< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Aleph. Blahoslavení ti, kteříž jsou ctného obcování, kteříž chodí v zákoně Hospodinově.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Blahoslavení, kteříž ostříhají svědectví jeho, a kteříž ho celým srdcem hledají.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Nečiní zajisté nepravosti, ale kráčejí po cestách jeho.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Ty jsi přikázal, aby pilně bylo ostříháno rozkazů tvých.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Ó by spraveny byly cesty mé k ostříhání ustanovení tvých.
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Tehdážť nebudu zahanben, když budu patřiti na všecka přikázaní tvá.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Oslavovati tě budu v upřímnosti srdce, když se vyučovati budu právům spravedlnosti tvé.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Ustanovení tvých budu ostříhati s pilností, toliko neopouštěj mne.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Beth. Jakým způsobem očistí mládenec stezku svou? Takovým, aby se choval vedlé slova tvého.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Celým srdcem svým hledám tebe, nedopouštějž mi blouditi od přikázaní tvých.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
V srdci svém skládám řeč tvou, abych nehřešil proti tobě.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Ty chvály hodný Hospodine, vyuč mne ustanovením svým.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Rty svými vypravuji o všech soudech úst tvých.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Z cesty svědectví tvých raduji se více, než z největšího zboží.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
O přikázaních tvých přemyšluji, a patřím na stezky tvé.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
V ustanoveních tvých se kochám, aniž se zapomínám na slovo tvé.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Gimel Tu milost učiň s služebníkem svým, abych, dokudž jsem živ, ostříhal slova tvého.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Otevři oči mé, abych spatřoval divné věci z zákona tvého.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Příchozí jsem na tom světě, neukrývejž přede mnou přikázaní svých.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Umdlévá duše má pro žádost soudů tvých všelikého času.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Vyhlazuješ pyšné, zlořečené, kteříž bloudí od přikázaní tvých.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Odejmi ode mne útržku a potupu, neboť ostříhám svědectví tvých.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Také i knížata se zasazují, a mluví proti mně, služebník pak tvůj přemýšlí o ustanoveních tvých.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Svědectví tvá zajisté jsou mé rozkoše a moji rádcové.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Daleth Přilnula k prachu duše má; obživiž mne podlé slova svého.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Cesty své předložilť jsem, a vyslýchals mne; vyuč mne ustanovením svým.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Cestě rozkazů tvých dej ať vyrozumívám, a ať přemýšlím o divných skutcích tvých.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Rozplývá se zámutkem duše má, očerstviž mne podlé slova svého.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Cestu lživou odvrať ode mne, a zákon svůj z milosti dej mi.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Cestu pravou jsem vyvolil, soudy tvé sobě předkládám.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Svědectví tvých se přídržím, Hospodine, nedejž mi zahanbenu býti.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Cestou rozkazů tvých poběhnu, když ty rozšíříš srdce mé.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
He Vyuč mne, Hospodine, cestě ustanovení svých, kteréž bych ostříhal do konce.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Dej mi ten rozum, ať šetřím zákona tvého, a ať ho ostříhám celým srdcem.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Dej, ať chodím cestou přikázaní tvých; nebo v tom svou rozkoš skládám.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Nakloň srdce mého k svědectvím svým, a ne k lakomství.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Odvrať oči mé, ať nehledí marnosti; na cestě své obživ mne.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Potvrď služebníku svému řeči své, kterýž se oddal k službě tvé.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Odvrať ode mne pohanění, jehož se bojím; nebo soudové tvoji dobří jsou.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Aj, toužím po rozkázaních tvých; dej, ať jsem živ v spravedlnosti tvé.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Vav Ó ať se přiblíží ke mně milosrdenství tvá, Hospodine, a spasení tvé vedlé řeči tvé,
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Tak abych odpovědíti uměl utrhači svému skutkem, že doufání skládám v slovu tvém.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
A nevynímej z úst mých slova nejpravějšího; neboť na soudy tvé očekávám.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
I budu ostříhati zákona tvého ustavičně, od věků až na věky,
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
