< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
[ALEPH] O the blessedness of those perfect in the way, They are walking in the Law of YHWH,
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
O the blessedness of those keeping His testimonies, They seek Him with the whole heart.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Indeed, they have not done iniquity, They have walked in His ways.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
You have commanded us to diligently keep Your precepts,
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
O that my ways were prepared to keep Your statutes,
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Then I am not ashamed In my looking to all Your commands.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
I confess You with uprightness of heart, In my learning the judgments of Your righteousness.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
I keep Your statutes, do not utterly leave me!
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
[BETH] With what does a young man purify his path? To observe—according to Your word.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
I have sought You with all my heart, Do not let me err from Your commands.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
I have hid Your saying in my heart, That I do not sin before You.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Blessed [are] You, O YHWH, teach me Your statutes.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
With my lips I have recounted All the judgments of Your mouth.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
I have rejoiced in the way of Your testimonies, As over all wealth.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
I meditate on Your precepts, And I attentively behold Your paths.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
I delight myself in Your statutes, I do not forget Your word.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
[GIMEL] Confer benefits on Your servant, I live, and I keep Your word.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Uncover my eyes, and I behold wonders out of Your law.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
I [am] a sojourner on earth, Do not hide Your commands from me.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
My soul has broken for desire To Your judgments at all times.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
You have rebuked the cursed proud, Who are erring from Your commands.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Remove reproach and contempt from me, For I have kept Your testimonies.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Princes also sat—they spoke against me, Your servant meditates on Your statutes,
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Your testimonies [are] also my delight, The men of my counsel!
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
[DALETH] My soul has cleaved to the dust, Quicken me according to Your word.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
I have recounted my ways, And You answer me, teach me Your statutes,
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Cause me to understand the way of Your precepts, And I meditate on Your wonders.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
My soul has dropped from affliction, Establish me according to Your word.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Turn aside the way of falsehood from me And favor me with Your law.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
I have chosen the way of faithfulness, I have compared Your judgments,
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
I have adhered to Your testimonies, O YHWH, do not put me to shame.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
I run the way of Your commands, For You enlarge my heart!
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
[HE] Show me, O YHWH, the way of Your statutes, And I keep it—[to] the end.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Cause me to understand, and I keep Your law, And observe it with the whole heart.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Cause me to tread in the path of Your commands, For I have delighted in it.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Incline my heart to Your testimonies, And not to dishonest gain.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Remove my eyes from seeing vanity, Quicken me in Your way.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Establish Your saying to Your servant, That [is] concerning Your fear.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Remove my reproach that I have feared, For Your judgments [are] good.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Behold, I have longed for Your precepts, Quicken me in Your righteousness,
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
[WAW] And Your kindness meets me, O YHWH, Your salvation according to Your saying.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
And I answer him who is reproaching me a word, For I have trusted in Your word.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
And You do not utterly take away The word of truth from my mouth, Because I have hoped for Your judgment.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
And I keep Your law continually, For all time and forever.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
And I habitually walk in a broad place, For I have sought Your precepts.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
And I speak of Your testimonies before kings, And I am not ashamed.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
And I delight myself in Your commands, That I have loved,
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
And I lift up my hands to Your commands, That I have loved, And I meditate on Your statutes!
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
[ZAYIN] Remember the word to Your servant, On which You have caused me to hope.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
This [is] my comfort in my affliction, That Your saying has quickened me.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
The proud have utterly scorned me, I have not turned aside from Your law.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
I remembered Your judgments of old, O YHWH, And I comfort myself.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Horror has seized me, Because of the wicked forsaking Your law.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Your statutes have been songs to me, In the house of my sojournings.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
I have remembered Your Name in the night, O YHWH, And I keep Your law.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
This has been to me, That I have kept Your precepts!
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
[HETH] YHWH [is] my portion; I have said I would keep Your words,
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
I appeased Your face with the whole heart, Favor me according to Your saying.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
I have reckoned my ways, And turn back my feet to Your testimonies.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
I have made haste, And did not delay, to keep Your commands.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Cords of the wicked have surrounded me, I have not forgotten Your law.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
At midnight I rise to give thanks to You, For the judgments of Your righteousness.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
I [am] a companion to all who fear You, And to those keeping Your precepts.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Of Your kindness, O YHWH, the earth is full, Teach me Your statutes!
