< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
אהבתי כי-ישמע יהוה-- את-קולי תחנוני
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
כי-הטה אזנו לי ובימי אקרא
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
אפפוני חבלי-מות--ומצרי שאול מצאוני צרה ויגון אמצא (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
ובשם-יהוה אקרא אנה יהוה מלטה נפשי
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
חנון יהוה וצדיק ואלהינו מרחם
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
שמר פתאים יהוה דלתי ולי יהושיע
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
שובי נפשי למנוחיכי כי-יהוה גמל עליכי
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
כי חלצת נפשי ממות את-עיני מן-דמעה את-רגלי מדחי
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
אתהלך לפני יהוה-- בארצות החיים
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
האמנתי כי אדבר אני עניתי מאד
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
אני אמרתי בחפזי כל-האדם כזב
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
מה-אשיב ליהוה-- כל-תגמולוהי עלי
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
כוס-ישועות אשא ובשם יהוה אקרא
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
נדרי ליהוה אשלם נגדה-נא לכל-עמו
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
יקר בעיני יהוה-- המותה לחסידיו
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
אנה יהוה כי-אני עבדך אני-עבדך בן-אמתך פתחת למוסרי
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
לך-אזבח זבח תודה ובשם יהוה אקרא
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
נדרי ליהוה אשלם נגדה-נא לכל-עמו
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
בחצרות בית יהוה-- בתוככי ירושלם הללו-יה

< Masalimo 116 >