< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Alleluia. Confess to the Lord, for he is good, for his mercy is forever.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let Israel now say: For he is good, for his mercy is forever.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let the house of Aaron now say: For his mercy is forever.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let those who fear the Lord now say: For his mercy is forever.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
In my tribulation, I called upon the Lord. And the Lord heeded me with generosity.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
The Lord is my helper. I will not fear what man can do to me.
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
The Lord is my helper. And I will look down upon my enemies.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
It is good to trust in the Lord, rather than to trust in man.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
It is good to hope in the Lord, rather than to hope in leaders.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
All the nations have surrounded me. And, in the name of the Lord, I have been avenged over them.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Surrounding me, they closed in on me. And, in the name of the Lord, I have been avenged over them.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
They surrounded me like a swarm, and they burned like fire among the thorns. And, in the name of the Lord, I have been avenged over them.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Having been pushed, I was overturned so as to fall. But the Lord took me up.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
The Lord is my strength and my praise. And he has become my salvation.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
A voice of exultation and salvation is in the tabernacles of the just.
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
The right hand of the Lord has wrought virtue. The right hand of the Lord has exalted me. The right hand of the Lord has wrought virtue.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
I will not die, but I will live. And I will declare the works of the Lord.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
When chastising, the Lord chastised me. But he has not delivered me over to death.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Open the gates of justice to me. I will enter them, and I will confess to the Lord.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
This is the gate of the Lord. The just will enter by it.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
I will confess to you because you have heard me. And you have become my salvation.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
The stone which the builders have rejected, this has become the head of the corner.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
By the Lord has this been done, and it is a wonder before our eyes.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
This is the day that the Lord has made. Let us exult and rejoice in it.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
O Lord, grant salvation to me. O Lord, grant good prosperity.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Blessed is he who arrives in the name of the Lord. We have blessed you from the house of the Lord.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
The Lord is God, and he has enlightened us. Establish a solemn day amid a dense crowd, even to the horn of the altar.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
You are my God, and I will confess to you. You are my God, and I will exalt you. I will confess to you, for you have heeded me. And you have become my salvation.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Confess to the Lord, for he is good, for his mercy is forever.

< Masalimo 118 >