< Masalimo 119 >
1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Salige de, hvis Vandel er fuldkommen, de, som vandrer i HERRENS Lov.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Salige de, der agter paa hans Vidnesbyrd, søger ham af hele deres Hjerte,
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
de, som ikke gør Uret, men vandrer paa hans Veje.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Du har givet dine Befalinger, for at de nøje skal holdes.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
O, maatte jeg vandre med faste Skridt, saa jeg holder dine Vedtægter!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Da skulde jeg ikke blive til Skamme, thi jeg saa hen til alle dine Bud.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Jeg vil takke dig af oprigtigt Hjerte, naar jeg lærer din Retfærds Lovbud.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Jeg vil holde dine Vedtægter, svigt mig dog ikke helt!
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Hvorledes holder en ung sin Vej ren? Ved at holde sig efter dit Ord.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Af hele mit Hjerte søger jeg dig, lad mig ikke fare vild fra dine Bud!
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Jeg gemmer dit Ord i mit Hjerte for ikke at synde imod dig.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Lovet være du, HERRE, lær mig dine Vedtægter!
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Jeg kundgør med mine Læber alle din Munds Lovbud.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Jeg glæder mig over dine Vidnesbyrds Vej, som var det al Verdens Rigdom.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Jeg vil grunde paa dine Befalinger og se til dine Stier.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
I dine Vedtægter har jeg min Lyst, jeg glemmer ikke dit Ord.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Und din Tjener at leve, at jeg kan holde dit Ord.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Oplad mine Øjne, at jeg maa skue de underfulde Ting i din Lov.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Fremmed er jeg paa Jorden, skjul ikke dine Bud for mig!
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Altid hentæres min Sjæl af Længsel efter dine Lovbud.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Du truer de frække; forbandede er de, der viger fra dine Bud.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Vælt Haan og Ringeagt fra mig, thi jeg agter paa dine Vidnesbyrd.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Om Fyrster oplægger Raad imod mig, grunder din Tjener paa dine Vedtægter.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Ja, dine Vidnesbyrd er min Lyst, det er dem, der giver mig Raad.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
I Støvet ligger min Sjæl, hold mig i Live efter dit Ord!
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Mine Veje lagde jeg frem, og du bønhørte mig, dine Vedtægter lære du mig.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Lad mig fatte dine Befalingers Vej og grunde paa dine Undere.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Af Kummer græder min Sjæl, oprejs mig efter dit Ord!
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Lad Løgnens Vej være langt fra mig og skænk mig i Naade din Lov!
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Troskabs Vej har jeg valgt, dine Lovbud attraar jeg.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Jeg hænger ved dine Vidnesbyrd, lad mig ikke beskæmmes, HERRE!
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Jeg vil løbe dine Buds Vej, thi du giver mit Hjerte at aande frit.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Lær mig, HERRE, dine Vedtægters Vej, saa jeg agter derpaa til Enden.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Giv mig Kløgt, saa jeg agter paa din Lov og holder den af hele mit Hjerte.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Før mig ad dine Buds Sti, thi jeg har Lyst til dem.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Bøj mit Hjerte til dine Vidnesbyrd og ej til uredelig Vinding.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Vend mine Øjne bort fra Tant, hold mig i Live ved dit Ord!
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Stadfæst for din Tjener dit Ord, saa jeg lærer at frygte dig.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Hold borte fra mig den Skændsel, jeg frygter, thi dine Lovbud er gode.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Se, dine Befalinger længes jeg efter, hold mig i Live ved din Retfærd!
