< Masalimo 116 >
1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Alléluia. J’ai aimé, parce que le Seigneur exaucera la voix de ma prière.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Parce qu’il a incliné son oreille vers moi, pendant tous mes jours je l’invoquerai.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
Les douleurs de la mort m’ont environné, et les périls de l’enfer m’ont atteint. (Sheol )
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Et j’ai invoqué le nom du Seigneur.
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Le Seigneur est miséricordieux et juste, et notre Dieu a de la pitié.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
Le Seigneur garde les petits: j’ai été humilié, et il m’a délivré.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Rentre, ô mon âme, en ton repos, parce que le Seigneur a été bon pour toi.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Parce qu’il a arraché mon âme à la mort, mes yeux aux larmes, mes pieds à la chute.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Je plairai au Seigneur dans la région des vivants.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
J’ai cru, c’est pourquoi j’ai parlé; mais j’ai été humilié jusqu’à l’excès.
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
J’ai dit dans mon transport: Tout homme est menteur.
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Que rendrai-je au Seigneur pour tous les biens qu’il m’a faits?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Je prendrai le calice du salut, et j’invoquerai le nom du Seigneur.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Je rendrai mes vœux au Seigneur devant tout son peuple;
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Précieuse est, en présence du Seigneur, la mort de ses saints.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Ô Seigneur, parce que je suis votre serviteur, je suis votre serviteur, et fils de votre servante. Vous avez rompu mes liens;
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
C’est à vous que je sacrifierai une hostie de louange, et j’invoquerai le nom du Seigneur.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Je rendrai mes vœux au Seigneur en présence de tout son peuple,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Dans les parvis de la maison du Seigneur, au milieu de toi, Jérusalem.