< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Nampenda Yahwe kwa kuwa anasikia sauti yangu na kuomba kwangu kwa ajili ya huruma.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Kwa sababu alinisikiliza, nitamuita yeye ningali ninaishi.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
Kamba za mauti zilinizunguka, na mitego ya kuzimu ilinikabili; niliona dhiki na huzuni. (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Kisha niliita kwa jina la Yahwe: “Tafadhali Yahwe, uiokoe nafsi yangu.”
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Yahwe ni mwenye neema na haki; Mungu wetu ni mwenye huruma.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
Yahwe huwalinda wasio na hila; nilishushwa chini akaniokoa.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Nafsi yangu inaweza kurudi mahali pake pa kupumzika, kwa kuwa Yahwe amekuwa mwema kwangu.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Kwa maana uliokoa uhai wangu dhidi ya kifo, mcho yangu dhidi ya machozi, na miguu yangu dhidi ya kujikwaa.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Nitamtumikia Yahwe katika nchi ya walio hai.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
Nilimwamini yeye, hata niliposema, “nimeteswa sana.”
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
Kwa haraka nilisema, “Watu wote ni waongo.”
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Nimlipeje Yahwe kwa wema wake wote kwangu?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Nitakiinua kikombe cha wokovu, na kuliitia jina la Yahwe.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Nitatimiza viapo vyangu kwa Yahwe katika uwepo wa watu wake wote.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Mauti ya wacha Mungu ina thamani machoni pa Mungu.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Ee Yahwe, hakika, mimi ni mtumishi wako; mimi ni mtumishi wako, mwana wa mjakazi wako; umefungua vifungo vyangu.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Nitakutolea dhabihu ya shukrani na nitaliitia jina la Yahwe.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Nitatimiza viapo vyangu kwa Yahwe katika uwepo wa watu wake wote,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
katika nyua za nyumba ya Yahwe, katikati yako, Yerusalemu. Msifuni Yahwe.

< Masalimo 116 >