< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
ALEPH Heureux ceux dont les voies sont irréprochables, qui marchent selon la loi de Yahvé.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Heureux ceux qui gardent ses statuts, qui le cherchent de tout leur cœur.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Oui, ils ne font rien de mal. Ils marchent dans ses voies.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Tu as ordonné tes préceptes, que nous devons leur obéir pleinement.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Oh, si mes voies étaient fermes pour obéir à tes statuts!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Alors je ne serais pas déçu, quand je considère tous tes commandements.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Je te louerai avec droiture de cœur, quand j'apprends tes jugements justes.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
J'observerai tes statuts. Ne m'abandonne pas complètement. BETH
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Comment un jeune homme peut-il garder sa voie pure? En vivant selon ta parole.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Je t'ai cherché de tout mon cœur. Ne me laisse pas m'éloigner de tes commandements.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
J'ai caché ta parole dans mon cœur, pour ne pas pécher contre toi.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Béni sois-tu, Yahvé. Apprends-moi tes statuts.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Avec mes lèvres, J'ai déclaré toutes les ordonnances de ta bouche.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Je me suis réjoui sur le chemin de tes témoignages, autant que dans toutes les richesses.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Je méditerai sur tes préceptes, et réfléchissez à votre façon de faire.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Je ferai mes délices de tes statuts. Je n'oublierai pas ta parole. GIMEL
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Fais du bien à ton serviteur. Je vivrai et j'obéirai à ta parole.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Ouvrez mes yeux, pour que je voie les merveilles de ta loi.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Je suis un étranger sur la terre. Ne me cachez pas vos commandements.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Mon âme se consume de désir pour tes ordonnances en tout temps.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Tu as réprimandé les orgueilleux qui sont maudits, qui s'éloignent de tes commandements.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Éloigne de moi l'opprobre et le mépris, car j'ai observé tes lois.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Quand les princes s'asseyent et me calomnient, ton serviteur méditera sur tes statuts.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Tes statuts sont mes délices, et mes conseillers. DALETH
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Mon âme est couchée dans la poussière. Ranime-moi selon ta parole!
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
J'ai exposé mes voies, et tu m'as répondu. Apprends-moi tes statuts.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Fais-moi comprendre l'enseignement de tes préceptes! Alors je méditerai sur tes merveilles.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Mon âme est fatiguée par la tristesse; fortifie-moi selon ta parole.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Garde-moi de la voie de la tromperie. Accorde-moi ta loi gracieusement!
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
J'ai choisi la voie de la vérité. J'ai mis vos ordonnances devant moi.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Je m'attache à tes statuts, Yahvé. Ne me laissez pas être déçu.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Je cours dans le sentier de tes commandements, car tu as libéré mon cœur. HE
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Enseigne-moi, Yahvé, la voie de tes statuts. Je les garderai jusqu'à la fin.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Donne-moi l'intelligence, et je garderai ta loi. Oui, j'y obéirai de tout mon cœur.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Dirige-moi dans le chemin de tes commandements, car je me réjouis d'eux.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Tourne mon cœur vers tes statuts, et non vers un gain égoïste.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Détourne mes yeux des choses sans valeur. Ravivez-moi dans vos voies.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Accomplis ta promesse à ton serviteur, pour que vous soyez craint.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Otez le déshonneur que je redoute, car tes ordonnances sont bonnes.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Voici, j'ai envie de tes préceptes! Ravivez-moi dans votre justice. VAV
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Que ta bonté vienne aussi à moi, Yahvé, ton salut, selon ta parole.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Ainsi, je répondrai à celui qui me fait des reproches, car j'ai confiance en ta parole.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
