< Masalimo 118 >
1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Исповедайтеся Господеви, яко благ, яко в век милость Его.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Да речет убо дом Израилев: яко благ, яко в век милость Его.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Да речет убо дом Ааронь: яко благ, яко в век милость Его.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Да рекут убо вси боящиися Господа: яко благ, яко в век милость Его.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
От скорби призвах Господа, и услыша мя в пространство.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
Господь мне помощник, и не убоюся: что сотворит мне человек?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
Господь мне помощник, и аз воззрю на враги моя.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
Благо есть надеятися на Господа, нежели надеятися на человека:
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
благо есть уповати на Господа, нежели уповати на князи.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Вси языцы обыдоша мя, и именем Господним противляхся им:
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
обышедше обыдоша мя, и именем Господним противляхся им:
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
обыдоша мя яко пчелы сот, и разгорешася яко огнь в тернии: и именем Господним противляхся им.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Отриновен превратихся пасти, и Господь прият мя.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
Крепость моя и пение мое Господь, и бысть ми во спасение.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
Глас радости и спасения в селениих праведных: десница Господня сотвори силу.
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
Десница Господня вознесе мя, десница Господня сотвори силу.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
Не умру, но жив буду и повем дела Господня.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
Наказуя наказа мя Господь, смерти же не предаде мя.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Отверзите мне врата правды: вшед в ня, исповемся Господеви.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
Сия врата Господня: праведнии внидут в ня.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
Исповемся Тебе, яко услышал мя еси и был еси мне во спасение.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
Камень, егоже небрегоша зиждущии, сей бысть во главу угла:
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
от Господа бысть сей, и есть дивен во очесех наших.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
Сей день, егоже сотвори Господь, возрадуемся и возвеселимся в онь.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
О, Господи, спаси же: о, Господи, поспеши же.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Благословен грядый во имя Господне: благословихом вы из дому Господня.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
Бог Господь, и явися нам: составите праздник во учащающих до рог олтаревых.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Бог мой еси Ты, и исповемся Тебе: Бог мой еси Ты, и вознесу Тя: исповемся Тебе, яко услышал мя еси и был еси мне во спасение.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Исповедайтеся Господеви, яко благ, яко в век милость Его.