< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Ina ƙaunar Ubangiji, gama ya ji muryata; ya ji kukata ta neman jinƙai.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Domin ya juye kunnensa gare ni, zan kira gare shi muddin ina da rai.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
Igiyoyin mutuwa sun shaƙe ni, wahalar kabari sun zo a kaina; na cika da wahala da ɓacin rai. (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Sai na kira ga sunan Ubangiji na ce, “Ya Ubangiji, ka cece ni!”
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Ubangiji mai alheri ne da kuma mai adalci; Allahnmu yana cike da tausayi.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
Ubangiji yana tsare masu tawali’u; sa’ad da nake cikin tsananin bukata, ya cece ni.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Ka kwantar da hankali, ya raina, gama Ubangiji mai alheri ne a gare ka.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Gama kai, ya Ubangiji, ka ceci raina daga mutuwa, idanuna daga hawaye, ƙafafuna daga tuntuɓe,
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
don in iya tafiya a gaban Ubangiji a ƙasar masu rai.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
Na gaskata, saboda haka na ce, “An azabtar da ni ƙwarai.”
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
Kuma cikin rikicewana na ce, “Dukan mutane maƙaryata ne.”
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Yaya zan sāka wa Ubangiji saboda dukan alherinsa gare ni?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Zan daga kwaf na ceto in kuma kira ga sunan Ubangiji.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Zan cika alkawurana ga Ubangiji a gaban dukan mutanensa.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Abu mai daraja a gaban Ubangiji shi ne mutuwar tsarkakansa.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Ya Ubangiji, da gaske ni bawanka ne; ni bawanka ne, ɗan baiwarka; ka’yantar da ni daga sarƙoƙi.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Zan yi hadayar godiya gare ka in kuma kira bisa sunan Ubangiji.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Zan cika alkawurana ga Ubangiji a gaban dukan mutanensa,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
a filayen gidan Ubangiji, a tsakiyarki, ya Urushalima. Yabi Ubangiji.

< Masalimo 116 >