< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Ngiyayithanda iNkosi, ngoba izwile ilizwi lami, ukunxusa kwami.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Ngoba ibeke indlebe yayo kimi, ngakho ngizayibiza ensukwini zami.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
Izibopho zokufa zangihanqa, lenhlungu zesihogo zangibamba; ngathola inhlupheko losizi. (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Ngasengibiza ibizo leNkosi, ngathi: O Nkosi, khulula umphefumulo wami.
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Ilomusa iNkosi, ilungile; ye, uNkulunkulu wethu ulesihawu.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
INkosi iyabalondoloza abathobekileyo; ngehliselwa phansi, yasingisindisa.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Buyela, mphefumulo wami, ekuphumuleni kwakho, ngoba iNkosi ikuphethe ngomusa.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Ngoba ikhulule umphefumulo wami ekufeni, amehlo ami ezinyembezini, unyawo lwami ekuweni.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Ngizahamba phambi kweNkosi emazweni abaphilayo.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
Ngakholwa, ngakho ngikhulumile. Mina ngahlupheka kakhulu.
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
Mina ngathi ekuphangiseni kwami: Wonke umuntu ungumqambimanga.
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Ngizabuyiselani eNkosiningazo zonke inzuzo zayo kimi?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Ngizathatha inkezo yosindiso, ngibize ibizo leNkosi.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Ngizakhokha izifungo zami eNkosini, khathesi phambi kwabantu bayo bonke.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Kuligugu emehlweni eNkosi ukufa kwabangcwele bayo.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Hawu Nkosi, isibili ngiyinceku yakho, ngiyinceku yakho, indodana yencekukazi yakho; uthukulule izibopho zami.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Ngizakuhlabela umhlatshelo wokubonga, ngibize ibizo leNkosi.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Ngizakhokha izifungo zami eNkosini, khathesi phambi kwabantu bayo bonke,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
emagumeni endlu yeNkosi, phakathi kwakho, Jerusalema. Dumisani iNkosi!

< Masalimo 116 >