< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Thank the Lord, for he is good! His trustworthy love lasts forever.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let all Israel say, “His trustworthy love lasts forever.”
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let Aaron's descendants say, “His trustworthy love lasts forever.”
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let those who honor the Lord say, “His trustworthy love lasts forever.”
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
I was suffering badly, so I cried out to the Lord for help. He answered me and set me free from my pain.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
The Lord is with me, so I have nothing to fear. No one can harm me.
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
The Lord is with me, he will help me. I will see those who hate me defeated.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
It's better to rely on the Lord than to trust in people.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
It's better to rely on the Lord than to trust in the rich and powerful.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Even though all the heathen nations surrounded me, I defeated them with the help of the Lord.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
They completely surrounded me, but even so I defeated them with the help of the Lord.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Like a swarm of bees they attacked, but their attack died out as quickly as burning thorn twigs. I defeated them with the help of the Lord.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
They tried as hard as they could to kill me, but the Lord helped me.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
The Lord is my strength, and the one I sing about. He is the one who saves me.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
Songs of celebration and victory come from the tents of the faithful. The Lord's powerful hand has done amazing things!
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
The Lord raises his powerful hand in victory! The Lord's powerful hand has done amazing things!
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
I'm not going to die. In fact I'm going to live, and let people know what the Lord has done.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
Even though the Lord punished me severely, he did not let me die.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Open the gates of the faithful for me so I can go in and thank the Lord.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
These are the gates of the Lord where God's faithful people enter.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
I want to thank you for answering me and for being the one who saves me.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
The stone rejected by the builders has turned out to be the chief cornerstone.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
The Lord has done this, and it looks wonderful to us!
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
The Lord made this day happen! We will celebrate and be happy for it!
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Lord, please save us! Lord, please make us successful!
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
May the one who comes in the power of the Lord by blessed! We bless you from the house of the Lord!
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
The Lord is God, and his goodness shines on us. Branches in hand, start the procession up towards the altar.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
You are my God, and I will thank you! You are my God, and I will praise you!
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Thank the Lord, for he is good! His trustworthy love lasts forever!

< Masalimo 118 >