< Masalimo 118 >
1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
O give thanks to the LORD, for he is good; For his kindness endureth for ever!
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let Israel now say, His kindness endureth for ever!
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let the house of Aaron now say, His goodness endureth for ever!
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let all who fear the LORD say, His kindness endureth for ever!
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
I called upon the LORD in distress; He heard, and set me in a wide place.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
The LORD is on my side, I will not fear: What can man do to me?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
The LORD is my helper; I shall see my desire upon my enemies.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
It is better to trust in the LORD Than to put confidence in man;
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
It is better to trust in the LORD Than to put confidence in princes.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
All the nations beset me around, But in the name of the LORD I destroyed them.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
They beset me on every side; But in the name of the LORD I destroyed them.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
They beset me around like bees; They were quenched like the fire of thorns, For in the name of the LORD I destroyed them.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Thou didst assail me with violence to bring me down! But the LORD was my support.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
The LORD is my glory and my song; For to him I owe my salvation.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
The voice of joy and salvation is in the habitations of the righteous: “The right hand of the LORD doeth valiantly;
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
The right hand of the LORD is exalted; The right hand of the LORD doeth valiantly.”
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
I shall not die, but live, And declare the deeds of the LORD.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
The LORD hath sorely chastened me, But he hath not given me over to death.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Open to me the gates of righteousness, That I may go in, and praise the LORD!
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
This is the gate of the LORD, Through which the righteous enter.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
I praise thee that thou hast heard me, And hast been my salvation.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
“The stone which the builders rejected Hath become the chief corner-stone.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
This is the LORD'S doing; It is marvellous in our eyes!
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
This is the day which the LORD hath made; Let us rejoice and be glad in it!
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Hear, O LORD! and bless us! Hear, O LORD! and send us prosperity!”
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
“Blessed be he that cometh in the name of the LORD! We bless you from the house of the LORD.”
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
“Jehovah is God, he hath shone upon us: Bind the sacrifice with cords to the horns of the altar!”
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Thou art my God, and I will praise thee; Thou art my God, and I will exalt thee!
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
O give thanks to the LORD, for he is good; For his kindness endureth for ever!