< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Autuaat ovat ne, jotka viattomasti elävät, ja jotka Herran laissa vaeltavat.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Autuaat ovat ne, jotka hänen todistuksiansa pitävät, ja kaikesta sydämestä häntä etsivät.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Sillä, jotka hänen teissänsä vaeltavat, ei he tee mitään pahaa.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Sinä olet käskenyt sangen visusti pitää sinun käskys.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
O jospa minun tieni ojennettaisiin pitämään sinun säätyjäs!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Koska minä katson kaikkia sinun käskyjäs, niin en minä tule häpiään.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Minä kiitän sinua oikiasta sydämestä, ettäs opetat minulle vanhurskautes oikeudet.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Sinun säätys minä pidän, älä minua ikänä hylkää.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Kuinka nuorukainen tiensä puhdistais? kuin hän itsensä käyttää sinun sanas jälkeen.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Minä etsin sinua kaikesta sydämestäni: älä salli minun eksyä sinun käskyistäs.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Minä pidän sydämessäni sinun sanas, etten minä rikkoisi sinua vastaan.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Kiitetty ole, sinä Herra: opeta minulle sinun säätyjäs!
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Minä luettelen huulillani kaikki sinun suus oikeudet.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Minä iloitsen sinun todistustes tiellä, niinkuin kaikkinaisesta rikkaudesta.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Minä tutkistelen sinun käskyjäs, ja katselen sinun teitäs.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Minä halajan sinun oikeuttas, ja en unohda sinun sanojas.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Tee hyvästi palvelialles, että minä eläisin ja sinun sanas pitäisin.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Avaa minun silmäni näkemään ihmeitä sinun laistas.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Minä olen vieras maan päällä: älä peitä minulta käskyjäs.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Minun sieluni on muserrettu rikki ikävöitsemisestä, alati sinun oikeutes jälkeen.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Sinä rankaiset ylpiät kirotut, jotka sinun käskyistäs poikkeevat.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Käännä minusta pois pilkka ja ylönkatse; sillä minä pidän sinun todistukses.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Istuvat myös päämiehet ja puhuvat minua vastaan; mutta sinun palvelias tutkistelee sinun säätyjäs.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Sinun todistukses ovat minun iloni, ne ovat minun neuvonantajani.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Minun sieluni tomussa makaa: virvoita minua sanas jälkeen.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Minä luen minun teitäni, ja sinä kuulet minua: opeta minulle sinun säätys.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Anna minun ymmärtää sinun käskyis tie, niin minä puhun sinun ihmeistäs.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Niin minä suren, että sydän sulaa minussa: vahvista minua sinun sanas jälkeen.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Käännä minusta pois väärä tie, ja suo minulle sinun lakis.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Totuuden tien minä olen valinnut, oikeutes olen minä asettanut eteeni.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Minä riipun sinun todistuksissas: Herra, älä salli minun häpiään tulla.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Koskas minun sydämeni vahvistat, niin minä juoksen sinun käskyis tietä myöten.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Opeta minulle, Herra, sinun säätyis tie, että minä sen loppuun asti kätkisin.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Anna minulle ymmärrys, kätkeäkseni sinun lakias, ja pitääkseni sitä koko sydämestäni.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Anna minun käydä sinun käskyis tietä; sillä niihin minä halajan.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Kallista minun sydämeni sinun todistuksiis, ja ei ahneuden puoleen.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Käännä minun silmäni pois katselemasta turhuutta; vaan virvoita minua sinun tiehes.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Anna palvelias lujasti sinun käskys pitää, että minä sinua pelkäisin.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Käännä minusta pois se pilkka, jota minä pelkään; sillä sinun oikeutes ovat suloiset.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Katso, minä pyydän sinun käskyjäs: virvoita minua vanhurskaudellas.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Herra, anna armos minulle tapahtua, autuutes sinun sanas jälkeen,
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Että minä voisin vastata minun pilkkaajiani; sillä minä luotan sinun sanaas.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Älä ota totuuden sanaa peräti pois minun suustani; sillä minä toivon sinun oikeuttas.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Minä pidän alati sinun lakis, aina ja ijankaikkisesti,
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Ja vaellan ilossa, sillä minä etsin sinun käskyjäs,
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Ja puhun sinun todistuksistas kuningasten edessä, ja en häpee,