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
[TETH] You did good with Your servant, O YHWH, According to Your word.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Teach me the goodness of reason and knowledge, For I have believed in Your commands.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Before I am afflicted, I am erring, And now I have kept Your saying.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
You [are] good, and doing good, Teach me Your statutes.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
The proud have forged falsehood against me, I keep Your precepts with the whole heart.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Their heart has been thick as fat, I have delighted in Your law.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
[It is] good for me that I have been afflicted, That I might learn Your statutes.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
The Law of Your mouth [is] better to me Than thousands of gold and silver!
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
[YOD] Your hands made me and establish me, Cause me to understand, and I learn Your commands.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Those fearing You see me and rejoice, Because I have hoped for Your word.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
I have known, O YHWH, That Your judgments [are] righteous, And [in] faithfulness You have afflicted me.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Please let Your kindness be to comfort me, According to Your saying to Your servant.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Your mercies meet me, and I live, For Your law [is] my delight.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
The proud are ashamed, For [with] falsehood they dealt perversely with me. I meditate on Your precepts.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Those fearing You turn back to me, And those knowing Your testimonies.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
My heart is perfect in Your statutes, So that I am not ashamed.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
[KAPH] My soul has been consumed for Your salvation, I have hoped for Your word.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
My eyes have been consumed for Your word, Saying, “When does it comfort me?”
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
For I have been as a bottle in smoke, I have not forgotten Your statutes.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
How many [are] the days of Your servant? When do You execute judgment Against my pursuers?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
The proud have dug pits for me, That [are] not according to Your law.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
All Your commands [are] faithfulness, They have pursued me [with] falsehood, Help me.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
They have almost consumed me on earth, And I have not forsaken Your precepts.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Quicken me according to Your kindness, And I keep the Testimony of Your mouth!
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
[LAMED] For all time, O YHWH, Your word is set up in the heavens.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Your faithfulness from generation to generation, You established earth, and it stands.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
According to Your ordinances They have stood this day, for the whole—Your servants.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Unless Your law [were] my delights, Then had I perished in my affliction.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
I do not forget Your precepts for all time, For You have quickened me by them.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
I [am] Yours, save me, for I have sought Your precepts.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Your wicked waited for me to destroy me, I understand Your testimonies.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
I have seen an end of all perfection, Your command [is] exceedingly broad!
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
[MEM] O how I have loved Your law! It [is] my meditation all the day.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Your command makes me wiser than my enemies, For it [is] before me for all time.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
I have acted wisely above all my teachers. For Your testimonies [are] my (meditation)
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Above elderly—I understand more, For I have kept Your precepts.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
I restrained my feet from every evil path, So that I keep Your word.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
I did not turn aside from Your judgments, For You have directed me.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
How sweet Your saying has been to my palate, Above honey to my mouth.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
I have understanding from Your precepts, Therefore I have hated every false path!
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
[NUN] Your word [is] a lamp to my foot, And a light to my path.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
I have sworn, and I confirm, To keep the judgments of Your righteousness.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
I have been afflicted very much, O YHWH, quicken me, according to Your word.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Please accept [the] free-will offerings of my mouth, O YHWH, And teach me Your judgments.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
My soul [is] in my hand continually, And I have not forgotten Your law.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
The wicked have laid a snare for me, And I did not wander from your precepts.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
I have inherited Your testimonies for all time, For they [are] the joy of my heart.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
I have inclined my heart To do Your statutes, for all time—[to] the end!
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
[SAMEKH] I have hated doubting ones, And I have loved Your law.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
You [are] my hiding place and my shield, I have hoped for Your word.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Turn aside from me, you evildoers, And I keep the commands of my God.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Sustain me according to Your saying, And I live, and You do not put me to shame because of my hope.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Support me, and I am saved, And I look on Your statutes continually.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
You have trodden down All going astray from Your statutes, For their deceit [is] falsehood.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Dross! You have caused to cease All the wicked of the earth; Therefore I have loved Your testimonies.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
My flesh has trembled from Your fear, And I have been afraid from Your judgments!
