< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Nalingaka Yawe, pamba te ayokaka mongongo mpe mabondeli na ngai.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Ayokaki ngai; boye nakobelela Ye bomoi na ngai mobimba.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
Minyololo ya kufa ezingelaki ngai, somo ya mboka ya bakufi ekangaki ngai; nakomaki moto ya pasi mpe ya mawa. (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Kasi nabelelaki Kombo ya Yawe: « Yawe, nabondeli Yo, bikisa ngai! »
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Yawe asalaka ngolu mpe azali sembo, Nzambe na biso ayokelaka bato mawa.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
Yawe abatelaka bato oyo bazangi mayele. Nalembaki nzoto, kasi abikisi ngai.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Molimo na ngai, zongela kimia na yo, pamba te Yawe asaleli yo bolamu.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Solo, okangoli ngai na kufa, okawusi mpinzoli na ngai mpe obateli makolo na ngai ete ekweya te.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Nakotambola liboso ya Yawe kati na mokili ya bato ya bomoi.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
Solo, nazalaka na elikya, ezala soki nalobaka: « Nazali moto na pasi makasi. »
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
Kati na mitungisi na ngai, nazalaki komilobela: « Bato nyonso bazali bakosi. »
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Nini nakoki kozongisela Yawe mpo na bolamu na Ye nyonso epai na ngai?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Nakotombola kopo ya elonga mpe nakobelela Kombo ya Yawe.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Nakokokisa bandayi na ngai epai na Yawe na miso ya bato na Ye nyonso.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Kufa ya bayengebene ya Yawe ezali na motuya makasi na miso na Ye.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Yawe, yoka ngai, nazali mosali na Yo. Nazali mosali na Yo, mwana mobali ya mwasi mosali na Yo. Ofungoli minyololo oyo ekangaki ngai.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Nakobonzela Yo mbeka mpo na kozongisa matondi, mpe nakobelela Kombo ya Yawe.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Nakokokisa bandayi na ngai epai na Yawe na miso ya bato na Ye nyonso,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
kati na lopango ya Tempelo ya Yawe; kati na yo, Yelusalemi. Bokumisa Yawe!

< Masalimo 116 >