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Ja iloitsen sinun käskyistäs, joita minä rakastan,
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Ja nostan käsiäni sinun käskyihis, joita minä rakastan, ja puhun sinun säädyistäs.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Muista sanaas sinun palvelialles, jota sinä annoit minun toivoa.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Tämä on minun turvani minun vaivassani, että sinun sanas virvoittaa minun.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Ylpiät irvistelevät minua sangen; en minä sentähden sinun laistas poikkee.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Herra, kuin minä ajattelen, kuinka sinä maailman alusta toiminut olet, niin minä lohdutetaan.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Minä hämmästyin jumalattomain tähden, jotka sinun lakis hylkäävät.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Sinun oikeutes ovat minun veisuni vaellukseni huoneessa.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Herra, minä ajattelen yöllä sinun nimeäs, ja pidän sinun lakis.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Se olis minun tavarani, että minä sinun käskys pitäisin.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Minä olen sanonut: Herra, se on minun perimiseni, että minä pidän sinun sanas.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Minä rukoilen sinun kasvois edessä täydestä sydämestä: ole minulle armollinen sinun sanas jälkeen.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Minä tutkin teitäni, ja käännän jalkani sinun todistustes puoleen.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Minä riennän, ja en viivy, sinun käskyjäs pitämään.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Jumalattomain joukko raatelee minua; mutta en minä unohda sinun lakias.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Puoliyöstä minä nousen sinua kiittämään, sinun vanhurskautes oikeuden tähden.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Minä olen heidän kumppaninsa, jotka sinua pelkäävät ja sinun käskyjäs pitävät,
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Herra! maa on täynnä sinun hyvyyttäs: opeta minulle sinun säätyjäs.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Hyvästi teit sinun palveliaas kohtaan, Herra, sinun sanas jälkeen.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Opeta minulle hyviä tapoja ja taitoa; sillä minä uskon sinun käskys.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Ennenkuin minä nöyryytettiin, eksyin minä; mutta nyt minä pidän sinun sanas.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Sinä olet hyvä ja teet hyvin: opeta minulle sinun säätyjäs.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Ylpiät ajattelevat valheen minun päälleni; mutta minä pidän täydestä sydämestä sinun käskys.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Heidän sydämensä on lihava niinkuin rasva; mutta minä iloitsen sinun laistas.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Se on minulle hyvä, ettäs minun nöyryytit, että minä sinun säätyjäs oppisin.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Sinun suus laki on minulle otollisempi kuin monta tuhatta kappaletta kultaa ja hopiaa.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Sinun kätes ovat minun tehneet ja valmistaneet: anna minulle ymmärrystä oppiakseni sinun käskyjäs.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Jotka sinua pelkäävät, ne minun näkevät ja iloitsevat; sillä minä toivon sinun sanaas.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Herra! minä tiedän sinun tuomios vanhurskaaksi, ja sinä olet minua totuudessa nöyryyttänyt.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Olkoon siis sinun armos minun lohdutukseni, niinkuin sinä palvelialles luvannut olet.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Anna minulle sinun laupiutes tapahtua, että minä eläisin; sillä sinun lakis on minun iloni.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Jospa ylpiät häpiään tulisivat, jotka minua painavat alas valheellansa; mutta minä ajattelen sinun käskyjäs.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Tulkaan ne minun tyköni, jotka sinua pelkäävät, ja sinun todistukses tuntevat.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Olkoon minun sydämeni toimellinen sinun säädyissäs, etten minä häväistäisi.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Minun sieluni ikävöitsee sinun autuuttas: minä toivon sinun sanas päälle.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Minun silmäni hiveltyvät sinun sanas jälkeen, ja sanovat: koskas minua lohdutat?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Sillä minä olen niinkuin nahka savussa: en minä unohda sinun säätyjäs.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Kuinka kauvan sinun palvelias odottaa? koskas tuomitset minun vainoojani?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Ylpiät minulle kuoppia kaivavat, jotka ei ole sinun lakis perään.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Kaikki sinun käskys ovat sula totuus: he valheella minua vaivaavat: auta minua.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
He olisivat juuri lähes minun maan päällä hukuttaneet; mutta en minä sinun käskyjäs hyljännyt.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Virvoita minua sinun armoillas, että minä pitäisin sinun suus todistuksen.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Herra! sinun sanas pysyy ijankaikkisesti taivaissa.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Sinun totuutes pysyy suvusta sukuun: sinä perustit maan, ja se pysyy.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Ne pysyvät tähän päivään asti sinun asetukses jälkeen; sillä kaikki sinua palvelevat.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Ellei sinun lakis olisi ollut minun lohdutukseni, niin minä olisin raadollisuudessani hukkunut.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