A bez přestání choditi na širokosti, neboť jsem se dotázal rozkazů tvých.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Nýbrž mluviti budu o svědectvích tvých i před králi, a nebudu se hanbiti.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Nebo rozkoš svou skládám v přikázaních tvých, kteráž jsem zamiloval.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Přičinímť i ruce své k přikázaním tvým, kteráž miluji, a přemýšleti budu o ustanoveních tvých.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Zajin Rozpomeň se na slovo k služebníku svému, kterýmž jsi mne ubezpečil.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Toť jest má útěcha v ssoužení mém, že mne slovo tvé obživuje.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Pyšní mi se velmi posmívají, však od zákona tvého se neuchyluji.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Neboť se rozpomínám na soudy tvé věčné, Hospodine, kterýmiž se potěšuji.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Děsím se nad bezbožnými, kteříž opouštějí zákon tvůj.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Ustanovení tvá jsou mé písničky na místě mého putování.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Rozpomínám se i v noci na jméno tvé, Hospodine, a ostříhám zákona tvého.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Toť mám odtud, abych ostříhal rozkazů tvých.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Cheth Díl můj, řekl jsem, Hospodine, ostříhati výmluvnosti tvé.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Modlívám se milosti tvé v celém srdci: Smiluj se nade mnou podlé slova svého.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Rozvážil jsem na mysli cesty své, a obrátil jsem nohy své k tvým svědectvím.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Pospíchámť a neodkládám ostříhati rozkazů tvých.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Rota bezbožníků zloupila mne, na zákon tvůj se nezapomínám.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
O půlnoci vstávám, abych tě oslavoval v soudech spravedlnosti tvé.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Účastník jsem všech, kteříž se bojí tebe, a těch, kteříž ostříhají přikázaní tvých.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Milosrdenství tvého, Hospodine, plná jest země, ustanovením svým vyuč mne.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Teth Dobrotivě jsi nakládal s služebníkem svým, Hospodine, podlé slova svého.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Pravému soudu a umění vyuč mne, nebo jsem přikázaním tvým uvěřil.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Prvé než jsem snížen byl, bloudil jsem, ale nyní výmluvnosti tvé ostříhám.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Dobrý jsi ty a dobrotivý, vyuč mne ustanovením svým.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Složiliť jsou lež proti mně pyšní, ale já celým srdcem ostříhám přikázaní tvých.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Zbřidlo jako tuk srdce jejich, já zákonem tvým se potěšuji.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
K dobrémuť jest mi to, že jsem pobyl v trápení, abych se naučil ustanovením tvým.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Za lepší sobě pokládám zákon úst tvých, nežli na tisíce zlata a stříbra.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Jod Ruce tvé učinily a sformovaly mne, dej mi ten rozum, abych se naučil přikázaním tvým,
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Tak aby bojící se tebe mne vidouce, radovali se, že na slovo tvé očekávám.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Seznávámť, Hospodine, že jsou spravedliví soudové tvoji, a že jsi mne hodně potrestal.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Nechať jest již zřejmé milosrdenství tvé ku potěšení mému, podlé řeči tvé mluvené služebníku tvému.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Přiďtež na mne slitování tvá, abych živ býti mohl; nebo zákon tvůj rozkoš má jest.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Zahanbeni buďte pyšní, proto že lstivě chtěli mne podvrátiti, já pak přemyšluji o přikázaních tvých.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Obraťtež se ke mně, kteříž se bojí tebe, a kteříž znají svědectví tvá.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Budiž srdce mé upřímé při ustanoveních tvých, tak abych nebyl zahanben.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Kaph Touží duše má po spasení tvém, na slovo tvé očekávám.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Hynou i oči mé žádostí výmluvností tvých, když říkám: Skoro-liž mne potěšíš?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Ačkoli jsem jako nádoba kožená v dymu, na ustanovení tvá však jsem nezapomenul.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Mnoho-liž bude dní služebníka tvého? Skoro-liž soud vykonáš nad těmi, kteříž mi protivenství činí?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Vykopali mi pyšní jámy, kterážto věc není podlé zákona tvého.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Všecka přikázaní tvá jsou pravda; bez příčiny mi se protiví, spomoziž mi.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Téměřť jsou mne již v nic obrátili na zemi, já jsem však neopustil přikázaní tvých.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Podlé milosrdenství svého obživ mne, abych ostříhal svědectví úst tvých.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Lamed Na věky, ó Hospodine, slovo tvé trvánlivé jest v nebesích.