés descendent sur moi, Eternel, ton salut, tel que tu l’as promis.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Je pourrai ainsi répliquer à qui m’outrage, car j’ai confiance en ta parole.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Ne supprime jamais une parole de vérité de ma bouche, car je mets mon attente en tes jugements.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Je veux observer ta Loi constamment, à tout jamais.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Ainsi je circulerai bien au large, car j’aurai eu le souci de tes préceptes.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Je ferai de tes vérités l’objet de mes discours, en face des rois, sans aucune fausse honte.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Et je ferai mes délices de tes commandements, qui me sont bien chers.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Je tendrai mes mains vers tes commandements, que j’aime, et consacrerai mes méditations à tes préceptes.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Rappelle-toi, en faveur de ton serviteur, la promesse où tu as voulu que je mette mon attente.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
C’Est là ma consolation dans la misère, que ta parole me rende la vie.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Des arrogants m’ont raillé au possible: je n’ai point dévié de ta Loi.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Je me remémore tes jugements de jadis, ô Eternel, et j’y trouve du réconfort.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Un violent frisson m’avait saisi à cause des méchants, qui abandonnent ta Loi.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Mais tes préceptes sont devenus pour moi un sujet de cantiques dans ma demeure passagère.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Je me souviens de ton nom pendant la nuit, Seigneur, et j’observe ta Loi.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
C’Est là mon bonheur à moi, de m’attacher à tes préceptes.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
"C’Est mon lot à moi, ô Eternel, me suis-je dit, d’observer tes paroles."
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Je t’implore de tout mon cœur, sois-moi propice, selon ta promesse.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
J’Ai médité sur mes voies, et ramené mes pas vers tes statuts.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Je me suis empressé, sans perdre un moment, d’observer tes commandements.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Les liens des méchants m’avaient enserré: je n’ai point oublié ta Loi.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Au milieu de la nuit je me lève pour te rendre grâce, à cause de tes équitables jugements.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Je suis l’allié de tous ceux qui te révèrent et qui pratiquent tes lois.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
De ta grâce, Eternel, la terre est remplie: enseigne-moi tes préceptes.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Tu as traité avec bienveillance ton serviteur, ô Eternel, conformément à ta parole.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Enseigne-moi ces choses précieuses: le jugement et la science, car j’ai foi en tes commandements.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Avant que je fusse humilié, je m’égarais; maintenant, je suis attentif à tes discours.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Tu es bon et tu exerces le bien, instruis-moi dans tes préceptes.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Des orgueilleux inventent des mensonges contre moi, et moi, de tout cœur, j’observe tes ordonnances.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Leur cœur est bouché comme par la graisse: moi, je fais mes délices de ta Loi.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
C’Est un avantage pour moi d’avoir connu la misère, pour mieux apprendre tes préceptes.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Plus précieux est pour moi l’enseignement de ta bouche que des monceaux de pièces d’or et d’argent.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Ce sont tes mains qui m’ont formé et organisé, donne-moi l’intelligence pour que j’apprenne à connaître tes commandements.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Ceux qui te craignent, en me voyant, seront dans la joie, car j’espère en ta parole.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Je sais, ô Seigneur, que tes arrêts sont toute justice, et que c’est en équité que tu m’as humilié.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Que ta grâce s’applique donc à me consoler, comme tu l’avais promis à ton serviteur.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Que ta miséricorde s’étende sur moi et que je vive, puisque ta Loi fait mes délices.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Que les orgueilleux soient déçus, pour m’avoir maltraité gratuitement; moi, je méditerai tes préceptes.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Que tes adorateurs reviennent à moi, et ceux qui connaissent tes vérités.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Que mon cœur soit sincèrement attaché à tes lois, afin que je n’aie point à rougir.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Mon âme languit après ton secours, c’est en ta parole que je mets mon espoir.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Mes yeux se consument dans l’attente de ta parole, tandis que je dis: "Quand me consoleras-tu?"
