< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
I love the LORD, because he hath heard my voice and my supplications.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Because he hath inclined his ear to me, therefore will I call upon him as long as I live.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
The sorrows of death surrounded me, and the pains of hell came upon me: I found trouble and sorrow. (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Then I called upon the name of the LORD; O LORD, I beseech thee, deliver my soul.
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Gracious is the LORD, and righteous; yea, our God is merciful.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
The LORD preserveth the simple: I was brought low, and he helped me.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Return to thy rest, O my soul; for the LORD hath dealt bountifully with thee.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
For thou hast delivered my soul from death, my eyes from tears, and my feet from falling.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
I will walk before the LORD in the land of the living.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
I believed, therefore have I spoken: I was greatly afflicted:
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
I said in my haste, All men are liars.
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
What shall I render to the LORD for all his benefits toward me?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
I will take the cup of salvation, and call upon the name of the LORD.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
I will pay my vows to the LORD now in the presence of all his people.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Precious in the sight of the LORD is the death of his saints.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
O LORD, truly I am thy servant; I am thy servant, the son of thy handmaid: thou hast loosed my bonds.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
I will offer to thee the sacrifice of thanksgiving, and will call upon the name of the LORD.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
I will pay my vows to the LORD now in the presence of all his people,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
In the courts of the LORD’S house, in the midst of thee, O Jerusalem. Praise ye the LORD.

< Masalimo 116 >