< Masalimo 118 >
1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Mbongeni uThixo ngoba ulungile; uthando lwakhe lumi laphakade.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
U-Israyeli katsho athi: “Uthando lwakhe lumi laphakade.”
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Kayithi indlu ka-Aroni: “Uthando lwakhe lumi laphakade.”
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Akuthi bonke abamesabayo uThixo bathi: “Uthando lwakhe lumi laphakade.”
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Ngathi ngidabukile ngakhala kuThixo, waphendula ngokungikhulula.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
UThixo ulami, angiyikwesaba. Umuntu angenzani kimi na?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
UThixo ulami; ungumsizi wami. Ngizazinyonkoloza ngegunya izitha zami.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
Kungcono ukuphephela kuThixo kulokuthemba umuntu.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
Kungcono ukuphephela kuThixo kulokuthemba amakhosana.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Zonke izizwe zangihanqa, kodwa ngegama likaThixo ngazichitha.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Zangihanqa inxa zonke kodwa ngegama likaThixo ngazichitha.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Zangiminyezela njengezinyosi kodwa zafa masinyane njengokungunguma komlilo wameva; ngebizo likaThixo ngazichitha.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Ngasunduzelwa emuva ngaphose ngawa, kodwa uThixo wangisiza.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
UThixo ungamandla ami lengoma yami; yena useyikusindiswa kwami.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
Imisindo yentokozo lokunqoba iphuma emathenteni abalungileyo: “Isandla sokunene sikaThixo senzile izinto ezinkulu!
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
Isandla sokunene sikaThixo siphakanyisiwe kakhulu; isandla sokunene sikaThixo senzile izinto ezinkulu!”
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
Angizukufa kodwa ngizaphila, ngizamemezela lokho akwenzileyo uThixo.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
UThixo ungitshayile kakhulu, kodwa kanginikelanga ekufeni.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Ngivulela amasango okulunga; ngizangena ngimbonge uThixo.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
Nanti isango likaThixo okungangena khona abalungileyo.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
Ngizakubonga, ngoba ungiphendulile; usuyinsindiso yami.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
Ilitshe ababelilahlile seliyilona ilitshe lekhoneni;
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
uThixo ukwenzile lokhu; njalo kuyamangalisa emehlweni ethu.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
Leli lilanga alenzileyo uThixo; kasithokoze sijabule ngalo.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Oh Thixo, sisindise; Oh Thixo, siphumelelise.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Ubusisiwe lowo obuya ngebizo likaThixo. Siyakubusisa sisendlini kaThixo.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
UThixo unguNkulunkulu, wenzile ukukhanya kwakhe kwehlela phezu kwethu. Liphethe izingatshana, ngenani edibini lomgido lize liyefika empondweni ze-alithare.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
UnguNkulunkulu wami, ngizakubonga; unguNkulunkulu wami, ngizakuphakamisa.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Mbongeni uThixo ngoba ulungile; uthando lwakhe lumi kuze kube phakade.