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Lad din Miskundhed komme over mig, HERRE, din Frelse efter dit Ord,
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
saa jeg har Svar til dem, der spotter mig, thi jeg stoler paa dit Ord.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Tag ikke ganske Sandheds Ord fra min Mund, thi jeg bier paa dine Lovbud.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Jeg vil stadig holde din Lov, ja evigt og altid;
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
jeg vil vandre i aabent Land, thi dine Befalinger ligger mig paa Sinde.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Jeg vil tale om dine Vidnesbyrd for Konger uden at blues;
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
jeg vil fryde mig over dine Bud, som jeg højligen elsker;
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
jeg vil udrække Hænderne mod dine Bud og grunde paa dine Vedtægter.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Kom Ordet til din Tjener i Hu, fordi du har ladet mig haabe.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Det er min Trøst i Nød, at dit Ord har holdt mig i Live.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
De frække haaned mig saare, dog veg jeg ej fra din Lov.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Dine Lovbud fra fordum, HERRE, kom jeg i Hu og fandt Trøst.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Harme greb mig over de gudløse, dem, der slipper din Lov.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Dine Vedtægter blev mig til Sange i min Udlændigheds Hus.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Om Natten kom jeg dit Navn i Hu, HERRE, jeg holdt din Lov.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Det blev min lykkelige Lod: at agte paa dine Befalinger.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Min Del er HERREN, jeg satte mig for at holde dine Ord.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Jeg bønfaldt dig af hele mit Hjerte, vær mig naadig efter dit Ord!
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Jeg overtænkte mine Veje og styred min Fod tilbage til dine Vidnesbyrd.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Jeg hasted og tøved ikke med at holde dine Bud.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
De gudløses Snarer omgav mig, men jeg glemte ikke din Lov.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Jeg staar op ved Midnat og takker dig for dine retfærdige Lovbud.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Jeg er Fælle med alle, der frygter dig og holder dine Befalinger.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Jorden er fuld af din Miskundhed, HERRE, lær mig dine Vedtægter!
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Du gjorde vel mod din Tjener, HERRE, efter dit Ord.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Giv mig Forstand og indsigt, thi jeg tror paa dine Bud.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Før jeg blev ydmyget, for jeg vild, nu holder jeg dit Ord.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
God er du og gør godt, lær mig dine Vedtægter!
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
De frække tilsøler mig med Løgn, men paa dine Bud tager jeg hjerteligt Vare.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Deres Hjerte er dorskt som Fedt, jeg har min Lyst i din Lov.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Det var godt, at jeg blev ydmyget, saa jeg kunde lære dine Vedtægter.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Din Munds Lov er mig mere værd end Guld og Sølv i Dynger.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Dine Hænder skabte og dannede mig, giv mig Indsigt, saa jeg kan lære dine Bud!
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
De, der frygter dig, ser mig og glædes, thi jeg bier paa dit Ord.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
HERRE, jeg ved, at dine Bud er retfærdige, i Trofasthed har du ydmyget mig.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Lad din Miskundhed være min Trøst efter dit Ord til din Tjener!
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Din Barmhjertighed finde mig, at jeg maa leve, thi din Lov er min Lyst.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Lad de frække beskæmmes, thi de gør mig skammelig Uret, jeg grunder paa dine Befalinger.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Lad dem, der frygter dig, vende sig til mig, de, der kender dine Vidnesbyrd.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Lad mit Hjerte være fuldkomment i dine Vedtægter, at jeg ikke skal blive til Skamme.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Efter din Frelse længes min Sjæl, jeg bier paa dit Ord.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Mine Øjne længes efter dit Ord og siger: »Hvornaar mon du trøster mig?«
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Thi jeg er som en Lædersæk i Røg, men dine Vedtægter glemte jeg ikke.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Hvor langt er vel din Tjeners Liv? Naar vil du dømme dem, der forfølger mig?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
De frække grov mig Grave, de, som ej følger din Lov.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Alle dine Bud er trofaste, med Løgn forfølger man mig, o hjælp mig!