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Od národu do pronárodu pravda tvá, utvrdil jsi zemi, a tak stojí.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Vedlé úsudků tvých stojí to vše do dnešního dne, všecko to zajisté jsou služebníci tvoji.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Byť zákon tvůj nebyl mé potěšení, dávno bych byl zahynul v svém trápení.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Na věky se nezapomenu na rozkazy tvé; jimi zajisté obživil jsi mne.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Tvůjť jsem já, zachovávejž mne; nebo přikázaní tvá zpytuji.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Očekávajíť na mne bezbožní, aby mne zahubili, já pak svědectví tvá rozvažuji.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Každé věci dokonalé vidím skončení; rozkaz tvůj jest přeširoký náramně.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Mem Ó jak miluji zákon tvůj, tak že každého dne on jest mé přemyšlování.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Nad nepřátely mé moudřejšího mne činíš přikázaními svými; nebo mám je ustavičně před sebou.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Nade všecky své učitele rozumnější jsem učiněn; nebo svědectví tvá jsou má přemyšlování.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
I nad starce opatrnější jsem, nebo přikázaní tvých ostříhám.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Od každé cesty zlé zdržuji nohy své, abych ostříhal slova tvého.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Od soudů tvých se neodvracuji, proto že ty mne vyučuješ.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Ó jak jsou sladké dásním mým výmluvnosti tvé, nad med ústům mým.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Z přikázaní tvých rozumnosti jsem nabyl, a protož všeliké cesty bludné nenávidím.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Nun Svíce nohám mým jest slovo tvé, a světlo stezce mé.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Přisáhl jsem, což i splním, že chci ostříhati soudů spravedlnosti tvé.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Ztrápenýť jsem přenáramně, Hospodine, obživiž mne vedlé slova svého.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Dobrovolné oběti úst mých, žádám, oblib, Hospodine, a právům svým vyuč mne.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Duše má jest v ustavičném nebezpečenství, a však na zákon tvůj se nezapomínám.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Polékli jsou mi bezbožní osídlo, ale já od rozkazů tvých se neodvracím.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Za dědictví věčné ujal jsem svědectví tvá, neboť jsou radost srdce mého.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Naklonil jsem srdce svého k vykonávání ustanovení tvých ustavičně, až i do konce.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Samech Výmyslků nenávidím, zákon pak tvůj miluji.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Skrýše má a pavéza má ty jsi, na slovo tvé očekávám.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Odstuptež ode mne nešlechetníci, abych ostříhal přikázaní Boha svého.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Zdržujž mne podlé slova svého, tak abych živ byl, a nezahanbuj mne v mém očekávání.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Posiluj mne, abych zachován byl, a patřil k ustanovením tvým ustavičně.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Potlačuješ všecky ty, kteříž odstupují od ustanovení tvých; neboť jest lživá opatrnost jejich.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Jako trůsku odmítáš všecky bezbožníky země, a protož miluji svědectví tvá.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Děsí se strachem před tebou tělo mé; nebo soudů tvých bojím se.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Ajin Èiním soud a spravedlnost, nevydávejž mne mým násilníkům.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Zastup sám služebníka svého k dobrému, tak aby mne pyšní nepotlačili.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Oči mé hynou čekáním na spasení tvé, a na výmluvnost spravedlnosti tvé.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Nalož s služebníkem svým vedlé milosrdenství svého, a ustanovením svým vyuč mne.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Služebník tvůj jsem já, dejž mi rozumnost, abych uměl svědectví tvá.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Èasť jest, abys se přičinil, Hospodine; zrušili zákon tvůj.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Z té příčiny miluji přikázaní tvá více nežli zlato, i to, kteréž jest nejlepší.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
