< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Bongani iNkosi, ngoba ilungile, ngoba isihawu sayo simi kuze kube nininini.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Katsho uIsrayeli khathesi ukuthi isihawu sayo simi kuze kube nininini.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Kayitsho indlu kaAroni khathesi ukuthi isihawu sayo simi kuze kube nininini.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Kabatsho khathesi abayesabayo iNkosi ukuthi isihawu sayo simi kuze kube nininini.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Ngisesizini ngabiza iNkosi; iNkosi yangiphendula yangibeka endaweni ebanzi.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
INkosi ingakimi, kangiyikwesaba; umuntu angenzani kimi?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
INkosi ingakimi labangisizayo; ngakho mina ngizabona isiloyiso sami phezu kwabangizondayo.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
Kungcono ukuphephela eNkosini kulokuthembela emuntwini.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
Kungcono ukuphephela eNkosini kulokuthembela kuziphathamandla.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Zonke izizwe zangihanqa; kodwa ebizweni leNkosi ngizaziquma.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Zangihanqa, yebo zangihanqa; kodwa ebizweni leNkosi ngizaziquma.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Zangihanqa njengenyosi, zacitshwa njengomlilo wameva; kodwa ebizweni leNkosi ngizaziquma.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Wangigudlumeza lokugudlumeza ngize ngiwe; kodwa iNkosi yangisiza.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
INkosi ingamandla lengoma yami, isibe lusindiso lwami.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
Ilizwi lentokozo losindiso lisemathenteni abalungileyo; esokunene seNkosi senza ngamandla.
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
Esokunene seNkosi siphakanyisiwe, esokunene seNkosi senza ngamandla.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
Kangiyikufa, kodwa ngizaphila, ngilandise imisebenzi yeNkosi.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
INkosi ingijezisile kabuhlungu, kodwa kayinginikelanga ekufeni.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Ngivulelani amasango okulunga; ngingene ngawo, ngidumise iNkosi.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
Yileli isango leNkosi; abalungileyo bazangena ngalo.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
Ngizakudumisa, ngoba ungiphendule, usube lusindiso lwami.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
Ilitshe abakhi abalalayo seliyinhloko yengonsi.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
Lokhu kwenziwa yiNkosi, kuyamangalisa emehlweni ethu.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
Lolu lusuku iNkosi eyalwenzayo, sizathaba sithokoze kulo.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Sindisa khathesi, Nkosi; ngiyakuncenga, ngiyakuncenga, Nkosi, khathesi unike impumelelo.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Ubusisiwe oza ngebizo leNkosi. Silibusisile sisendlini yeNkosi.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
UNkulunkulu uyiNkosi, osinike ukukhanya. Bopha umnikelo womkhosi ngezibopho kuze kube sempondweni zelathi.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Wena unguNkulunkulu wami, ngizakudumisa; Nkulunkulu wami, ngizakuphakamisa.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Bongani iNkosi, ngoba ilungile; ngoba isihawu sayo simi kuze kube nininini.

< Masalimo 118 >