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Car je suis comme une outre dans des flots de fumée: tes préceptes, je ne les ai point oubliés.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Que dureront les jours de ton serviteur? Quand feras-tu justice de mes persécuteurs?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Des pervers m’ont creusé des fosses, au mépris de ta Loi.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Tous tes commandements sont loyauté parfaite, eux me pourchassent sans motif: viens à mon aide.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Peu s’en faut qu’ils ne m’aient anéanti sur terre, alors que moi, je n’ai point délaissé tes préceptes.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Fidèle à ta bonté, conserve-moi en vie, et je respecterai le témoignage de ta bouche.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Pour l’éternité, Seigneur, ta parole demeure immuable dans les cieux.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
D’Âge en âge dure ta fidélité: tu as affermi la terre, et elle est inébranlable.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Selon tes lois, les êtres subsistent aujourd’hui, car ils sont tous tes serviteurs.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Si ta Loi n’avait fait mes délices, j’aurais succombé dans ma misère.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Jamais je n’oublierai tes préceptes, car par eux tu m’assures la vie.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Je suis à toi, prête-moi secours, car je m’enquiers de tes ordres.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Des méchants me guettent pour me perdre: je cherche à pénétrer le sens de tes prescriptions.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
A tout bien j’ai vu des limites: ta Loi est infiniment vaste.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Combien j’aime ta Loi! Tout le temps elle est l’objet de mes méditations.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Tes commandements me rendent plus sage que mes ennemis, car ils sont pour moi un bien inépuisable.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Je suis plus avisé que tous mes précepteurs, car tes vérités sont le thème de mes réflexions.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
J’Ai plus d’expérience que les vieillards, car je respecte tes préceptes.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
J’Ai tenu mes pas éloignés de tout mauvais chemin, en vue d’observer tes paroles.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Je n’ai point dévié de tes règles, car c’est toi qui m’as instruit.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Que tes paroles sont douces à mon palais! Le miel l’est moins à ma bouche.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
J’Ai puisé mon savoir dans tes préceptes, c’est pourquoi je hais toute voie mensongère.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Ta parole est un flambeau qui éclaire mes pas, une lumière qui rayonne sur ma route.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
J’Ai fait le serment, et je le tiendrai, d’observer les règles de ta justice.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Je suis extrêmement accablé, Eternel, conserve-moi en vie selon ta parole.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Agrée de grâce, Seigneur, les vœux de ma bouche, et enseigne-moi tes lois.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Mon âme court sans cesse des dangers, et je n’ai point oublié ta loi.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Des méchants me dressent des pièges, pourtant je ne dévie point de tes préceptes.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Je reste pour toujours en possession de tes vérités, car elles sont la joie de mon cœur.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
J’Ai incliné mon cœur à accomplir tes lois à tout jamais, jusqu’à la fin dernière.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Je hais les gens à double face, mais ta Loi, je l’aime.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Tu es mon abri et mon bouclier, j’espère en ta parole.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Loin de moi, ô malfaiteurs! Je veux observer les commandements de mon Dieu.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Soutiens-moi selon ta promesse pour que je vive, et ne laisse pas mon espoir se changer en déception.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Accorde-moi ton appui pour que je sois sauvé, je me tournerai sans cesse vers tes lois.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Tu foules aux pieds ceux qui errent loin de tes préceptes, car leurs ruses habiles ne sont que mensonge.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Comme des scories, tu élimines tous les méchants sur terre, c’est pourquoi j’aime tes vérités.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Ma chair frissonne de la terreur que tu inspires, et je redoute tes jugements.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
J’Ai pratiqué la justice et l’équité, ne m’abandonne pas à mes oppresseurs.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Interviens pour le bonheur de ton serviteur, que des arrogants ne m’accablent point.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mes yeux languissent après ton secours, et après ta parole de salut.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Traite ton serviteur selon ta grâce, et enseigne-moi tes préceptes.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Je suis ton serviteur, donne-moi la sagacité, pour que je comprenne tes vérités.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Le temps est venu d’agir pour l’Eternel: on a violé ta Loi.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
C’Est pourquoi j’aime tes commandements, plus que l’or et le métal fin.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
C’Est pourquoi je reconnais la parfaite droiture de tous tes préceptes, et déteste toute voie mensongère.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Merveilleux sont tes statuts, aussi mon âme les garde-t-elle avec soin.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