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
[AYIN] I have done judgment and righteousness, Do not leave me to my oppressors.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Make Your servant sure for good, Do not let the proud oppress me.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
My eyes have been consumed for Your salvation. And for the saying of Your righteousness.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Do with Your servant according to Your kindness. And teach me Your statutes.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
I [am] Your servant—cause me to understand, And I know Your testimonies.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Time for YHWH to work! They have made Your law void.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Therefore I have loved Your commands Above gold—even fine gold.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Therefore all my appointments I have declared wholly right, I have hated every path of falsehood!
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
[PE] Your testimonies [are] wonderful, Therefore my soul has kept them.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
The opening of Your words enlightens, Instructing the simple.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
I have opened my mouth, indeed, I pant, For I have longed for Your commands.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Look to me, and favor me, As customary to those loving Your Name.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Establish my steps by Your saying, And any iniquity does not rule over me.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Ransom me from the oppression of man, And I observe Your precepts,
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Cause Your face to shine on Your servant, And teach me Your statutes.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Streams of waters have come down my eyes, Because they have not kept Your law!
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
[TSADE] You [are] righteous, O YHWH, And Your judgments [are] upright.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
You have appointed Your testimonies, Righteous and exceedingly faithful,
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
My zeal has cut me off, For my adversaries forgot Your words.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Your saying [is] tried exceedingly, And Your servant has loved it.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
I [am] small, and despised, I have not forgotten Your precepts.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Your righteousness [is] righteousness for all time, And Your law [is] truth.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Adversity and distress have found me, Your commands [are] my delights.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
The righteousness of Your testimonies [Is] to cause me to understand, and I live!
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
[QOF] I have called with the whole heart, Answer me, O YHWH, I keep Your statutes,
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
I have called You, save me, And I keep Your testimonies.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
I have gone forward in the dawn, and I cry, I have hoped for Your word.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
My eyes have gone before the watches, To meditate on Your saying.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Hear my voice, according to Your kindness, YHWH, quicken me according to Your judgment.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
My wicked pursuers have been near, They have been far off from Your law.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
You [are] near, O YHWH, And all Your commands [are] truth.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
I have known Your testimonies of old, That You have founded them for all time!
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
[RESH] See my affliction, and deliver me, For I have not forgotten Your law.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Plead my plea, and redeem me, Quicken me according to Your saying.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Salvation [is] far from the wicked, For they have not sought Your statutes.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Your mercies [are] many, O YHWH, Quicken me according to Your judgments.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
My pursuers and adversaries are many, I have not turned aside from Your testimonies.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
I have seen treacherous ones, And grieve myself, Because they have not kept Your saying.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
See, for I have loved Your precepts, YHWH, quicken me according to Your kindness.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
The sum of Your word [is] truth, And every judgment of Your righteousness [is] for all time!
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
[SHIN] Princes have pursued me without cause, And my heart was afraid because of Your words.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
I rejoice concerning Your saying, As one finding abundant spoil.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
I have hated falsehood, indeed I detest [it], I have loved Your law.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Seven [times] in a day I have praised You, Because of the judgments of Your righteousness.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Those loving Your law have abundant peace, And they have no stumbling-block.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
I have waited for Your salvation, O YHWH, And I have done Your commands.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
My soul has kept Your testimonies, And I love them exceedingly.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
I have kept Your precepts and Your testimonies, For all my ways are before You!
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
[TAW] My loud cry comes near before You, O YHWH; Cause me to understand according to Your word.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
My supplication comes in before You, Deliver me according to Your saying.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
My lips utter praise, For You teach me Your statutes.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
My tongue sings of Your saying, For all Your commands [are] righteous.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Your hand is for a help to me, For I have chosen Your commands.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
I have longed for Your salvation, O YHWH, And Your law [is] my delight.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
My soul lives, and it praises You, And Your judgments help me.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
I wandered as a lost sheep, [so] seek Your servant, For I have not forgotten Your precepts!

< Masalimo 119 >