En minä ikänä unohda sinun käskyjäs; sillä niillä sinä minua lohdutat.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Sinun minä olen: auta minua! sillä minä etsin sinun käskyjäs.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Jumalattomat minua vartioitsevat hukuttaaksensa; mutta sinun todistuksistas minä otan vaarin.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Kaikista kappaleista minä olen lopun nähnyt; mutta sinun käskys ovat määrättömät.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Kuinka minä rakastan sinun lakias? Joka päivä minä sitä ajattelen.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Sinä teit minun taitavammaksi käskyilläs kuin minun viholliseni ovat; sillä se on minun ijankaikkinen tavarani.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Minä olen oppineempi kuin kaikki minun opettajani; sillä sinun todistukses ovat minun ajatukseni.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Enemmän minä ymmärrän kuin vanhemmat; sillä minä pidän sinun käskys.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Minä estän jalkani kaikista pahoista teistä, että minä sinun sanas pitäisin.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
En minä poikkee sinun oikeudestas; sillä sinä opetat minua.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Sinun sanas ovat minun suulleni makiammat kuin hunaja.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Sinun käskys tekevät minun ymmärtäväiseksi; sentähden minä vihaan kaikkia vääriä teitä.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Sinun sanas on minun jalkaini kynttilä, ja valkeus teilläni.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Minä vannon, ja sen vahvana pidän, että minä sinun vanhurskautes oikeudet pitää tahdon.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Minä olen sangen kovin vaivattu: Herra, virvoita minua sinun sanas perästä.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Olkoon sinulle, Herra, otolliset minun suuni mieluiset uhrit, ja opeta minulle sinun oikeutes.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Minun sieluni on alati minun käsissäni, ja en unohda sinun lakias.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Jumalattomat virittävät minulle paulan; mutta en minä eksy sinun käskyistäs.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Sinun todistukses ovat minun ijankaikkiset perimiseni; sillä ne ovat minun sydämeni ilo.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Minä kallistan minun sydämeni tekemään sinun säätys jälkeen, aina ja ijankaikkisesti.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Minä vihaan viekkaita henkiä, ja rakastan sinun lakias.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Sinä olet minun varjelukseni ja kilpeni: minä toivon sinun sanas päälle.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Poiketkaat minusta, te pahanilkiset; ja minä pidän minun Jumalani käskyt.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Tue minua sanallas, että minä eläisin, ja älä anna minun toivoni häpiään tulla.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Vahvista minua, että minä autetuksi tulisin, niin minä halajan alati sinun säätyjäs.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Sinä tallaat alas kaikki, jotka sinun säädyistäs horjuvat; sillä heidän viettelyksensä on sula valhe.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Sinä heität pois kaikki jumalattomat maan päältä niinkuin loan; sentähden minä rakastan sinun todistuksias.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Minä pelkään sinua, niin että minun ihoni värisee, ja vapisen sinun tuomioitas.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Minä teen oikeuden ja vanhurskauden: älä minua hylkää niille, jotka minulle väkivaltaa tekevät.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Vastaa palvelias edestä, ja lohduta häntä, ettei ylpiät tekisi minulle väkivaltaa.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Minun silmäni hiveltyvät sinun autuutes perään, ja sinun vanhurskautes sanan jälkeen.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Tee palvelias kanssa sinun armos jälkeen, ja opeta minulle sinun säätyjäs.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Sinun palvelias minä olen: anna minulle ymmärrystä, että minä tuntisin sinun todistukses.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Jopa aika on, että Herra siihen jotakin tekis: he ovat sinun lakis särkeneet.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Sentähden minä rakastan sinun käskyjäs, enempi kuin kultaa ja parasta kultaa.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Sentähden minä pidän visusti kaikkia sinun käskyjäs: minä vihaan kaikkia vääriä teitä.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Ihmeelliset ovat sinun todistukses; sentähden minun sieluni ne pitää.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Kuin sinun sanas julistetaan, niin se valistaa ja antaa yksinkertaisille ymmärryksen.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Minä avaan suuni ja huokaan; sillä minä halajan sinun käskys.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Käännä sinuas minun puoleeni, ja ole minulle armollinen, niinkuin sinä olet niille tottunut tekemään, jotka sinun nimeäs rakastavat.