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
De har næsten tilintetgjort mig paa Jorden, men dine Befalinger slipper jeg ikke.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Hold mig i Live efter din Miskundhed, at jeg kan holde din Munds Vidnesbyrd.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
HERRE, dit Ord er evigt, staar fast i Himlen.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Din Trofasthed varer fra Slægt til Slægt, du grundfæsted Jorden, og den staar fast.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Dine Lovbud staar fast, de holder dine Tjenere oppe.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Havde din Lov ej været min Lyst, da var jeg omkommet i min Elende.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Aldrig i Evighed glemmer jeg dine Befalinger, thi ved dem holdt du mig i Live.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Din er jeg, frels mig, thi dine Befalinger ligger mig paa Sinde.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
De gudløse lurer paa at lægge mig øde, dine Vidnesbyrd mærker jeg mig.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
For alting saa jeg en Grænse, men saare vidt rækker dit Bud.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Hvor elsker jeg dog din Lov! Hele Dagen grunder jeg paa den.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Dit Bud har gjort mig visere end mine Fjender, thi det er for stedse mit.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Jeg er klogere end alle mine Lærere, thi jeg grunder paa dine Vidnesbyrd.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Jeg har mere Forstand end de gamle; jeg agter paa dine Bud.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Jeg holder min Fod fra hver Vej, som er ond, at jeg kan holde dit Ord.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Fra dine Lovbud veg jeg ikke, thi du underviste mig.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Hvor sødt er dit Ord for min Gane, sødere end Honning for min Mund.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Ved dine Befalinger fik jeg Forstand, saa jeg hader al Løgnens Vej.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Dit Ord er en Lygte for min Fod, et Lys paa min Sti.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Jeg svor en Ed og holdt den: at følge dine retfærdige Lovbud.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Jeg er saare ydmyget, HERRE, hold mig i Live efter dit Ord!
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Lad min Munds frivillige Ofre behage dig, HERRE, og lær mig dine Lovbud!
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Altid gaar jeg med Livet i Hænderne, men jeg glemte ikke din Lov.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
De gudløse lægger Snarer for mig, men fra dine Befalinger for jeg ej vild.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Dine Vidnesbyrd fik jeg til evigt Eje, thi de er mit Hjertes Glæde.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Jeg bøjed mit Hjerte til at holde dine Vedtægter for evigt til Enden.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Jeg hader tvesindet Mand, men jeg elsker din Lov.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Mit Skjul og mit Skjold er du, jeg bier paa dit Ord.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Vig fra mig, I, som gør ondt, jeg vil holde min Guds Bud.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Støt mig efter dit Ord, at jeg maa leve, lad mig ikke beskæmmes i mit Haab!
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Hold mig oppe, at jeg maa frelses og altid have min Lyst i dine Vedtægter!
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Du forkaster alle, der farer vild fra dine Vedtægter, thi de higer efter Løgn.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
For Slagger regner du alle Jordens gudløse, derfor elsker jeg dine Vidnesbyrd.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Af Rædsel for dig gyser mit Kød, og jeg frygter for dine Lovbud.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Ret og Skel har jeg gjort, giv mig ikke hen til dem, der trænger mig!
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Gaa i Borgen for din Tjener, lad ikke de frække trænge mig!
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mine Øjne vansmægter efter din Frelse og efter dit Retfærds Ord.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Gør med din Tjener efter din Miskundhed og lær mig dine Vedtægter!
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Jeg er din Tjener, giv mig Indsigt, at jeg maa kende dine Vidnesbyrd!
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Det er Tid for HERREN at gribe ind, de har krænket din Lov.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Derfor elsker jeg dine Bud fremfor Guld og Skatte.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Derfor følger jeg oprigtigt alle dine Befalinger og hader hver Løgnens Sti.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Underfulde er dine Vidnesbyrd, derfor agted min Sjæl paa dem.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Tydes dine Ord, saa bringer de Lys, de giver enfoldige Indsigt.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Jeg aabned begærligt min Mund, thi min Attraa stod til dine Bud.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Vend dig til mig og vær mig naadig, som Ret er for dem, der elsker dit Navn!
