< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Ninampenda Bwana kwa maana amesikia sauti yangu; amesikia kilio changu ili anihurumie.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Kwa sababu amenitegea sikio lake, nitamwita siku zote za maisha yangu.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
Kamba za mauti zilinizunguka, maumivu makuu ya kuzimu yalinipata, nikalemewa na taabu na huzuni. (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Ndipo nikaliitia jina la Bwana: “Ee Bwana, niokoe!”
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Bwana ni mwenye neema na haki, Mungu wetu ni mwingi wa huruma.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
Bwana huwalinda wanyenyekevu, nilipokuwa katika shida kubwa, aliniokoa.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Ee nafsi yangu, tulia tena, kwa kuwa Bwana amekuwa mwema kwako.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Kwa kuwa wewe, Ee Bwana, umeniokoa nafsi yangu na mauti, macho yangu kutokana na machozi, miguu yangu kutokana na kujikwaa,
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
ili niweze kutembea mbele za Bwana, katika nchi ya walio hai.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
Niliamini, kwa hiyo nilisema, “Mimi nimeteseka sana.”
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
Katika taabu yangu nilisema, “Wanadamu wote ni waongo.”
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Nimrudishie Bwana nini kwa wema wake wote alionitendea?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Nitakiinua kikombe cha wokovu na kulitangaza jina la Bwana.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Nitazitimiza nadhiri zangu kwa Bwana mbele za watu wake wote.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Kifo cha watakatifu kina thamani machoni pa Bwana.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Ee Bwana, hakika mimi ni mtumishi wako, mimi ni mtumishi wako, mwana wa mjakazi wako; umeniweka huru toka katika minyororo yangu.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Nitakutolea dhabihu ya kukushukuru na kuliita jina la Bwana.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Nitazitimiza nadhiri zangu kwa Bwana mbele za watu wake wote,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
katika nyua za nyumba ya Bwana, katikati yako, ee Yerusalemu. Msifuni Bwana.

< Masalimo 116 >