La révélation de tes paroles projette de la lumière, donne de l’intelligence aux simples.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
J’Ouvre largement la bouche pour aspirer, car j’ai la passion de tes commandements.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Tourne-toi vers moi et sois-moi propice, comme tu le fais pour ceux qui aiment ton nom.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Affermis mes pas par tes discours, qu’aucune mauvaise passion ne prenne le dessus sur moi.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Délivre-moi de l’oppression des hommes, pour que je puisse observer tes préceptes.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Fais luire ta face sur ton serviteur, et enseigne-moi tes préceptes.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Mes yeux ont versé des torrents de larmes, parce qu’on n’observe pas ta Loi.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Tu es juste, ô Seigneur, et équitables sont tes jugements.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Tu as imposé tes justes ordonnances: elles sont tout à fait infaillibles.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Je suis consumé par mon zèle jaloux, car mes adversaires oublient tes paroles.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Ta parole est infiniment épurée, elle est chère à ton serviteur.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Je suis chétif et méprisé: tes préceptes, je ne les ai point oubliés.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Ta justice est éternellement équitable, et ta Loi est vérité.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
La détresse et l’angoisse m’ont atteint: tes commandements sont mes délices.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Tes statuts sont à jamais équitables, permets-moi de les comprendre, pour que je vive.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Je t’invoque de tout cœur, exauce-moi, Seigneur! Je veux observer tes préceptes.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Je t’appelle, viens à mon secours, et je garderai tes statuts.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Dès l’aurore je m’empresse d’implorer, j’espère en ta parole.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Mes yeux devancent les veilles de la nuit, pour méditer ta parole.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Daigne écouter ma voix, selon ta bonté, Eternel; fais-moi vivre selon l’arrêt de ta justice.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Ils m’approchent, ceux qui courent après l’infamie, il s’éloignent de ta Loi.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Toi, Seigneur, tu es près de moi, tous tes commandements sont vérité.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Dès longtemps j’avais connaissance de tes statuts, car tu les as établis pour l’éternité.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Vois ma misère et tire-moi du danger, car je n’ai pas oublié ta Loi.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Prends en main ma cause et délivre-moi, fais-moi vivre pour me consacrer à ta parole.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Le salut est loin des méchants, car ils ne se soucient pas de tes préceptes.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Grande est ta miséricorde, Eternel, fais-moi vivre selon l’arrêt de ta justice.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Nombreux sont mes persécuteurs et mes ennemis; je n’ai point dévié de tes statuts.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
J’Ai observé les traîtres et j’en ai été écœuré, car ils ne respectent pas ta parole.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Vois comme j’aime tes prescriptions, Seigneur, selon ta bonté, fais-moi vivre.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
L’Ensemble de tes paroles est vérité, éternels sont tous les arrêts de ta justice.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Des grands me persécutent gratuitement, et mon cœur tremble devant ta parole.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Je me réjouis de tes promesses, comme quelqu’un qui a trouvé un riche butin.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Je hais le mensonge, je l’ai en horreur, c’est ta Loi que j’aime.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Sept fois par jour je célèbre tes louanges, en raison de tes justes arrêts.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Un grand bonheur attend ceux qui aiment ta Loi: pour eux point de cause de chute.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
J’Ai pleine confiance en ton secours, Seigneur, et j’accomplis tes commandements.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Mon âme observe tes témoignages, je les aime infiniment.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
J’Observe tes prescriptions et tes statuts, car toutes mes voies sont sous tes regards.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Que mon hymne arrive jusqu’à toi, Eternel, fais-moi comprendre le sens de ta parole.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Que ma supplication vienne devant toi, sauve-moi selon ta promesse.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Mes lèvres laisseront s’échapper tes louanges, car tu m’enseignes tes préceptes.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Ma langue chantera ta parole, car tous tes commandements sont équité.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Puisse ta main s’appliquer à me secourir, puisque j’ai fait choix de tes prescriptions!
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
J’Aspire à ton secours, Eternel, et ta Loi fait mes délices.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Que mon âme vive pour te louer, que tes jugements soient mon soutien.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
J’Erre comme une brebis égarée; mets-toi à la recherche de ton serviteur! Car je n’ai pas oublié tes commandements.

< Masalimo 119 >