N'arrache pas de ma bouche la parole de vérité, car j'ai mis mon espoir dans vos ordonnances.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Ainsi, j'obéirai sans cesse à ta loi, pour toujours et à jamais.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Je marcherai dans la liberté, car j'ai cherché tes préceptes.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Je parlerai aussi de tes statuts devant les rois, et vous ne serez pas déçu.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Je ferai mes délices de tes commandements, parce que je les aime.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Je tends les mains vers tes commandements, que j'aime. Je méditerai sur tes statuts. ZAYIN
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Souviens-toi de ta parole envers ton serviteur, parce que tu m'as donné de l'espoir.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
C'est ma consolation dans ma détresse, car ta parole m'a fait revivre.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Les arrogants se moquent excessivement de moi, mais je ne m'écarte pas de ta loi.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Je me souviens de tes ordonnances d'autrefois, Yahvé, et je me suis consolé.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
L'indignation s'est emparée de moi, à cause des méchants qui abandonnent ta loi.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Tes statuts ont été mes chants dans la maison où je vis.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Je me suis souvenu de ton nom, Yahvé, dans la nuit, et j'obéis à ta loi.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
C'est mon chemin, que je garde tes préceptes. HETH
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Yahvé est mon partage. J'ai promis d'obéir à vos paroles.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
J'ai cherché ta faveur de tout mon cœur. Sois miséricordieux envers moi selon ta parole.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
J'ai réfléchi à ma façon de faire, et tourné mes pas vers tes statuts.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Je me dépêcherai, et ne tarderai pas, pour obéir à tes commandements.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Les cordes des méchants me lient, mais je n'oublierai pas votre loi.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
A minuit, je me lèverai pour te rendre grâce, à cause de vos justes ordonnances.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Je suis l'ami de tous ceux qui te craignent, de ceux qui observent tes préceptes.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
La terre est pleine de ta bonté, Yahvé. Apprends-moi tes statuts. TETH
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Tu as bien traité ton serviteur, selon ta parole, Yahvé.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Enseigne-moi le bon jugement et la connaissance, car je crois en tes commandements.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Avant d'être affligé, je me suis égaré; mais maintenant j'observe ta parole.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Tu es bon, et tu fais le bien. Apprends-moi tes statuts.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Les orgueilleux m'ont entaché de mensonge. De tout mon cœur, je garderai tes préceptes.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Leur cœur est aussi dur que la graisse, mais je me réjouis de ta loi.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Il est bon pour moi que j'aie été affligé, pour que j'apprenne tes statuts.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
La loi de ta bouche vaut mieux pour moi que des milliers de pièces d'or et d'argent. YODH
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Tes mains m'ont fait et m'ont formé. Donne-moi l'intelligence, afin que j'apprenne tes commandements.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Ceux qui te craignent me verront et se réjouiront, parce que j'ai mis mon espoir dans ta parole.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Yahvé, je sais que tes jugements sont justes, que c'est par fidélité que tu m'as affligé.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
S'il vous plaît, que votre bonté soit pour mon confort, selon ta parole, à ton serviteur.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Que tes tendres compassions viennent à moi, afin que je vive; car ta loi fait mes délices.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Que les orgueilleux soient déçus, car c'est à tort qu'ils m'ont renversé. Je méditerai sur tes préceptes.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Que ceux qui te craignent se tournent vers moi. Ils connaîtront vos statuts.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Que mon cœur soit irréprochable envers tes décrets, pour que je ne sois pas déçu. KAPF
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Mon âme se languit de ton salut. J'espère en ta parole.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Mes yeux se languissent de ta parole. Je dis: « Quand me consoleras-tu? »
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Car je suis devenu comme une outre à vin dans la fumée. Je n'oublie pas vos statuts.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Combien de jours compte ton serviteur? Quand exécuteras-tu le jugement sur ceux qui me persécutent?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Les orgueilleux ont creusé des fosses pour moi, contraire à votre loi.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Tous tes commandements sont fidèles. Ils me persécutent à tort. Aidez-moi!
