< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Mwebaze Mukama, kubanga mulungi; okwagala kwe kubeerera emirembe gyonna.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Kale Isirayiri ayogere nti, “Okwagala kwa Mukama kubeerera emirembe gyonna.”
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
N’ab’ennyumba ya Alooni boogere nti, “Okwagala kwe kubeerera emirembe gyonna.”
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Abo abatya Mukama boogere nti, “Okwagala kwe kubeerera emirembe gyonna.”
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Bwe nnali mu nnaku empitirivu, nakoowoola Mukama, n’annyanukula, n’agimponya.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
Mukama ali ku ludda lwange, siriiko kye ntya. Abantu bayinza kunkolako ki?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
Mukama ali nange, ye anyamba. Abalabe bange nnaabatunuuliranga n’amaaso ag’obuwanguzi.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
Kirungi okwesiga Mukama okusinga okwesiga omuntu.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
Kirungi okuddukira eri Mukama okusinga okwesiga abalangira.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Ensi zonna zanzinda ne zinneebungulula, naye mu linnya lya Mukama naziwangula.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Banneebungulula enjuuyi zonna; naye mu linnya lya Mukama nabawangula.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Bankuŋŋaanirako ne banneebungulula ng’enjuki; naye ne basirikka ng’amaggwa agakutte omuliro; mu linnya lya Mukama nabawangula.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Bannumba n’amaanyi mangi, ne mbulako katono okugwa; naye Mukama n’annyamba.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
Mukama ge maanyi gange, era lwe luyimba lwange, afuuse obulokozi bwange.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
Muwulire ennyimba ez’essanyu ez’obuwanguzi, nga ziyimbirwa mu weema z’abatuukirivu nti, “Omukono gwa Mukama ogwa ddyo gutukoledde ebikulu!
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
Omukono gwa Mukama ogwa ddyo gugulumizibbwa; omukono gwa Mukama ogwa ddyo gutukoledde ebikulu!”
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
Sijja kufa, wabula nzija kuba mulamu, ndyoke ntegeeze ebyo byonna Mukama by’akoze.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
Mukama ambonerezza nnyo, naye tandese kufa.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Munzigulirewo emiryango egy’obutuukirivu, nnyingire, neebaze Mukama.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
Guno gwe mulyango omunene ogwa Mukama, abatuukirivu mmwe banaayingiriranga.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
Nkwebaza kubanga onnyanukudde n’ofuuka obulokozi bwange.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
Ejjinja abazimbi lye baagaana lye lifuuse ejjinja ekkulu ery’oku nsonda.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
Kino Mukama ye yakikola; era ffe tukiraba nga kya kitalo mu maaso gaffe.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
Luno lwe lunaku Mukama lw’akoze; tusanyuke tulujagulizeeko.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Ayi Mukama tukwegayiridde, tulokole, Ayi Mukama tukwegayiridde otuwe obuwanguzi.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Alina omukisa oyo ajja mu linnya lya Mukama. Tubasabidde omukisa nga tuli mu nnyumba ya Mukama.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
Mukama ye Katonda, y’atwakiza omusana. Mukumbire wamu nga mukutte amatabi mu ngalo zammwe n’ekiweebwayo kyammwe kituukire ddala ku mayembe g’ekyoto.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Ggwe Katonda wange, nnaakwebazanga; ggwe Katonda wange, nange nnaakugulumizanga.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Mwebaze Mukama kubanga mulungi, n’okwagala kwe kubeerera emirembe gyonna.

< Masalimo 118 >