< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Give thanks to YHWH, for he is good, for his loving kindness endures forever.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let Israel now say that his loving kindness endures forever.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let the house of Aaron now say that his loving kindness endures forever.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Now let those who fear YHWH say that his loving kindness endures forever.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Out of my distress, I called on JAH. JAH answered me with freedom.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
YHWH is my helper; I will not fear. What can humans do to me?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
YHWH is my helper; and I will look in triumph on those who hate me.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
It is better to take refuge in YHWH, than to put confidence in man.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
It is better to take refuge in YHWH, than to put confidence in princes.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
All the nations surrounded me, but in the name of YHWH, I cut them off.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
They surrounded me, yes, they surrounded me. In the name of YHWH I indeed cut them off.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
They surrounded me like bees. They blazed like a fire among thorns. In the name of YHWH I cut them off.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
I was pushed hard, to make me fall, but YHWH helped me.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
JAH is my strength and my song, and he has become my salvation.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
The voice of rejoicing and salvation is in the tents of the righteous. "The right hand of YHWH does valiantly.
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
The right hand of YHWH is exalted. The right hand of YHWH does valiantly."
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
I will not die, but live, and declare the works of JAH.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
JAH has punished me severely, but he has not given me over to death.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Open to me the gates of righteousness. I will enter into them and praise JAH.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
This is the gate of YHWH; the righteous will enter into it.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
I will give thanks to you, for you have answered me, and have become my salvation.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
The stone which the builders rejected has become the cornerstone.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
This is YHWH's doing. It is marvelous in our eyes.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
This is the day that YHWH has made. We will rejoice and be glad in it.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Save us now, we beg you, YHWH. YHWH, we beg you, send prosperity now.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Blessed is he who comes in the name of YHWH. We have blessed you out of the house of YHWH.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
YHWH is God, and he has given us light. Bind the sacrifice with cords, even to the horns of the altar.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
You are my God, and I will give thanks to you. You are my God, I will exalt you.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Oh give thanks to YHWH, for he is good, for his loving kindness endures forever.

< Masalimo 118 >