< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Alleluia. Give thanks to the Lord; for [he is] good: for his mercy [endures] for ever.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let now the house of Israel say, that [he is] good: for his mercy [endures] for ever.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let now the house of Aaron say, that [he is] good: for his mercy [endures] for ever.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let now all that fear the Lord say, that [he is] good: for his mercy [endures] for ever.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
I called on the Lord out of affliction: and he hearkened to me, [so as to bring me] into a wide place.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
The Lord is my helper; and I will not fear what man shall do to me.
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
The Lord is my helper; and I shall see [my desire] upon mine enemies.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
[It is] better to trust in the Lord than to trust in man.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
[It is] better to hope in the Lord, than to hope in princes.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
All nations compassed me about: but in the name of the Lord I repulsed them.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
They completely compassed me about: but in the name of the Lord I repulsed them.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
They compassed me about as bees [do] a honeycomb, and they burst into flame as fire among thorns: but in the name of the Lord I repulsed them.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
I was thrust, and sorely shaken, that I might fall: but the Lord helped me.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
The Lord is my strength and my song, and is become my salvation.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
The voice of exultation and salvation is in the tabernacles of the righteous: the right hand of the Lord has wrought mightily.
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
The right hand of the Lord has exalted me: the right hand of the Lord has wrought powerfully.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
I shall not die, but live, and recount the works of the Lord.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
The Lord has chastened me sore: but he has not given me up to death.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Open to me the gates of righteousness: I will go into them, and give praise to the Lord.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
This is the gate of the Lord: the righteous shall enter by it.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
I will give thanks to thee; because thou hast heard me, and art become my salvation.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
The stone which the builders rejected, the same is become the head of the corner.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
This has been done of the Lord; and it is wonderful in our eyes.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
This is the day which the Lord has made: let us exult and rejoice in it.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
O Lord, save now: O Lord, send now prosperity.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Blessed is he that comes in the name of the Lord: we have blessed you out of the house of the Lord.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
God is the Lord, and he has shined upon us: celebrate the feast with thick [branches, binding the victims] even to the horns of the altar.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Thou art my God, and I will give thee thanks: thou art my God, and I will exalt thee. I will give thanks to thee, for thou hast heard me, and art become my salvation.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Give thanks to the Lord; for he is good: for his mercy [endures] for ever.

< Masalimo 118 >