< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Es mīlu(to Kungu), ka Tas Kungs klausa manu balsi un manu pielūgšanu.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Jo Viņš griež Savu ausi pie manis, tādēļ es Viņu piesaukšu visu mūžu.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
Nāves saites mani bija apņēmušas, un elles bēdas man bija uzgājušas, bēdas un bailes man nāca virsū. (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Bet es piesaucu Tā Kunga vārdu: ak Kungs, izglāb manu dvēseli!
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Tas Kungs ir žēlīgs un taisns, un mūsu Dievs ir sirds žēlīgs.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
Tas Kungs pasargā vientiesīgos; kad es biju bēdās, tad Viņš man palīdzēja.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Esi atkal mierā, mana dvēsele, jo Tas Kungs tev dara labu.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Jo tu manu dvēseli esi izglābis no nāves, manas acis no asarām, manu kāju no slīdēšanas.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Es staigāšu Tā Kunga priekšā dzīvo zemē.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
Es ticu, tāpēc es runāju. Es biju ļoti apbēdināts;
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
Es sacīju savās bailēs: visi cilvēki ir melkuļi.
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Kā es Tam Kungam maksāšu visas labdarīšanas, ko Viņš pie manis darījis?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Es pacelšu to pestīšanas biķeri un piesaukšu Tā Kunga vārdu.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Es maksāšu Tam Kungam savus solījumus visu Viņa ļaužu priekšā.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Viņa svēto nāve ir dārga Tā Kunga acīs.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Ak Kungs, es esmu tiešām Tavs kalps, es esmu Tavs kalps, Tavas kalpones dēls, Tu manas saites esi atraisījis.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Tev es upurēšu pateicības upurus un piesaukšu Tā Kunga vārdu.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Es maksāšu Tam Kungam savus solījumus visu Viņa ļaužu priekšā,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Tā Kunga nama pagalmos, tavā vidū, Jeruzāleme. Alleluja!

< Masalimo 116 >