< Masalimo 116 >
1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Amo ao Senhor, porque elle ouviu a minha voz e a minha supplica.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Porque inclinou a mim os seus ouvidos; portanto o invocarei emquanto viver.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
Os cordeis da morte me cercaram, e angustias do inferno se apoderaram de mim: encontrei aperto e tristeza. (Sheol )
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Então invoquei o nome do Senhor, dizendo: Ó Senhor, livra a minha alma.
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Piedoso é o Senhor e justo: o nosso Deus tem misericordia.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
O Senhor guarda aos simplices: fui abatido, mas elle me livrou.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Alma minha, volta para o teu repouso, pois o Senhor te fez bem.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Porque tu, Senhor, livraste a minha alma da morte, os meus olhos das lagrimas, e os meus pés da queda.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Andarei perante a face do Senhor na terra dos viventes.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
Cri, por isso fallei: estive muito afflicto.
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
Dizia na minha pressa: Todos os homens são mentirosos.
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Que darei eu ao Senhor, por todos os beneficios que me tem feito?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Tomarei o calix da salvação, e invocarei o nome do Senhor.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Pagarei os meus votos ao Senhor, agora, na presença de todo o seu povo.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Preciosa é á vista do Senhor a morte dos seus sanctos.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Ó Senhor, devéras sou teu servo: sou teu servo, filho da tua serva; soltaste as minhas ataduras.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Offerecer-te-hei sacrificios de louvor, e invocarei o nome do Senhor.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Pagarei os meus votos ao Senhor, na presença de todo o meu povo.
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Nos atrios da casa do Senhor, no meio de ti, ó Jerusalem. Louvae ao Senhor.