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Lad ved dit Ord mine Skridt blive faste og ingen Uret faa Magten over mig!
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Udløs mig fra Menneskers Vold, at jeg maa holde dine Befalinger!
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Lad dit Ansigt lyse over din Tjener og lær mig dine Vedtægter!
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Vand i Strømme græder mine Øjne, fordi man ej holder din Lov.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Du er retfærdig, HERRE, og retvise er dine Lovbud.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Du slog dine Vidnesbyrd fast ved Retfærd og Troskab saa saare.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Min Nidkærhed har fortæret mig, thi mine Fjender har glemt dine Ord.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Dit Ord er fuldkommen rent, din Tjener elsker det.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Ringe og ussel er jeg, men dine Befalinger glemte jeg ikke.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Din Retfærd er Ret for evigt, din Lov er Sandhed.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Trængsel og Angst har ramt mig, men dine Bud er min Lyst.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Dine Vidnesbyrd er Ret for evigt, giv mig indsigt, at jeg maa leve!
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Jeg raaber af hele mit Hjerte, svar mig, HERRE, jeg agter paa dine Vedtægter.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Jeg raaber til dig, o frels mig, at jeg kan holde dine Vidnesbyrd!
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Aarle raaber jeg til dig om Hjælp og bier paa dine Ord.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Før Nattevagtstimerne vaager mine Øjne for at grunde paa dit Ord.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Hør mig efter din Miskundhed, HERRE, hold mig i Live efter dit Lovbud!
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
De, der skændigt forfølger mig, er mig nær, men de er langt fra din Lov.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Nær er du, o HERRE, og alle dine Bud er Sandhed.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
For længst vandt jeg Indsigt af dine Vidnesbyrd, thi du har grundfæstet dem for evigt.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Se min Elende og fri mig, thi jeg glemte ikke din Lov.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Før min Sag og udløs mig, hold mig i Live efter dit Ord!
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Frelsen er langt fra de gudløse, thi dine Vedtægter ligger dem ikke paa Sinde.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Din Barmhjertighed er stor, o HERRE, hold mig i Live efter dine Lovbud!
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Mange forfølger mig og er mig fjendske, fra dine Vidnesbyrd veg jeg ikke.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Jeg væmmes ved Synet af troløse, der ikke holder dit Ord.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Se til mig, thi jeg elsker dine Befalinger, HERRE, hold mig i Live efter din Miskundhed!
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Summen af dit Ord er Sandhed, og alt dit retfærdige Lovbud varer evigt.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Fyrster forfulgte mig uden Grund, men mit Hjerte frygted dine Ord.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Jeg glæder mig over dit Ord som en, der har gjort et vældigt Bytte.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Jeg hader og afskyr Løgn, din Lov har jeg derimod kær.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Jeg priser dig syv Gange daglig for dine retfærdige Lovbud.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Megen Fred har de, der elsker din Lov, og intet bliver til Anstød for dem.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Jeg haaber paa din Frelse, HERRE, og jeg har holdt dine Bud.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Min Sjæl har holdt dine Vidnesbyrd, jeg har dem saare kære.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Jeg holder dine Befalinger og Vidnesbyrd, thi du kender alle mine Veje.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Lad min Klage naa frem for dit Aasyn, HERRE, giv mig Indsigt efter dit Ord!
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Lad min Bøn komme frem for dit Aasyn, frels mig efter dit Ord!
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Mine Læber skal synge din Pris, thi du lærer mig dine Vedtægter.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Min Tunge skal synge om dit Ord, thi alle dine Bud er Retfærd.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Lad din Haand være mig til Hjælp, thi jeg valgte dine Befalinger.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Jeg længes efter din Frelse, HERRE, og din Lov er min Lyst.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Gid min Sjæl maa leve, at den kan prise dig, og lad dine Lovbud være min Hjælp!
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Farer jeg vild som det tabte Faar, saa opsøg din Tjener, thi jeg glemte ikke dine Bud.