A proto, že všecky rozkazy tvé o všech věcech pravé býti poznávám, všeliké stezky bludné nenávidím.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Pe Předivnáť jsou svědectví tvá, a protož jich ostříhá duše má.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Začátek učení tvého osvěcuje, a vyučuje sprostné rozumnosti.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Ústa svá otvírám, a dychtím, nebo přikázaní tvých jsem žádostiv.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Popatřiž na mne, a smiluj se nade mnou podlé práva těch, kteříž milují jméno tvé.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Kroky mé utvrzuj v slovu svém, a nedej, aby nade mnou panovati měla jaká nepravost.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Vysvoboď mne z nátisků lidských, abych ostříhal rozkazů tvých.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Zasvěť tvář svou nad služebníkem svým, a ustanovením svým vyuč mne.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Potůčkové vod vyplývají z očí mých příčinou těch, kteříž neostříhají zákona tvého.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Tsade Spravedlivý jsi, Hospodine, a upřímý v soudech svých.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Ty jsi vydal spravedlivá svědectví svá, a vší víry hodná.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Až svadnu, tak horlím, že se zapomínají na slovo tvé nepřátelé moji.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Zprubovanáť jest řeč tvá dokonale, tou příčinou ji miluje služebník tvůj.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Maličký a opvržený jsem já, však na rozkazy tvé se nezapomínám.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Spravedlnost tvá jest spravedlnost věčná, a zákon tvůj pravda.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Ssoužení a nátisk mne stihají, přikázaní tvá jsou mé rozkoše.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Spravedlnost svědectví tvých trvá na věky; dej mi z ní rozumnosti nabýti, tak abych živ býti mohl.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Koph Z celého srdce volám, vyslyšiš mne, ó Hospodine, abych ostříhal ustanovení tvých.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
K tobě volám, vysvoboď mne, abych šetřil svědectví tvých.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Předstihám svitání a volám, na tvéť slovo očekávám.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Předstihají oči mé bdění proto, abych přemýšlel o výmluvnostech tvých.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Hlas můj slyš podlé svého milosrdenství, Hospodine, podlé soudů svých obživ mne.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Přibližují se následovníci nešlechetnosti, ti, kteříž se od zákona tvého vzdálili.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Ty blíže jsi, Hospodine; nebo všecka přikázaní tvá jsou pravda.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Jižť to dávno vím o svědectvích tvých, že jsi je stvrdil až na věky.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Reš Popatřiž na mé trápení, a vysvoboď mne; neboť se na zákon tvůj nezapomínám.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Zasaď se o mou při, a ochraň mne; pro řeč svou obživ mne.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Dalekoť jest od bezbožných spasení, nebo nedotazují se na ustanovení tvá.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Slitování tvá mnohá jsou, Hospodine; podlé soudů svých obživ mne.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Jakžkoli jsou mnozí protivníci moji a nepřátelé moji, však od svědectví tvých se neuchyluji.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Viděl jsem ty, kteříž se převráceně měli, velmi to těžce nesa, že řeči tvé neostříhali.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Popatřiž, žeť rozkazy tvé miluji, Hospodine; podlé milosrdenství svého obživ mne.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Nejpřednější věc slova tvého jest pravda, a na věky trvá všeliký úsudek spravedlnosti tvé.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Šin Knížata mi se protiví bez příčiny, však slova tvého děsí se srdce mé.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Já raduji se z řeči tvé tak jako ten, kterýž dochází hojné kořisti.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Falše pak nenávidím, a jí v ohavnosti mám; zákon tvůj miluji.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Sedmkrát za den chválím tě z soudů tvých spravedlivých.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Pokoj mnohý těm, kteříž milují zákon tvůj, a nemají žádné urážky.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Očekávám na spasení tvé, Hospodine, a přikázaní tvá vykonávám.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Ostříhá duše má svědectví tvých, nebo je velice miluji.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Ostříhám rozkazů tvých a svědectví tvých; nebo všecky cesty mé jsou před tebou.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Thav Předstupiž úpění mé před oblíčej tvůj, Hospodine, a podlé slova svého uděl mi rozumnosti.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Vejdiž pokorná prosba má před tvář tvou, a vedlé řeči své vytrhni mne.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
I vynesou rtové moji chválu, když ty mne vyučíš ustanovením svým.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Zpívati bude i jazyk můj slovo tvé, a že všecka přikázaní tvá jsou spravedlnost.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Budiž mi ku pomoci ruka tvá; neboť jsem sobě zvolil přikázaní tvá.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Toužím po spasení tvém, Hospodine, a zákon tvůj jest rozkoš má.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Živa bude duše má, a bude tě chváliti, a soudové tvoji budou mi na pomoc.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Bloudím jako ovce ztracená, hledejž služebníka svého, neboť se na přikázaní tvá nezapomínám.

< Masalimo 119 >