< Masalimo 116 >
1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Amo a Yahvé, porque escucha mi voz, y mis gritos de piedad.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Porque ha vuelto su oído hacia mí, por lo que lo invocaré mientras viva.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
Las cuerdas de la muerte me rodearon, los dolores del Seol se apoderaron de mí. Encontré problemas y penas. (Sheol )
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Entonces invoqué el nombre de Yahvé: “Yahvé, te lo ruego, libera mi alma”.
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Yahvé es clemente y justo. Sí, nuestro Dios es misericordioso.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
Yahvé preserva a los sencillos. Yo estaba hundido, y él me salvó.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Vuelve a tu descanso, alma mía, porque el Señor ha sido generoso contigo.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Porque has librado mi alma de la muerte, mis ojos de las lágrimas, y mis pies de caer.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Caminaré delante de Yahvé en la tierra de los vivos.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
Yo creí, por eso dije, “Me afligí mucho”.
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
Dije en mi apuro, “Todas las personas son mentirosas”.
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
¿Qué le daré a Yahvé por todos sus beneficios para conmigo?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Tomaré la copa de la salvación e invocaré el nombre de Yahvé.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Pagaré mis votos a Yahvé, sí, en presencia de todo su pueblo.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Preciosa a los ojos de Yahvé es la muerte de sus santos.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Yahvé, en verdad soy tu siervo. Soy tu siervo, el hijo de tu sierva. Me has liberado de mis cadenas.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Te ofreceré el sacrificio de acción de gracias, e invocarán el nombre de Yahvé.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Pagaré mis votos a Yahvé, sí, en presencia de todo su pueblo,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
en los atrios de la casa de Yahvé, en medio de ti, Jerusalén. ¡Alabado sea Yah!