< Masalimo 118 >
1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Alaben al Señor, porque él es bueno; porque su misericordia es inmutable para siempre.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Deja que Israel ahora diga, que su misericordia es inmutable para siempre.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Diga ahora la casa de Aarón, que su misericordia es inmutable para siempre.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Que digan ahora todos los adoradores del Señor, que su misericordia es inmutable para siempre.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Hice mi oración al Señor en mi angustia; y el Señor me dio una respuesta, y me puso en un lugar amplio.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
El Señor está de mi lado; No tendré miedo: ¿qué puede hacerme el hombre?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
El Señor es mi gran ayudante: veré mi deseo contra mis enemigos.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
Es mejor tener fe en el Señor que poner la esperanza en el hombre.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
Es mejor tener fe en el Señor que poner la esperanza en los gobernantes.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Todas las naciones me han rodeado; pero en el nombre del Señor los destruiré.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Ellos están a mi alrededor, sí, todos están sobre mí; pero en el nombre del Señor los destruiré.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Me rodean como las abejas; pero son apagados como un fuego entre espinas; porque en el nombre del Señor los destruiré.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
He sido duramente empujado por ti, para que yo tenga una caída; pero el Señor fue mi ayudador.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
Jehová es mi fortaleza y mi canción; él se ha convertido en mi salvación.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
El sonido de alegría y salvación está en las tiendas de los rectos; la diestra del Señor hace obras de poder.
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
La diestra del Señor se levanta; la diestra del Señor hace obras de poder.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
La vida y no la muerte serán mi parte, y daré la historia de las obras del Señor.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
La mano del Señor a sido dura conmigo; pero él no me ha entregado a la muerte.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Sean las puertas de la justicia abiertas para mí; Entraré y alabaré al Señor.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
Esta es la puerta de la casa del Señor; los trabajadores de la justicia entrarán a través de ella.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
Te daré alabanza, porque me has dado una respuesta, y te has convertido en mi salvación.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
La piedra que los constructores pusieron de un lado se ha convertido en la principal piedra del edificio.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
Esta es la obra del Señor; es una maravilla en nuestros ojos.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
Este es el día que el Señor ha hecho; estaremos llenos de alegría y deleite en ello.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Envía la salvación ahora, oh Señor; Señor, envíanos tu bendición.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Bendición sea sobre el que viene en el nombre del Señor; te damos bendición de la casa del Señor.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
Jehová es Dios, y él nos ha dado luz; que la danza sagrada se ordene con ramas, incluso hasta los cuernos del altar.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Tú eres mi Dios, y yo te alabaré; Dios mío, y daré honor a tu nombre.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Alaben al Señor, porque él es bueno, porque su misericordia es inmutable para siempre.