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Ils m'avaient presque effacé de la terre, mais je n'ai pas abandonné tes préceptes.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Préserve ma vie selon ta bonté, alors j'obéirai aux lois de ta bouche. LAMEDH
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Yahvé, ta parole est fixée dans les cieux pour toujours.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Ta fidélité s'étend à toutes les générations. Tu as établi la terre, et elle demeure.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Tes lois demeurent jusqu'à ce jour, car toutes choses te servent.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Si ta loi n'avait pas fait mes délices, J'aurais péri dans mon affliction.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Je n'oublierai jamais tes préceptes, car avec eux, tu m'as fait revivre.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Je suis à toi. Sauve-moi, car j'ai cherché tes préceptes.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Les méchants m'ont attendu, pour me détruire. Je prendrai en considération vos statuts.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
J'ai vu une limite à toute perfection, mais vos ordres sont illimités. MEM
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Comme j'aime ta loi! C'est ma méditation toute la journée.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Tes commandements me rendent plus sage que mes ennemis, car tes commandements sont toujours avec moi.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
J'ai plus de compréhension que tous mes professeurs, car vos témoignages sont ma méditation.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
que je comprends mieux que les personnes âgées, parce que j'ai gardé tes préceptes.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
J'ai gardé mes pieds de toute mauvaise voie, pour que je puisse observer ta parole.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Je ne me suis pas détourné de tes ordonnances, car tu m'as appris.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Comme tes promesses sont douces à mon goût, plus que du miel dans ma bouche!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Par tes préceptes, j'obtiens la compréhension; c'est pourquoi je déteste toute voie fausse. NUN
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Ta parole est une lampe pour mes pieds, et une lumière pour mon chemin.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
J'ai juré, et je l'ai confirmé, que j'obéirai à tes justes ordonnances.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Je suis très affligé. Ranime-moi, Yahvé, selon ta parole.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Accepte, je t'en prie, les offrandes volontaires de ma bouche. Yahvé, enseigne-moi tes ordonnances.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Mon âme est continuellement dans ma main, mais je n'oublierai pas votre loi.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Les méchants m'ont tendu un piège, mais je ne me suis pas écarté de vos préceptes.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
J'ai pris vos témoignages comme un héritage pour toujours, car ils sont la joie de mon cœur.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
J'ai mis mon cœur à pratiquer tes lois pour toujours, même jusqu'à la fin. SAMEKH
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Je déteste les hommes à double esprit, mais j'aime votre loi.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Tu es ma cachette et mon bouclier. J'espère en ta parole.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Éloignez-vous de moi, méchants, afin que je puisse garder les commandements de mon Dieu.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Soutiens-moi selon ta parole, afin que je vive. Que je n'aie pas honte de mon espérance.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Tenez-moi, et je serai en sécurité, et respectera sans cesse vos statuts.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Tu rejettes tous ceux qui s'écartent de tes statuts, car leur ruse est vaine.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Tu as fait disparaître tous les méchants de la terre comme des scories. C'est pourquoi j'aime vos témoignages.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Ma chair tremble par peur de toi. J'ai peur de vos jugements. AYIN
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
J'ai fait ce qui est juste et équitable. Ne me laissez pas à mes oppresseurs.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Veillez au bien-être de votre serviteur. Ne laisse pas les orgueilleux m'opprimer.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mes yeux défaillent en cherchant ton salut, pour ta parole juste.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Traite ton serviteur selon ta bonté. Apprends-moi tes statuts.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Je suis ton serviteur. Donne-moi l'intelligence, pour que je connaisse vos témoignages.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Il est temps d'agir, Yahvé, car ils violent ta loi.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
C'est pourquoi j'aime tes commandements plus que l'or, oui, plus que de l'or pur.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
C'est pourquoi je considère que tous tes préceptes sont justes. Je déteste toutes les fausses routes. PE
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Vos témoignages sont merveilleux, c'est pourquoi mon âme les garde.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
L'entrée de vos paroles donne de la lumière. Il donne de la compréhension aux simples.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