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Vahvista minun käymiseni sinun sanassas, ja älä anna väkivallan minua vallita.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Lunasta minua ihmisten väkivallasta, niin minä pidän sinun käskys.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Valista sinun kasvos palvelias päälle, ja opeta minulle sinun säätys.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Minun silmäni vettä vuotavat, niinkuin virta, ettei sinun käskyjäs pidetä.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Herra! sinä olet vanhurskas ja sinun tuomios ovat oikiat.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Sinä olet vanhurskautes todistukset ja totuuden visusti käskenyt.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Minä olen lähes surmakseni kiivannut, että minun viholliseni ovat sinun sanas unohtaneet.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Sinun puhees on sangen koeteltu, ja sinun palvelias sen rakkaana pitää.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Minä olen halpa ja ylönkatsottu, mutta en minä unohda sinun käskyjäs.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Sinun vanhurskautes on ijankaikkinen vanhurskaus, ja sinun lakis on totuus.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Ahdistus ja tuska ovat minun saavuttaneet; mutta minä iloitsen sinun käskyistäs.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Sinun todistustes vanhurskaus pysyy ijankaikkisesti: anna minulle ymmärrys, niin minä elän.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Minä huudan kaikesta sydämestäni: kuule, Herra, minua, että minä sinun säätys pitäisin.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Sinua minä huudan, auta minua, että minä sinun todistukses pitäisin.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Varhain minä ennätän, ja huudan: sinun sanas päälle minä toivon.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Varhain minä herään, tutkistelemaan sinun sanojas.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Kuule minun ääneni sinun armos jälkeen: Herra, virvoita minua sinun oikeutes jälkeen.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Pahanilkiset vainoojat karkaavat minun päälleni, ja ovat kaukana sinun laistas.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Herra, sinä olet läsnä, ja sinun käskys ovat sula totuus.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Mutta minä sen aikaa tiesin, että sinä olet todistukses ijankaikkisesti perustanut.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Katso minun raadollisuuttani, ja pelasta minua; sillä enpä minä unohda sinun lakias.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Toimita minun asiani ja päästä minua: virvoita minua sinun sanas kautta.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Autuus on kaukana jumalattomista, sillä ei he tottele säätyjäs.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Herra, sinun laupiutes on suuri: virvoita minua sinun oikeutes jälkeen.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Minun vainoojaani ja vihollistani on monta; mutta en minä poikkee sinun todistuksistas.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Minä näen ylönkatsojat, ja siihen suutun, ettei he sinun sanaas pidä.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Katso, minä rakastan sinun käskyjäs: Herra, virvoita minua sinun armos jälkeen.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Sinun sanas on alusta totuus ollut: kaikki sinun vanhurskautes oikeudet pysyvät ijankaikkisesti.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Päämiehet vainoovat minua ilman syytä; mutta minun sydämeni pelkää sinun sanojas.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Minä iloitsen sinun puheestas, niinkuin se joka suuren saaliin löytänyt on.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Valhetta minä vihaan ja kauhistun; mutta sinun lakias minä rakastan.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Seitsemästi päivässä minä kiitän sinua sinun vanhurskautes oikeuden tähden.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Suuri rauha on niillä, jotka sinun lakias rakastavat, ja ei he itsiänsä loukkaa.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Herra! minä odotan sinun autuuttas, ja teen sinun käskys.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Minun sieluni pitää sinun todistukses, ja minä rakastan niitä sangen suuresti.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Minä pidän sinun käskys ja todistukses; sillä kaikki minun tieni ovat edessäs.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Herra! anna minun huutoni tulla sinun etees: anna minulle ymmärrystä sinun sanas jälkeen.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Anna minun rukoukseni tulla sinun etees: pelasta minua sinun sanas jälkeen.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Minun huuleni kiittävät, koskas minulle opetat sinun säätys.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Minun kieleni puhuu sinun sanastas; sillä kaikki sinun käskys ovat vanhurskaat.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Olkoon sinun kätes minulle avullinen; sillä minä olen valinnut sinun käskys.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Herra, minä ikävöitsen sinun autuuttas, ja halajan sinun lakias.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Anna minun sieluni elää, että hän sinua kiittäis, ja sinun oikeutes auttakoon minua!
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Minä olen eksyvä niinkuin kadotettu lammas, etsi sinun palveliaas; sillä en minä unohda sinun käskyjäs.

< Masalimo 119 >