< Masalimo 118 >
1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
CELEBRATE il Signore; perciocchè [egli è] buono, Perciocchè la sua benignità [è] in eterno.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Or dica Israele, Che la sua benignità [è] in eterno.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Or dica la casa d'Aaronne, Che la sua benignità [è] in eterno.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Or dicano quelli che temono il Signore, Che la sua benignità [è] in eterno.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Essendo in distretta, io invocai il Signore; E il Signore mi rispose, [e mi mise] al largo.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
Il Signore [è] per me; io non temerò Ciò che mi possa far l'uomo.
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
Il Signore [è] per me, fra quelli che mi soccorrono; E [però] io vedrò [ciò che io desidero] ne' miei nemici.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
Meglio [è] sperar nel Signore, Che confidarsi negli uomini.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
Meglio [è] sperar nel Signore, Che confidarsi ne' principi.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Nazioni d'ogni parte mi avevano intorniato; Nel nome del Signore [è avvenuto] che io le ho sconfitte.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Mi avevano circondato, ed anche accerchiao; Nel Nome del Signore [è avvenuto] che io le ho sconfitte.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Mi avevano intorniato come api; [Ma] sono state spente come fuoco di spine; Nel Nome del Signore [è avvenuto] che io le ho sconfitte.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Tu mi avevi fieramente sospinto, [o nemico], per farmi cadere; Ma il Signore mi ha soccorso.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
Il Signore [è] la mia forza, ed il [mio] cantico; E mi è stato in salute.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
Voce di giubilo e di vittoria [è] ne' tabernacoli de' giusti; La destra del Signore fa prodezze.
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
La destra del Signore è innalzata; La destra del Signore fa prodezze.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
Io non morrò, anzi viverò, E racconterò le opere del Signore.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
Il Signore veramente mi ha gastigato; Ma non mi ha dato alla morte.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Apritemi le porte di giustizia; Io entrerò per esse, [e] celebrerò il Signore.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
Questa [è] la porta del Signore, I giusti entreranno per essa.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
Io ti celebrerò; perciocchè tu mi hai risposto, E mi sei stato in salute.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
La pietra [che] gli edificatori avevano rigettata, E stata posta in capo del cantone.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
Questo è proceduto dal Signore; [Ed] è cosa maravigliosa davanti agli occhi nostri.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
Questo [è] il giorno [che] il Signore ha operato: Festeggiamo, e rallegriamoci in esso.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Deh! Signore, ora salva; Deh! Signore, ora prospera.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Benedetto [sia] colui che viene nel Nome del Signore; Noi vi benediciamo dalla Casa del Signore.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
Il Signore [è] Iddio, e ci ha fatta apparire una chiara luce; Legate con funi [l'ostia del]la solennità Alle corna dell'altare.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Tu [sei] il mio Dio, io ti celebrerò; [Tu sei] il mio Dio, io ti esalterò.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Celebrate il Signore; perciocchè [egli è] buono, Perciocchè la sua benignità [è] in eterno.