J'ai ouvert la bouche en grand et j'ai haleté, car je me languissais de tes commandements.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Tournez-vous vers moi, et ayez pitié de moi, comme tu le fais toujours à ceux qui aiment ton nom.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Établis mes pas dans ta parole. Ne laisse pas l'iniquité dominer sur moi.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Délivre-moi de l'oppression de l'homme, alors j'observerai tes préceptes.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Fais briller ton visage sur ton serviteur. Apprends-moi tes statuts.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Des ruisseaux de larmes coulent dans mes yeux, parce qu'ils n'observent pas ta loi. TZADHE
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Tu es juste, Yahvé. Vos jugements sont justes.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Tu as commandé tes statuts avec justice. Ils sont entièrement dignes de confiance.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Mon zèle m'épuise, parce que mes ennemis ignorent vos paroles.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Vos promesses ont été testées de manière approfondie, et ton serviteur les aime.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Je suis petit et méprisé. Je n'oublie pas tes préceptes.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Ta justice est une justice éternelle. Votre loi est la vérité.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
La détresse et l'angoisse se sont emparées de moi. Tes commandements sont mes délices.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Tes témoignages sont justes à jamais. Donne-moi l'intelligence, pour que je puisse vivre. QOPH
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
J'ai appelé de tout mon cœur. Réponds-moi, Yahvé! Je garderai vos statuts.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Je t'ai appelé. Sauve-moi! J'obéirai à tes statuts.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Je me lève avant l'aube et j'appelle à l'aide. Je mets mon espoir dans vos paroles.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Mes yeux restent ouverts pendant les veilles de la nuit, pour que je puisse méditer sur ta parole.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Écoute ma voix, selon ta bonté. Ranime-moi, Yahvé, selon tes ordonnances.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Ils s'approchent, ceux qui suivent la méchanceté. Ils sont loin de votre loi.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Tu es proche, Yahvé. Tous tes commandements sont la vérité.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Je le sais depuis longtemps grâce à vos témoignages, que tu les as fondés pour toujours. RESH
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Considérez ma détresse, et délivrez-moi, car je n'oublie pas ta loi.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Plaidez ma cause, et rachetez-moi! Ranime-moi selon ta promesse.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Le salut est loin des méchants, car ils ne cherchent pas tes statuts.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Grandes sont tes tendres compassions, Yahvé. Ranime-moi selon tes ordonnances.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Mes persécuteurs et mes adversaires sont nombreux. Je ne me suis pas écarté de vos témoignages.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Je regarde les infidèles avec dégoût, parce qu'ils n'observent pas ta parole.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Considérez combien j'aime vos préceptes. Ranime-moi, Yahvé, selon ta bonté.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Toutes vos paroles sont vraies. Chacune de tes justes ordonnances est éternelle. SIN ET SHIN
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Les princes m'ont persécuté sans raison, mais mon cœur est en admiration devant vos mots.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Je me réjouis de ta parole, comme celui qui trouve un grand butin.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Je déteste et abhorre le mensonge. J'aime votre loi.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Sept fois par jour, je te loue, à cause de vos justes ordonnances.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Ceux qui aiment ta loi ont une grande paix. Rien ne les fait trébucher.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
J'ai espéré en ton salut, Yahvé. J'ai appliqué tes commandements.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Mon âme a observé vos témoignages. Je les aime énormément.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
J'ai obéi à tes préceptes et à tes témoignages, car toutes mes voies sont devant toi. TAV
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Que mon cri parvienne jusqu'à toi, Yahvé. Donne-moi l'intelligence selon ta parole.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Que ma supplication vienne devant toi. Délivre-moi selon ta parole.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Que mes lèvres prononcent des louanges, car tu m'enseignes tes statuts.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Que ma langue chante ta parole, car tous tes commandements sont justes.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Que ta main soit prête à m'aider, car j'ai choisi tes préceptes.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Je me suis langui de ton salut, Yahvé. Votre loi est mon plaisir.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Fais vivre mon âme, afin que je te loue. Que vos ordonnances m'aident.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Je me suis égaré comme une brebis égarée. Cherche ton serviteur, car je n'oublie pas tes commandements.

< Masalimo 119 >