< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
бо Він нахилив Своє ухо до мене, і я кли́катиму в свої дні!
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
Болі смерти мене оточи́ли і знайшли мене му́ки шео́лу, нещастя та сму́ток знайшов я! (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
А я в Ім'я́ Господа кличу: „О Господи, ви́зволи ж душу мою!“
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Господь милости́вий та справедливий, і наш Бог милосердний!
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
Пильнує Господь недосві́дчених, — став я нужде́нний, та Він допомо́же мені!
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Вернися, о душе́ моя, до свого відпочи́нку, бо Госпо́дь робить добре тобі,
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
бо від смерти Ти ви́зволив душу мою, від сльози́ — моє око, ногу мою від спотика́ння.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Я ходитиму перед обличчям Господнім на землях живих!
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
Я вірив, коли говорив: „Я сильно пригні́чений!“
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
Я сказав був у по́спіху: Кожна люди́на говорить неправду!“
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Чим я відплачу́ Господе́ві за всі доброді́йства Його на мені?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Я чашу спасі́ння прийму́, і прикли́чу Господнє Ім'я́!
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Прися́ги свої Господе́ві я ви́конаю перед усім наро́дом Його́!
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Дорога́ в очах Господа смерть богобі́йних Його!
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
О Господи, я бо Твій раб, я Твій раб, син Твоєї неві́льниці, — Ти кайда́ни мої розв'яза́в!
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Я жертву подяки Тобі принесу́, і Господнім Ім'я́м буду кли́кати!
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Прися́ги свої Господе́ві я виконаю перед усім наро́дом Його,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
на подві́р'ях Господнього Дому, посеред тебе, о Єрусалиме! Алілу́я!

< Masalimo 116 >